-
‘Amadzaza Mitima Yathu’Nsanja ya Olonda—2013 | July 1
-
-
Kodi Yehova amatisamaliradi kapena alibe nazo ntchito za mavuto amene anthufe timakumana nawo? Baibulo limapereka yankho lolimbikitsa kwambiri. Mulungu amatikonda ndipo amafuna kuti tizisangalala ndi moyo. Tsiku lililonse amatichitira zinthu zabwino ndipo amachita zimenezi ngakhale kwa anthu osayamika. Tiyeni tione zimene mtumwi Paulo ananena.—Werengani Machitidwe 14:16, 17.
Polankhula ndi anthu a mumzinda wa Lusitara, omwe sankalambira Mulungu, Paulo ananena kuti: “M’mbuyomu iye analola anthu a mitundu yonse kuyenda m’njira zawo. Komabe iye sanangokhala wopanda umboni wakuti anachita zabwino. Anakupatsani mvula kuchokera kumwamba ndi nyengo zimene zokolola zanu zimakhala zambiri. Anadzaza mitima yanu ndi chakudya komanso chimwemwe.” Kodi mawu amenewa ankatanthauza chiyani kwa anthu amene Paulo ankawalalikira?
-
-
‘Amadzaza Mitima Yathu’Nsanja ya Olonda—2013 | July 1
-
-
Yehova amatipatsa ufulu wosankha zochita. Mawu a Paulo anasonyeza kuti Yehova analola anthu omwe sanali Ayuda “kuyenda m’njira zawo.” Buku lina lothandiza anthu omasulira Baibulo linanena kuti mawu amenewa amatanthauza “kuchita zimene akufuna,” kapena “kuchita zimene akuona kuti n’zoyenera.” Yehova satikakamiza kuti tizimulambira. Anatipatsa ufulu woti tizitha kusankha tokha zimene tikufuna kuchita.—Deuteronomo 30:19.
-