-
Nkhani ya Mwana WotaikaNsanja ya Olonda—1989 | February 1
-
-
“Munthu wina,” Yesu akuyamba tero, “anali ndi ana amuna aŵiri. Ndipo wam’ng’onoyo anati kwa atate wake, ‘Atate, ndigawirenitu zanga za pa chuma chanu.’ Ndipo [atateyo] anagawira za moyo wake.” Kodi nchiyani chimene wam’ng’onoyo akuchita ndi zimene walandira?
-
-
Nkhani ya Mwana WotaikaNsanja ya Olonda—1989 | February 1
-
-
Pano pali chinachake choyenera kulingalira: Ngati atate wake anamtembenukira iye ndi kufuula mwaukali pa iye pamene iye anachoka panyumba, mwana wamwamunayo mwachidziŵikire sakanakhoza kukhala wa malingaliro amodzi chotero ponena za chimene iye akachita. Iye akanagamulapo kubwerera ndi kuyesera kupeza ntchito kwinakwake m’dziko la kumudzi kwawo kotero kuti sakanakhoza kuyang’anizana ndi atate wake. Ngakhale kuli tero, palibe ganizo lirilonse loterolo linaloŵa m’malingaliro ake. Kumudzi ndi kumene iye anafuna kukhala!
-