Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w90 4/15 tsamba 31
  • Kodi Ndinu Fano la Inumwini?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Ndinu Fano la Inumwini?
  • Nsanja ya Olonda​—1990
Nsanja ya Olonda​—1990
w90 4/15 tsamba 31

Kodi Ndinu Fano la Inumwini?

Mosadziŵa, anthu ena amapanga mafano a iwo eni. Baibulo pa Aefeso 5:5 (NW) limalongosola kuti: “Pakuti inu muchidziŵa ichi, mukumadzidziŵira nokha, kuti palibe wadama kapena munthu wauchisi kapena munthu waumbombo​—zimene zimatanthauza kukhala wopembedza mafano​—ali ndi choloŵa chiri chonse mu ufumu wa Kristu ndi wa Mulungu.” (Akolose 3:5; yerekezerani ndi Agalatiya 5:19-21.) Zikhumbo zakuthupi zingabwere pakati pa munthu ndi Mulungu. Paulo akunena za zimenezo kuti “mulungu wawo ndiyo mimba yawo.” (Afilipi 3:18, 19) M’mawu ena, iwo ali ndi “mulungu” wina pambali pa Yehova, namaika zikhumbo zawo zakuthupi m’malo oyamba. Mkhalidwe woterowo ungalepheretse munthu kuloŵa mu Ufumu wa Mulungu. (1 Akorinto 6:9, 10) Chotero, pali chifukwa chabwino, kulabadira mawu a mtumwi Paulo akuti: “Chifukwa chake, okondedwa anga, thaŵani kupembedza mafano.”​—1 Akorinto 10:14.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena