Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Mukufunitsitsa Kukhala Wolemera Mwauzimu?
    Galamukani!—2007 | June
    • Kodi Mukufunitsitsa Kukhala Wolemera Mwauzimu?

      KUTI munthu akhale wolemera pamafunika khama ndi kudzimana. N’chimodzimodzinso ndi kulemera mwauzimu. Yesu anasonyeza zimenezi pamene anati: “Kundikani chuma chanu kumwamba.” (Mateyo 6:20) Chuma chauzimu sichimangobwera chokha. Monga mmene munthu sangakhalire ndi chuma chambiri chifukwa chongokhala ndi akaunti kubanki, munthu sangalemere mwauzimu chifukwa chongokhala ndi chipembedzo. Kuti munthu akhale paubwenzi wabwino ndi Mulungu, akonde zinthu zauzimu, ndiponso akhale ndi makhalidwe abwino, pamafunika nthawi, khama, kudzimana ndi kuikirapo mtima.—Miyambo 2:1-6.

  • Kodi Mukufunitsitsa Kukhala Wolemera Mwauzimu?
    Galamukani!—2007 | June
    • Phindu Losaneneka

      Mosiyana ndi chuma cha padzikoli chimene mbala zingabe, chuma chauzimu n’chokhalitsa. (Miyambo 23:4, 5; Mateyo 6:20) Komabe, n’zovuta kunena kuti munthu wafika pati mwauzimu. Tingathe kudziwa kuchuluka kwa chuma chimene munthu ali nacho, koma n’zovuta kudziwa kuti munthu ali ndi chikondi, chisangalalo, kapena chikhulupiriro chotani. Koma phindu la chuma chauzimu ndi losaneneka. Ponena za ophunzira ake amene anasiya zinthu zowathandiza pamoyo monga nyumba ndi minda kuti achite zinthu zauzimu, Yesu anati: “Ndithu ndikukuuzani amuna inu, Palibe amene anasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena amayi, kapena atate, kapena ana, kapena minda, chifukwa cha ine, ndi chifukwa cha uthenga wabwino, amene tsopano lino sadzapeza zochuluka kuwirikiza nthawi 100 m’nthawi ino, nyumba ndi abale ndi alongo ndi amayi ndi ana ndi minda, limodzi ndi mazunzo, ndipo m’dongosolo la zinthu limene likubweralo, moyo wosatha.”—Maliko 10:29, 30.

      Pakati pa Mulungu ndi chuma, kodi n’chiyani chidzakhala patsogolo m’moyo wanu?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena