-
Anapemphera Pamene Anali ndi Chisoni KwambiriYesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
-
-
Yesu ankada nkhawa kwambiri kuti akaphedwa ngati chigawenga zichititsa kuti anthu anyoze dzina la Atate wake. Yehova anamva zimene Mwana wake ankamupempha moti anamutumizira mngelo kuti amulimbikitse. Komabe Yesu sanasiye kuchonderera Atate wake ndipo anapitiriza “kupemphera ndi mtima wonse.” Pa nthawiyi Yesu anavutika maganizo kwambiri chifukwa chodziwa udindo waukulu womwe anali nawo. Ngati akanalephera kupilira akanataya mwayi wodzakhala ndi moyo mpaka kalekale komanso anthu amene ankamukhulupirira sakanakhala ndi chiyembekezo chodzapeza moyo wosatha. Yesu anavutika kwambiri moti “thukuta lake linaoneka ngati madontho amagazi amene akugwera pansi.”—Luka 22:44.
-