Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Zimene Zachitika M’zaka 100 Zimene Ufumu Wakhala Ukulamulira
    Nsanja ya Olonda—2015 | November 15
    • 2. (a) Kodi n’kutheka kuti panali anthu angati pamene Yesu anapereka lamulo la pa Mateyu 28:19, 20? (b) Kodi tikudziwa bwanji kuti ambiri mwa anthuwa anadzakhala Akhristu?

      2 Tsiku lina Yesu ataukitsidwa, anakumana ndi anthu oposa 500. (1 Akor. 15:6) N’kutheka kuti pa nthawiyi m’pamene anapereka lamulo lakuti otsatira ake azikalalikira “anthu a mitundu yonse.”a Koma ntchito imene anawauza kuti agwireyi sinali yophweka. Iye ananeneratu kuti ntchito yolalikirayi idzachitika mpaka “m’nyengo ya mapeto a nthawi ino.” Choncho tikamagwira nawo ntchito imeneyi timathandiza kuti ulosiwu ukwaniritsidwe.—Mat. 28:19, 20.

  • Zimene Zachitika M’zaka 100 Zimene Ufumu Wakhala Ukulamulira
    Nsanja ya Olonda—2015 | November 15
    • a Zikuoneka kuti ambiri mwa anthuwa anadzakhala Akhristu. Tikutero chifukwa chakuti m’kalata imene Paulo analembera Akhristu a ku Korinto, ananena kuti anthu oposa 500 aja tsopano anali “abale.” Iye ananenanso kuti: “Ambiri a iwo akali ndi moyo mpaka lero, koma ena anagona mu imfa.” Choncho zikuoneka kuti Paulo ankadziwana ndi ena mwa Akhristu amene analipo pamene Yesu ankapereka lamulo loti ophunzira ake azilalikira.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena