-
Mboni Zachikristu Zokhala ndi Unzika WakumwambaNsanja ya Olonda—1995 | July 1
-
-
2. Kodi ndi chinthu chatsopano chiti chimene Yohane Mbatizi analengeza kuti Yesu adzachita, ndipo kodi chinthu chatsopanocho chinali chokhudza chiyani?
2 Pamene Yohane Mbatizi anali kukonzera njira Yesu, analengeza kuti Yesu adzachita chinthu china chatsopano. Cholembedwacho chimati: “[Yohane] analalikira, kuti, Wondipambana ine mphamvu akudza pambuyo panga, sindiyenera kuŵerama kumasula lamba la nsapato zake ine. Ndakubatizani inu ndi madzi; koma iye adzakubatizani ndi mzimu woyera.” (Marko 1:7, 8) Nthaŵiyo isanafike, palibe aliyense amene anabatizidwa ndi mzimu woyera. Kameneka kanali kakonzedwe katsopano kophatikizapo mzimu woyera, ndipo kanali kokhudza chifuno cha Yehova chimene chinali pafupi kuvumbulidwa cha kukonzekeretsa anthu ulamuliro wakumwamba.
-
-
Mboni Zachikristu Zokhala ndi Unzika WakumwambaNsanja ya Olonda—1995 | July 1
-
-
5. Kodi ndiliti pamene ophunzira okhulupirika anabatizidwa ndi mzimu woyera, ndipo ndi kugwira ntchito kotani kwa mzimu woyera kumene kunachitika panthaŵi imodzimodziyo?
5 Pamene Yesu analankhula kwa Nikodemo, mzimu woyera unali utadza kale pa Yesu, ukumamdzoza kaamba ka ufumu wake wamtsogolo mu Ufumu wa Mulungu, ndipo Mulungu anavomereza poyera kuti Yesu anali Mwana Wake. (Mateyu 3:16, 17) Yehova anabala ana ena auzimu pa Pentekoste wa 33 C.E. Ophunzira okhulupirika amene anasokhana m’chipinda chapamwamba mu Yerusalemu anabatizidwa ndi mzimu woyera. Panthaŵi imodzimodzi, anabadwa mwatsopano mwa mzimu woyera kukhala ana auzimu a Mulungu. (Machitidwe 2:2-4, 38; Aroma 8:15) Ndiponso, iwo anadzozedwa ndi mzimu woyera kaamba ka choloŵa chakumwamba chamtsogolo, ndipo anasindikizidwa chizindikiro choyambirira cha mzimu woyera monga chikole chotsimikizira chiyembekezo chakumwamba chimenecho.—2 Akorinto 1:21, 22.
-