Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Anapemphera Pamene Anali ndi Chisoni Kwambiri
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
    • Yesu ankada nkhawa kwambiri kuti akaphedwa ngati chigawenga zichititsa kuti anthu anyoze dzina la Atate wake. Yehova anamva zimene Mwana wake ankamupempha moti anamutumizira mngelo kuti amulimbikitse. Komabe Yesu sanasiye kuchonderera Atate wake ndipo anapitiriza “kupemphera ndi mtima wonse.” Pa nthawiyi Yesu anavutika maganizo kwambiri chifukwa chodziwa udindo waukulu womwe anali nawo. Ngati akanalephera kupilira akanataya mwayi wodzakhala ndi moyo mpaka kalekale komanso anthu amene ankamukhulupirira sakanakhala ndi chiyembekezo chodzapeza moyo wosatha. Yesu anavutika kwambiri moti “thukuta lake linaoneka ngati madontho amagazi amene akugwera pansi.”—Luka 22:44.

  • Anapemphera Pamene Anali ndi Chisoni Kwambiri
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
    • THUKUTA LA YESU LINAONEKA NGATI MADONTHO A MAGAZI

      Luka yemwe anali dokotala sanafotokoze bwinobwino zimene zinachitika kuti thukuta la Yesu likhale “ngati madontho amagazi.” (Luka 22:44) N’kutheka kuti Luka ankayerekezera thukuta la Yesu ndi magazi amene akutuluka pabala. Zimene dokotala wina dzina lake William D. Edwards (The Journal of the American Medical Association) analemba zingatithandize kudziwa zimene zinachitika kuti thukuta la Yesu likhale ngati madontho a magazi. Dokotala ameneyu ananena kuti: “Ngakhale kuti sizichitikachitika kuti munthu atulutse thukuta losakanikirana ndi magazi . . . koma nthawi zina zimachitika ngati munthu wavutika kwambiri maganizo. . . . Mitsempha imene inalumikizana ndi tiziwalo timene timatulutsa thukuta ikaphulika, magazi amalowelera m’tiziwaloto ndipo zimenezi zimachititsa kuti munthu azituluka thukuta losakanikirana ndi magazi.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena