-
Pezani Chitonthozo kwa YehovaNsanja ya Olonda—1996 | November 1
-
-
14. (a) Kodi ndi lonjezo lotani limene Yesu anapereka pa usiku wa imfa yake? (b) Kodi chofunika nchiyani kuti tipindule modzala ndi chitonthozo cha mzimu woyera wa Mulungu?
14 Pa usiku wa imfa yake, Yesu ananena momvekera bwino kwa atumwi ake okhulupirika kuti posachedwa adzawasiya ndi kubwerera kwa Atate wake. Zimenezi zinawavutitsa mtima ndi chisoni chachikulu. (Yohane 13:33, 36; 14:27-31) Pozindikira kufunika kwawo chitonthozo cha nthaŵi zonse, Yesu analonjeza kuti: “Ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani inu Nkhoswe [“wotonthoza,” NW] ina, kuti akhale ndi inu ku nthaŵi yonse.” (Yohane 14:16) Yesu pano anali kunena za mzimu woyera wa Mulungu, umene unatsanuliridwa pa ophunzirawo masiku 50 pambuyo pa kuukitsidwa kwake.a Kuwonjezera pa zinthu zina, mzimu wa Mulungu unawatonthoza pokumana ndi mayesero ndi kuwalimbitsa kuti apitirize kuchita chifuniro cha Mulungu. (Machitidwe 4:31) Komabe, chithandizo choterocho sichiyenera kuonedwa monga chinthu chimene chimangofika chokha. Kuti apindule nawo mokwanira, Mkristu aliyense ayenera kupitiriza kupempherera chithandizo chopereka chitonthozo chimene Mulungu amapereka kupyolera mwa mzimu wake woyera.—Luka 11:13.
-
-
Pezani Chitonthozo kwa YehovaNsanja ya Olonda—1996 | November 1
-
-
a Imodzi ya ntchito zazikulu za mzimu wa Mulungu pa Akristu a m’zaka za zana loyamba inali kuwadzoza monga ana olera auzimu a Mulungu ndi abale a Yesu. (2 Akorinto 1:21, 22) Zimenezi zimangochitika kwa ophunzira a Kristu okwanira 144,000. (Chivumbulutso 14:1, 3) Lerolino, Akristu ochuluka apatsidwa chiyembekezo cha moyo wosatha padziko lapansi la paradaiso. Ngakhale kuti sali odzozedwa, iwonso amalandirako chithandizo ndi chitonthozo cha mzimu woyera wa Mulungu.
-