Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Tizichita Zinthu Mogwirizana ndi Pemphero la Ambuye—Gawo 1
    Nsanja ya Olonda—2015 | June 15
    • “ATATE WATHU WAKUMWAMBA”

      4. (a) Kodi mawu akuti “Atate wathu” akutikumbutsa za chiyani? (b) N’chifukwa chiyani tinganene kuti Yehova ndi “Atate” wa anthu amene akuyembekezera kudzakhala padziko lapansi?

      4 Yesu anayamba pempheroli ndi mawu akuti “Atate wathu” osati “Atate wanga.” Zimenezi zikutikumbutsa kuti tili m’gulu la abale ambiri omwe amakondana. (1 Pet. 2:17) Umenewutu ndi mwayi waukulu kwambiri. Akhristu ena asankhidwa ndi Mulungu kuti akhale ana ake ndiponso kuti apite kumwamba. Iwo ndi oyenereradi kunena kuti Yehova ndi “Atate” wawo. (Aroma 8:15-17) Koma Akhristu amene akuyembekezera kudzakhala padzikoli anganenenso kuti Yehova ndi “Atate” wawo. Tikutero chifukwa chakuti Yehova ndi amene anawapatsa moyo ndipo amawapatsanso zinthu zonse zofunika. M’tsogolomu, iwonso adzakhala ana enieni a Mulungu. Izi zidzachitika akadzakhala angwiro komanso akadzadutsa bwinobwino mayesero omaliza.—Aroma 8:21; Chiv. 20:7, 8.

  • Tizichita Zinthu Mogwirizana ndi Pemphero la Ambuye—Gawo 1
    Nsanja ya Olonda—2015 | June 15
    • “DZINA LANU LIYERETSEDWE”

      7. Kodi ifeyo tili ndi mwayi uti, nanga tiyenera kuchita chiyani?

      7 Ifeyo tili ndi mwayi wodziwa dzina la Mulungu komanso wokhala “anthu odziwika ndi dzina lake.” (Mac. 15:14; Yes. 43:10) Timapempha Yehova kuti dzina lake liyeretsedwe. Koma tiyenera kumupemphanso kuti azitithandiza kupewa chilichonse chimene chinganyozetse dzinalo. Sitifuna kufanana ndi anthu ena a m’nthawi ya atumwi amene zochita zawo zinkasemphana ndi zimene ankalalikira. Mtumwi Paulo anauza anthuwo kuti: “Dzina la Mulungu likunyozedwa pakati pa anthu amitundu chifukwa cha inu.”—Aroma 2:21-24.

      8, 9. Perekani chitsanzo chosonyeza kuti Yehova amadalitsa anthu amene amafuna kuti dzina lake liyeretsedwe.

      8 Timafunitsitsa kuchita zinthu zimene zingalemekeze dzina la Mulungu. Mlongo wina wa ku Norway anavutika kwambiri mwamuna wake atamwalira. Anamusiya ndi mwana wazaka ziwiri ndipo mlongoyo anati: “Nthawi imeneyi inali yovuta kwambiri. Ndinkapemphera tsiku lililonse mwinanso ola lililonse kuti Yehova azindikhazika mtima m’malo. Sindinkafuna kuti Satana azitonza Yehova chifukwa choti ndachita zosayenera. Ndinkafuna kulemekeza dzina la Yehova ndiponso kuthandiza mwana wanga kuti adzakumane ndi bambo ake m’Paradaiso.”—Miy. 27:11.

      9 Yehova anayankha pemphero la mlongoyu. Popeza iye ankakonda kucheza ndi abale ndi alongo, iwo ankamulimbikitsa kwambiri. Patapita zaka 5, anakwatiwa ndi mkulu. Panopa mwana wake uja ali ndi zaka 20 ndipo anabatizidwa. Mlongoyu anati: “Ndikusangalala kwambiri kuti mwamuna wanga watsopanoyu wandithandiza kulera bwino mwanayu.”

      10. N’chiyani chiyenera kuchitika kuti dzina la Mulungu liyeretsedwe?

      10 N’chiyani chiyenera kuchitika kuti dzina la Mulungu liyeretsedwe? Yehova ayenera kuchotsa aliyense amene amakana ulamuliro wake. (Werengani Ezekieli 38:22, 23.) Kenako anthu onse adzathandizidwa kuti akhale angwiro. Timalakalaka kwambiri nthawi imene aliyense adzaganiza, kulankhula komanso kuchita zinthu zolemekeza dzina la Mulungu. Pamapeto pake, Atate wathu wakumwamba adzakhala “zinthu zonse kwa aliyense.”—1 Akor. 15:28.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena