-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
12. (a) Kodi nkusintha kotani kuchoka pa njira yanthaŵi zonseyi ya kupereka zilozero ku Malemba Achihebri kumene Yesu anakupanga mu Ulaliki wake wa pa Phiri, ndipo kodi nchifukwa ninji? (b) Kodi tikuphunziranji m’kugwiritsira ntchito kwachisanu ndi chimodzi kwa mawu akuti “Kunanenedwa”?
12 Pamene Yesu poyambirira anagwira mawu kuchokera m’Malemba Achihebri, iye anati: “Kwalembedwa.” (Mateyu 4:4, 7, 10) Koma nthaŵi zisanu ndi imodzi mu Ulaliki wa pa Phiri, iye anayamba yomwe inamveka ngati ndemanga yochokera m’Malemba Achihebri ndi mawu akuti: “Kunanenedwa.” (Mateyu 5:21, 27, 31, 33, 38, 43) Kodi nchifukwa ninji? Chifukwa chakuti iye ankalozera ku Malemba monga momwe anamasulidwira mlingaliro la miyambo ya Afarisi imene inatsutsana ndi malamulo a Mulungu. (Deuteronomo 4:2; Mateyu 15:3) Ichi chamveketsedwa m’kulozera kwa Yesu kwa chisanu ndi chimodzi ndi komalizira uku mumpambowu: “Munamva kuti kunanenedwa, Uzikondana ndi mnansi wako, ndi kumuda mdani wako.” Koma panalibe lamulo la Mose limene linati, ‘Uzida mdani wako.’ Alembi ndi Afarisi ndiwo analinena. Uku kunali kumasulira kwawo Chilamulo kwa kukondana ndi mnansi wako—mnansi wako Wachiyuda, osati wina aliyense.
-
-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
18. (a) Kodi Ayuda anachisintha motani chilamulo chonena za kukonda mnansi wako, koma kodi Yesu analowereramo motani? (b) Kodi ndiliti limene linali yankho la Yesu kwa munthu wachilamulo wina amene anafuna kuika polekezera kugwiritsiridwa ntchito kwa “mnansi”?
18 M’chitsanzo chachisanu ndi chimodzi ndipo chomalizira, Yesu anasonyeza momvekera bwino mmene Chilamulo cha Mose chinafooketsedwera ndi miyambo ya arabi motere: “Munamva kuti kunanenedwa, Uzikondana ndi mnansi wako, ndi kumuda mdani wako: koma Ine ndinena kwa inu, Kondanani nao adani anu, ndi kupempherera iwo akuzunza inu.” (Mateyu 5:43, 44) Chilamulo cha Mose cholembedwa sichinaike polekezera chikondi: “Uzikonda mnansi wako monga udzikonda wekha.” (Levitiko 19:18) Anali Afarisi amene anatsekereza lamulo ili, ndipo m’kupatuka kwawo pa iyo iwo anaika polekezera liwu lakuti “mnansi” kwa anthu omwe anasunga miyamboyo. Zidatero kuti pamene Yesu pambuyo pake anakumbutsa wachilamulo wina za lamulo la ‘kukonda mnansi wanu monga inueni,’ munthuyo m’mawu ake anazemba motere: “Mnansi wanga ndani?” Yesu anamuyankha mwa kufotokoza fanizo la Msamariya wachifundo—dzipangeni nokha mnansi kwa okufunani.—Luka 10:25-37.
-