-
Kuŵala kwa kuunika—Kwakukulu ndi Kwakung’ono (Mbali 2)Nsanja ya Olonda—1995 | May 15
-
-
“Maulamuliro Apamwamba” Amveketsedwa
4, 5. (a) Kodi Ophunzira Baibulo anaona motani Aroma 13:1? (b) Kodi kaimidwe kamene pambuyo pake kanaonedwa kukhala ka Malemba kulinga ku “maulamuliro apamwamba” kanali kotani?
4 Kuŵala kwakukulu kwa kuunika kunaoneka mu 1962 mogwirizana ndi Aroma 13:1, amene amati: “Moyo uliwonse ugonjere maulamuliro apamwamba [“maulamuliro aakulu,” Revised Nyanja Version].” (King James Version) Ophunzira Baibulo oyambirira anadziŵa kuti “maulamuliro apamwamba” otchulidwa pamenepo ananena za maulamuliro adziko. Iwo anakhulupirira kuti lemba limeneli linatanthauza kuti ngati Mkristu alembedwa usilikali panthaŵi ya nkhondo, iye anayenera kuvala yunifomu, kunyamula mfuti, ndi kupita kunkhondo, m’maenje. Anaganiza kuti popeza Mkristu sangaphe munthu mnzake, iye akanakakamizika kuwombera mfuti m’mwamba ngati zinthu zafika povuta.a
5 Nsanja ya Olonda ya July 1, 1963 ndi ya July 15, 1963, inaŵalitsa kuunika kooneka bwino pa nkhaniyo pofotokoza mawu a Yesu pa Mateyu 22:21: “Patsani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.” Mawu a atumwi pa Machitidwe 5:29 anali ofunika: “Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu.” Akristu amagonjera Kaisara—“maulamuliro apamwamba”—malinga ngati kuchita zimenezo sikumafuna kuti Mkristu asemphane ndi lamulo la Mulungu. Kugonjera Kaisara kunaonedwa kukhala ndi malire, osati kopanda malire. Akristu amapatsa Kaisara zinthu zokha zimene sizimasemphana ndi zofuna za Mulungu. Kunali kokhutiritsa chotani nanga kukhala ndi kuunika kooneka bwino pankhaniyo!
-
-
Kuŵala kwa kuunika—Kwakukulu ndi Kwakung’ono (Mbali 2)Nsanja ya Olonda—1995 | May 15
-
-
a Chifukwa cha lingaliro limeneli, The Watch Tower ya June 1 ndi ya June 15, 1929, inafotokoza “maulamuliro apamwamba” kukhala Yehova Mulungu ndi Yesu Kristu. Linali makamaka lingaliro limenelo limene linawongoleredwa mu 1962.
-