-
Anawakonzekeretsa Kuti Azilalikira Ngakhale Pamene AkuzunzidwaYesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
-
-
Ngakhale kuti otsatira a Yesu ankayembekezera kukumana ndi mavuto oopsa, iye anawalonjeza kuti: “Akakuperekani kumeneko, musade nkhawa za mmene mukalankhulire kapena zimene mukanene. Mudzapatsidwa nthawi yomweyo zoti mulankhule, pakuti wolankhula simudzakhala inu panokha, koma mzimu wa Atate wanu udzalankhula kudzera mwa inu.” Yesu ananenanso kuti: “Munthu adzapereka m’bale wake ku imfa, ndipo bambo adzapereka mwana wake. Ana adzaukira makolo awo ndipo adzawaphetsa. Anthu onse adzadana nanu chifukwa cha dzina langa, koma yekhayo amene adzapirire mpaka pa mapeto ndi amene adzapulumuke.”—Mateyu 10:19-22.
-
-
Anawakonzekeretsa Kuti Azilalikira Ngakhale Pamene AkuzunzidwaYesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
-
-
Kunena zoona Yesu anachenjeza, kulimbikitsa komanso kupereka malangizo abwino kwambiri kwa atumwi ake 12. Malangizo amene Yesu anapereka nthawi imeneyi anali othandizanso kwa anthu amene anali kudzagwira ntchito yolalikirayi Yesu atafa komanso ataukitsidwa. Tikutero chifukwa Yesu anauza ophunzira ake kuti “anthu onse adzadana nanu” osati anthu okhawo amene atumwiwa ankawalalikira. Ndipotu Baibulo silifotokoza zoti pa nthawi imene atumwiwa ankalalikira ku Galileya anthu anawatengera kwa mabwanamkubwa ndi mafumu kapena kuti anaperekedwa ndi achibale awo kuti aphedwe.
Choncho, n’zoonekeratu kuti pamene Yesu ankapereka malangizo amenewa kwa atumwi ake ankanena zimene zidzachitike m’tsogolo. Kumbukiraninso kuti anauza ophunzira ake kuti sadzamaliza kuzungulira mizinda yonse akugwira ntchito yolalikirayi “Mwana wa munthu asanafike.” Ponena mawu amenewa Yesu ankatanthauza kuti ophunzira ake sadzamaliza kulalikira za Ufumu wa Mulungu, Yesu Khristu yemwe ndi Mfumu asanabwere monga woweruza.
-