-
Tito—‘Wantchito Mnzanga Pokuthandizani’Nsanja ya Olonda—1998 | November 15
-
-
Makalata a Paulo opita kwa Akorinto akusonyeza kuti choyamba anawalembera kuti ‘asayanjane ndi achigololo.’ Anawauza kuchotsa wachigololo wosalapayo amene anali pakati pawo. Inde, Paulo anawalembera kalata yamphamvu, kuchita zimenezo “ndi misozi yambiri.” (1 Akorinto 5:9-13; 2 Akorinto 2:4) Zidakali choncho, Tito anatumidwa ku Korinto kukathandiza kusonkhanitsa zinthu za Akristu osoŵa a ku Yudeya zimene zinali kusonkhanitsidwa kumeneko. Mwina anatumidwanso kuti akaone mmene Akorinto akulabadirira kalata ya Paulo.—2 Akorinto 8:1-6.
-
-
Tito—‘Wantchito Mnzanga Pokuthandizani’Nsanja ya Olonda—1998 | November 15
-
-
Nanga za mbali inayo ya ulendo wa Tito wa ku Korinto—kulinganiza zopereka zopita kwa oyera mtima a ku Yudeya? Malinga ndi chidziŵitso chimene timapeza pa 2 Akorinto, tinganene kuti Tito anali kuchitanso zimenezo. Kalata imeneyo iyenera kuti inalembedwa ku Makedoniya chakumapeto kwa 55 C.E., Tito ndi Paulo atangokumana kumene. Paulo analemba kuti Tito, amene anayambitsa zoperekazo, anali atatumidwanso komweko ndi omthandiza ena aŵiri amene sanawatchule maina kuti akamalizitse ntchitoyo. Pokhala wowaderadi nkhaŵa Akorinto, Tito anali wofunitsitsa kubwerera. Pamene Tito anali paulendo wobwerera ku Korinto, ayenera kuti anali atanyamula kalata yachiŵiri youziridwa ya Paulo yopita kwa Akorinto.—2 Akorinto 8:6, 17, 18, 22.
-