-
Njira ya Chikondi SilepheraNsanja ya Olonda—1999 | February 15
-
-
9. Kodi Baibulo lili ndi zitsanzo zochenjeza zotani za anthu amene anali kutsata za iwo okha?
9 Chikondi “sichitsata za mwini yekha.” (1 Akorinto 13:5) Munthu wachikondi sachenjerera ena kuti apeze zimene akufuna. Baibulo lili ndi zitsanzo zochenjeza zokhudza nkhani imeneyi. Mwachitsanzo: Timaŵerenga za Delila, Yezebeli, ndi Ataliya—akazi amene anachenjerera ena kuti akwaniritse zolinga zawo zadyera. (Oweruza 16:16; 1 Mafumu 21:25; 2 Mbiri 22:10-12) Panalinso Abisalomu, mwana wa Mfumu Davide. Iye anali kufikira anthu obwera ku Yerusalemu kuti milandu yawo idzaweruzidwe. Ndiyeno anali kuneneza bwalo la mfumu mwamachenjera kuti silisamala za mavuto a anthuwo. Kenako ankanena mosapita mbali kuti bwalolo lingofunikira munthu wokoma mtima ngati iyeyo! (2 Samueli 15:2-4) Inde, Abisalomu sanali kufunira anthu ovutikawo zabwino, koma iye mwini. Pochita monga mfumu yodzilonga yokha, iye anakopa mitima ya anthu ambiri. Koma m’kupita kwa nthaŵi, Abisalomu anagonjetsedwa kotheratu. Atamwalira, sanaonedwenso kukhala wofunikira kuikidwa m’manda mwaulemu.—2 Samueli 18:6-17.
10. Kodi tingasonyeze motani kuti tikupenyereranso za ena?
10 Limeneli ndi chenjezo kwa Akristu lerolino. Kaya ndife amuna kapena akazi, mwina mwachibadwa timatha kusonkhezera anthu ena. Zingakhale zosavuta kwa ife kuchita zimene tikufuna, kunena kwake titero, mwa kuyankhula kwambiri kuposa ena pokambirana nawo kapena mwa kuumirira malingaliro ako kuti awo amene ali ndi malingaliro osiyana agonje. Koma ngati ndifedi achikondi, tidzapenyereranso za ena. (Afilipi 2:2-4) Sitidzapondereza ena kapena kuchirikiza malingaliro okayikitsa chifukwa cha chidziŵitso chathu kapena malo athu m’gulu la Mulungu, monga kuti malingaliro athu okha ndi amene angagwiritsidwe ntchito. M’malo mwake, tidzakumbukira mwambi wa m’Baibulo wakuti: “Kunyada kutsogolera kuwonongeka; mtima wodzikuza ndi kutsogolera kupunthwa.”—Miyambo 16:18.
-
-
Njira ya Chikondi SilepheraNsanja ya Olonda—1999 | February 15
-
-
11. (a) Kodi chikondi chokoma mtima komanso chosachita zosayenera tingachisonyeze m’njira zotani? (b) Kodi tingasonyeze motani kuti sitikondwera ndi chinyengo?
11 Paulo analembanso kuti chikondi chili “chokoma mtima” ndi kutinso “sichichita zosayenera.” (1 Akorinto 13:4, 5) Inde, chikondi sichidzatilola kukhala amwano, owola mkamwa, kapena opanda ulemu. M’malo mwake, tidzaganiziranso malingaliro a ena. Mwachitsanzo, munthu wachikondi adzapeŵa kuchita zinthu zimene zingavutitse chikumbumtima cha ena. (Yerekezerani ndi 1 Akorinto 8:13.) Chikondi “sichikondwera ndi chinyengo, koma chikondwera ndi choonadi.” (1 Akorinto 13:6) Ngati tikonda malamulo a Yehova, sitidzaona chisembwere ngati nkhani yaing’ono ndiponso sitidzakondwera ndi zinthu zimene Mulungu amadana nazo. (Salmo 119:97) Chikondi chidzatithandiza kukondwera ndi zinthu zomangirira osati zowononga.—Aroma 15:2; 1 Akorinto 10:23, 24; 14:26.
12, 13. (a) Kodi tiyenera kuchita motani wina akatilakwira? (b) Tchulani zitsanzo za m’Baibulo zosonyeza kuti ngakhale kukwiya pazifukwa zomveka kungatipangitse kuchita zinthu mosaganiza bwino?
12 Paulo analemba kuti chikondi “sichipsa mtima” (“sichikhala cha mtima wapachala,” Phillips). (1 Akorinto 13:5) Zoonadi, anthu opanda ungwirofe n’chibadwa chathu kuvutika maganizo kapena kukwiya wina akatilakwira. Komabe, n’kulakwa kusunga chakukhosi kwa nthaŵi yaitali kapena kukhalabe wokwiya. (Salmo 4:4; Aefeso 4:26) Ngakhale titakwiya pachifukwa chomveka, ngati sitidziletsa tingachite zinthu mosaganiza bwino, ndipo Yehova adzatiimba mlandu.—Genesis 34:1-31; 49:5-7; Numeri 12:3; 20:10-12; Salmo 106:32, 33.
13 Ena alola zophophonya za ena kukhudza chosankha chawo cha kupezeka pamisonkhano yachikristu kapena kukhala ndi mbali mu utumiki wakumunda. Kumbuyoko, ambiri mwa anthu ameneŵa anachita bwino pomenya nkhondo yolimba ya chikhulupiriro, mwinamwake mwa kupirira chitsutso cha banja lawo, kunyozedwa ndi anzawo akuntchito, ndi zina zotero. Anapirira zopinga zimenezo chifukwa chakuti anaziona ngati ziyeso za kukhulupirika kwawo, ndipo zinalidi motero. Koma kodi n’chiyani chimachitika Mkristu mnzawo akanena kapena kuchita kenakake kosasonyeza chikondi? Kodi ichinso si chiyeso cha kukhulupirika? Ndithudi n’chiyeso, popeza kuti ngati tikhalabe okwiya, ‘tingam’patse malo Mdyerekezi.’—Aefeso 4:27.
14, 15. (a) Kodi ‘kulemba cholakwa’ kumatanthauzanji? (b) Kodi tingam’tsanzire motani Yehova pa kukhala wokhululukira?
14 Ndiye chifukwa chake Paulo anawonjezera kuti chikondi “sichilingirira zoipa [“sichilemba zolakwa,” NW].” (1 Akorinto 13:5) Pamenepa anagwiritsa ntchito liwu la oŵerengera ndalama, mwachionekere akumapereka lingaliro la kulemba cholakwa cha wina m’buku la ngongole kuti chisaiŵalidwe. Kodi chingakhale chikondi kumakumbukira nthaŵi zonse mawu kapena zochita zimene zinatipweteketsa mtima, monga kuti nthaŵi ina yake m’tsogolo mudzazifuna? Ndife okondwa chotani nanga kuti Yehova samationa m’njira yopanda chifundo imeneyo! (Salmo 130:3) Inde, tikalapa, iye amafafaniza zolakwa zathu.—Machitidwe 3:19.
15 Tingatsanzire Yehova pankhaniyi. Sitiyenera kuvutika maganizo mopambanitsa ngati taona kuti wina watinyozera. Ngati tikwiya msanga, tingadzivulaze tokha kuposanso mmene munthu wotilakwirayo angativulazire. (Mlaliki 7:9, 22) M’malo mwake timayenera kukumbukira kuti chikondi “chikhulupirira zinthu zonse.” (1 Akorinto 13:7) Inde, palibe aliyense wa ife amene akufuna kukhala wonyengeka msanga, komanso sitiyenera kumangokayikira zolinga za abale athu. Nthaŵi zonse ngati tingathe, tiyeni tisakayikire zolinga za ena.—Akolose 3:13.
-