Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mungatani Kuti Kuwerenga Baibulo Kuzikuthandizani Kwambiri?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 3. Kodi mungatani kuti muzipeza nthawi yowerenga Baibulo?

      Kodi zimakuvutani kuti mupeze nthawi yowerenga Baibulo? Ambirife zimativuta. Muziyesetsa ‘kugwiritsa ntchito bwino nthawi yanu.’ (Aefeso 5:16) Kuti mukwanitse kuchita zimenezi, muzisankha nthawi yoti muziwerenga Baibulo tsiku lililonse. Anthu ena amakonda kuwerenga Baibulo m’mamawa. Ena amakonda kuwerenga chakumasana, mwina pa nthawi yopuma. Pomwe ena amakonda kuwerenga chakumadzulo asanakagone. Nanga inuyo mungakonde kumawerenga nthawi yanji?

  • N’chiyani Chingatithandize Kuti Tizisankha Zinthu Mwanzeru?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 3. Muzitsatira mfundo za m’Baibulo

      Kodi mfundo za m’Baibulo zingatithandize bwanji tikamasankha zochita? Onerani VIDIYO, kenako mukambirane mafunso otsatirawa.

      VIDIYO: Muzitsatira Mfundo za M’Baibulo Mukamasankha Zochita (5:54)

      • Kodi Yehova anatipatsa mphatso yamtengo wapatali iti?

      • N’chifukwa chiyani Yehova anatipatsa mphatso imeneyi?

      • Kodi Yehova watipatsa chiyani pofuna kutithandiza kusankha zinthu mwanzeru?

      Kuti muone chitsanzo cha mfundo ya m’Baibulo, werengani Aefeso 5:15, 16. Kenako mukambirane mmene ‘mungagwiritsire ntchito bwino nthawi yanu’ . . .

      • powerenga Baibulo tsiku lililonse.

      • kuti mukhale mwamuna kapena mkazi wabwino, kholo kapenanso mwana wabwino.

      • kuti muzichita nawo misonkhano yampingo.

  • Muzisankha Zosangalatsa Zomwe Sizingakhumudwitse Yehova
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 2. N’chifukwa chiyani tifunika kusamala kuti tisamangokhalira kuchita zosangalatsa?

      Ngakhale titasankha zosangalatsa zimene sizingakhumudwitse Yehova, tifunika kusamala kuti tisamangokhalira kuchita zosangalatsazo. Zili choncho chifukwa chakuti kupanda kusamala tingalephere kupeza nthawi yochitira zinthu zofunika kwambiri. Baibulo limatilimbikitsa kuti ‘tizigwiritsa ntchito bwino nthawi yathu.’​—Werengani Aefeso 5:15, 16.

  • Muzisankha Zosangalatsa Zomwe Sizingakhumudwitse Yehova
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 4. Muzigwiritsa ntchito nthawi yanu mwanzeru

      Onerani VIDIYO, kenako mukambirane funso ili:

      VIDIYO: Kodi Mumagwiritsa Ntchito Bwanji Nthawi Yanu? (2:45)

      • Ngakhale kuti m’bale wamuvidiyoyi sankaonera zinthu zoipa, kodi vuto lake linali lotani?

      Werengani Afilipi 1:10, kenako mukambirane funso ili:

      • Kodi vesili lingatithandize bwanji kupewa kuthera nthawi yaitali pa zinthu zosangalatsa?

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena