Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kuwoneratu Ulemerero wa Ufumu wa Kristu
    Nsanja ya Olonda—1988 | January 1
    • YESU waima panjira kuyenda ku Kaisareya wa Filipi, ndipo iye akuphunzitsa khamu limodzi ndi atumwi ake. Iye akupanga chilengezo chochititsa mantha ichi kwa iwo: “Indetu ndinena kwa inu, kuti alipo ena a iwo aima pano sadzalawa ndithu imfa, kufikira adzawona Mwana wa munthu atadza mu ufumu wake.”

      ‘Kodi nchiyani chimene Yesu akanatanthauza?’ ophunzirawo ayenera kudabwa. Chifupifupi mlungu umodzi pambuyo pake, Yesu akutenga Petro, Yakobo, ndi Yohane limodzi naye nakwera phiri lalitali. Mwinamwake uli usiku, popeza ophunzirawo ali ndi tulo. Pamene Yesu ali kupemphera, iye asandulika pamaso pawo. Nkhope yake iyamba kuwala monga dzuŵa, ndi zovala zake ziyera mbu monga ngati kuwala.

  • Kuwoneratu Ulemerero wa Ufumu wa Kristu
    Nsanja ya Olonda—1988 | January 1
    • Ndi olimbikitsa chotani nanga mmene masomphenya amenewa atsimikizira kukhala, ponse paŵiri kwa Yesu ndi kwa ophunzira! Masomphenyawo ali, monga momwe kunaliri, kuwoneratu za ulemerero wa Ufumu wa Kristu. Ophunzirawo awona, m’chenicheni, “Mwana wa munthu akudza mu ufumu wake,” monga mmene Yesu analonjezera mlungu woyambirirawo. Pambuyo pa imfa ya Yesu, Petro analemba ponena za kukhala ‘mboni zowona ndi maso ukulu wa Kristu pokhala pamodzi ndi iye m’phiri lopatulika lija.’

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena