-
Kodi Tiyenera Kupemphera Motani kwa Mulungu?Nsanja ya Olonda—1996 | July 15
-
-
PAMENE wophunzira anapempha malangizo onena za pemphero, Yesu sanakane kumpatsa. Malinga ndi Luka 11:2-4, iye anayankha kuti: “Mmene mupemphera nenani, Atate, dzina lanu liyeretsedwe; ufumu wanu udze; tipatseni ife tsiku ndi tsiku chakudya cha patsiku. Ndipo mutikhululukire ife machimo athu; pakuti ifenso tikhululukira munthu yense wa mangawa athu. Ndipo musatitengere ife kokatiyesa.” Limeneli ambiri amalidziŵa kukhala Pemphero la Ambuye. Limapereka chidziŵitso chochuluka.
-
-
Kodi Tiyenera Kupemphera Motani kwa Mulungu?Nsanja ya Olonda—1996 | July 15
-
-
Chokondweretsa ndicho chakuti Yesu anasonyezanso kuti mapemphero athu angaphatikizepo nkhani zaumwini zimene zimatikhudza. Iye anati: “Tipatseni ife tsiku ndi tsiku chakudya cha patsiku. Ndipo mutikhululukire ife machimo athu; pakuti ifenso tikhululukira munthu yense wa mangawa athu. Ndipo musatitengere ife kokatiyesa.” (Luka 11:3, 4) Mawu a Yesu amatanthauza kuti m’zochitika za tsiku ndi tsiku tingapemphe chifuniro cha Mulungu, kuti tingafikire Yehova pa chilichonse chimene chingatidetse nkhaŵa kapena kusokoneza mtendere wathu wamaganizo. Kuchonderera Mulungu m’njira imeneyi nthaŵi zonse kumatithandiza kuzindikira kuti timadalira pa iye. Motero timazindikira bwino lomwe kuti amalamulira moyo wathu. Mofananamo nkopindulitsa kupempha Mulungu tsiku ndi tsiku kuti atikhululukire zolakwa zathu. Chotero timazindikira bwino lomwe zofooka zathu—ndi kukhala ololera kwambiri zophophonya za ena. Chilimbikitso cha Yesu chakuti tizipempherera kulanditsidwa kwathu pa ziyeso nchoyenereranso, makamaka chifukwa cha makhalidwe omaluluzika a dziko lino. Mogwirizana ndi pemphero limenelo, timasamala kupeŵa mikhalidwe imene ingatichititse kulakwa.
-