Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 4 | Mulungu Angakuthandizeni Kuthetsa Mtima Wachidani
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2022 | Na. 1
    • Baibulo Limati:

      “Makhalidwe amene mzimu woyera umatulutsa ndiwo chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, kukoma mtima, ubwino, chikhulupiriro, kufatsa ndi kudziletsa.”​—AGALATIYA 5:22, 23.

      Zimene Lembali Limatanthauza:

      Mulungu angatithandize kuthetsa chidani. Mzimu wake woyera ungatithandize kukhala ndi makhalidwe amene patokha sitingakwanitse kukhala nawo. Choncho, m’malo moyesetsa kulimbana ndi kuthetsa mtima wachidani patokha, tingachite bwino kudalira Mulungu kuti atithandize. Tikachita zimenezi tidzafanana ndi Paulo yemwe analemba kuti: “Pa zinthu zonse, ndimapeza mphamvu kuchokera kwa iye amene amandipatsa mphamvu.” (Afilipi 4:13) Komanso tidzanena kuti: “Thandizo langa lichokera kwa Yehova.”​—Salimo 121:2.

  • 4 | Mulungu Angakuthandizeni Kuthetsa Mtima Wachidani
    Nsanja ya Olonda (Yogawira)—2022 | Na. 1
    • Waldo sanasangalale ataona kuti mkazi wake wayamba kuphunzira Baibulo ndi a Mboni za Yehova. Iye anati: “Ndinkadana ndi a Mboni ndipo nthawi zambiri ndinkawatukwana. Koma ndinkadabwa nawo chifukwa sankandibwezera.”

      Patapita nthawi nayenso anayamba kuphunzira Baibulo. Iye anati: “Zinkandivuta kuti ndizigwiritsa ntchito zimene ndinkaphunzira. Ndinkaona kuti n’zosatheka kusiya khalidwe langa lankhanza.” Koma mfundo ina imene anaphunzira m’Baibulo inamuthandiza kusintha maganizo amenewa.

      Waldo anafotokoza kuti: “Tsiku lina m’bale amene ankandiphunzitsa Baibulo, dzina lake Alejandro, anandiuza kuti ndiwerenge Agalatiya 5:22, 23. . . . Alejandro anandiuza kuti sindingakhale ndi makhalidwe amenewa pandekha, ndikufunika kudalira mzimu woyera wa Mulungu. Mfundo imeneyi inandithandiza kusintha maganizo amene ndinali nawo.”

      Waldo anakwanitsa kusiya kudana ndi anthu ena chifukwa chakuti anadalira Mulungu kuti amuthandize. Iye anati: “Abale anga komanso anzanga samamvetsa akaona kuti ndinasintha.” Iye ananenanso kuti: “Yehova wandithandiza kuti ndisinthe khalidwe langa lokonda zachiwawa moti panopa ndine munthu wokonda mtendere.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena