-
“Osaphunzira Ndiponso Anthu Wamba”‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
-
-
18. Kodi anthu a mumpingo ku Yerusalemu ankathandizana bwanji?
18 Pasanapite nthawi, mpingo umene unali utangoyamba kumene ku Yerusalemu unakula kwambiri ndipo unali ndi anthu oposa 5,000.d Ngakhale kuti ophunzirawo anali ochokera m’madera osiyanasiyana, iwo anali ndi “mtima umodzi ndi maganizo amodzi” ndipo ankagwirizana. (Mac. 4:32; 1 Akor. 1:10) Ophunzirawo ankachita zinthu zambiri kuwonjezera pa kupemphera kwa Yehova kuti adalitse ntchito yawo. Iwo ankathandizana mwauzimu komanso mwakuthupi ngati panafunika kutero. (1 Yoh. 3:16-18) Mwachitsanzo, wophunzira wina dzina lake Yosefe, amene atumwi anam’patsa dzina lakuti Baranaba, anagulitsa malo ake ndipo anapereka ndalama zonse kuti athandizire anthu ochokera kutali amene anatsalira ku Yerusalemu kuti apitirize kuphunzira zambiri zokhudza chikhulupiriro chawo chatsopanocho.
-
-
“Osaphunzira Ndiponso Anthu Wamba”‘Kuchitira Umboni Mokwanira za Ufumu wa Mulungu’
-
-
d Zikuoneka kuti mu 33 C.E., ku Yerusalemu kunali Afarisi okwana 6,000 okha ndi Asaduki ochepa kwambiri. Zimenezi zingasonyeze chifukwa china chimene magulu awiriwa ankachitira mantha kwambiri ndi zimene ophunzirawo ankaphunzitsa zokhudza Yesu.
-