Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mphatso Zoyenera Kupatsa Mfumu
    Nsanja ya Olonda—2015 | March 1
    • Kodi zonunkhira zomwe zinkachokera ku mayiko ena, zinkachokera mayiko ati? Aloye, kasiya ndi sinamoni ankachokera kudera lomwe masiku ano ndi China, India ndi Sri Lanka. Mule ndi lubani ankachokera m’dera lachipululu lomwe linkayambira kum’mwera kwa Arabia mpaka kukafika ku Somalia, komwe ndi ku Africa. Ndipo nado wambiri ankachokera ku India, kumapiri a Himalaya.

  • Mphatso Zoyenera Kupatsa Mfumu
    Nsanja ya Olonda—2015 | March 1
    • Perefyumu komanso mankhwala. Anthu olemera ankagwiritsa ntchito zonunkhirazi kununkhiritsa m’nyumba zawo, zovala zawo, pabedi komanso ngati mafuta odzola. (Esitere 2:12; Miyambo 7:17; Nyimbo ya Solomo 3:6, 7; 4:13, 14) Mariya, mchemwali wake wa Lazaro, anathira tsitsi ndi miyendo ya Yesu “mafuta onunkhira. Mafutawa anali nado weniweni,” ndipo anali odula kwambiri. Botolo laling’ono la “nado,” mtengo wake unali wofanana ndi malipiro a chaka chonse.—Maliko 14:3-5; Yohane 12:3-5.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena