Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ubatizo Ungakuthandizeni Kukhala Ndi Tsogolo Labwino
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 3. Kodi munthu ayenera kuchita chiyani kuti abatizidwe?

      Musanabatizidwe, muyenera kuphunzira zokhudza Yehova komanso kuyamba kumukhulupirira kwambiri. (Werengani Aheberi 11:6.) Mukapitiriza kuphunzira zambiri zokhudza Yehova komanso kumukhulupirira, m’pamenenso mudzayambe kumukonda kwambiri. Kenako mudzayamba kufuna kulalikira zokhudza Yehova komanso kuchita zimene Iye amafuna pa moyo wanu. (2 Timoteyo 4:2; 1 Yohane 5:3) Munthu akangoyamba ‘kuyenda mogwirizana ndi zimene Yehova amafuna, kuti azimukondweretsa pa chilichonse,’ amasankha kupereka moyo wake kwa Mulungu kenako amabatizidwa.​—Akolose 1:9, 10.a

  • Ubatizo Ungakuthandizeni Kukhala Ndi Tsogolo Labwino
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • a Munthu ayenera kubatizidwanso ngakhale kuti anabatizidwa kale ku chipembedzo china. Tikutero chifukwa chipembedzocho sichinamuthandize kudziwa choonadi cha m’Baibulo.​—Onani Machitidwe 19:1-5 ndi Phunziro 13.

  • Kodi Mwakonzeka Kubatizidwa?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 1. Kodi muyenera kudziwa zinthu zochuluka bwanji kuti mubatizidwe?

      Kuti mubatizidwe, muyenera ‘kudziwa choonadi molondola.’ (1 Timoteyo 2:4) Zimenezi sizikutanthauza kuti muyenera kudziwa yankho la funso lililonse limene anthu angafunse lokhudza Baibulo. Tikutero chifukwa chakuti ngakhale Akhristu amene anabatizidwa kalekale, amapitirizabe kuphunzira zinthu zina. (Akolose 1:9, 10) Komabe, kuti mubatizidwe mufunika kuyamba kumvetsa bwino zimene Baibulo limaphunzitsa. Akulu amumpingo adzakuthandizani kudziwa ngati mwadziwa zinthu zokwanira zokhudza Baibulo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena