-
Kodi N’chifukwa Chiyani Saulo Anazunza Akristu?Nsanja ya Olonda—1999 | June 15
-
-
Damasiko anali pamtunda wa makilomita 220—ulendo woyenda masiku asanu ndi aŵiri kapena asanu ndi atatu—kuchokera ku Yerusalemu. Komabe, “wosaleka kupumira pa akuphunzira . . . kuopsa ndi kupha,” Saulo anapita kwa mkulu wa ansembe ndi kumupempha makalata opita nawo ku masunagoge ku Damasiko. Chifukwa? Kutero kuti Saulo atakapeza ena otsata “Njirayo” akabwere nawo omangidwa ku Yerusalemu. Pokhala atalolezedwa ndi akuluakulu, iye “anapasula Mpingo, naloŵa m’nyumba m’nyumba, nakokamo amuna ndi akazi, nawaika m’ndende.” Ena ‘anawapanda m’masunagoge,’ ndipo ‘anavomerezapo’ (kwenikweni, kuponya “mwala [wake] wovotera”) kuvomereza kuti aphedwe.—Machitidwe 8:3; 9:1, 2, 14; 22:5, 19; 26:10, NW, mawu amtsinde.
Polingalira za maphunziro amene Saulo analandira kwa Gamaliyeli ndiponso mphamvu zimene tsopano anali nazo, akatswiri a maphunziro ena amakhulupirira kuti iye anali atakwera kwambiri kuchoka pokhala chabe wophunzira Chilamulo kufika pokhala munthu waulamuliro winawake mu Chiyuda. Mwachitsanzo, wina analingalira kuti Saulo mwina angakhale atakhala mphunzitsi m’sunagoge wina ku Yerusalemu. Komabe, sitingatsimikize kuti Saulo anatanthauza chiyani mwa ‘kuponya voti yake’—kaya ngati membala wa bwalo lalikulu kapena monga munthu amene anali kusonyeza kuti anali kuchirikiza kuphedwa kwa Akristu.a
-
-
Kodi N’chifukwa Chiyani Saulo Anazunza Akristu?Nsanja ya Olonda—1999 | June 15
-
-
a Malinga ndi kunena kwa buku lakuti The History of the Jewish People in the Age of Jesus Christ (Mbiri ya Ayuda m’Nthaŵi ya Yesu Kristu) (175 B.C.–A.D. 135), lolembedwa ndi Emil Schürer, ngakhale kuti Mishnah sinenapo chilichonse pa mmene Sanihedirini Yaikulu, kapena kuti Sanihedirini ya Mamembala 71 inali kugwirira ntchito, zochita za Masanihedirini ang’onoang’ono, a mamembala 23, zinalongosoledwa mwatsatanetsatane. Ophunzira Chilamulo anali kukamverera milandu yolandira chilango cha imfa imene inali kukambidwa ndi Masanihedirini ang’onoang’ono, kumene anali kuloledwa kulankhula kokha movomereza ndipo osati motsutsa woimbidwa mlanduyo. M’nkhani zosakhudza chilango cha imfa, ankatha kuchita zonse.
-