Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w01 9/1 tsamba 31
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
  • Nsanja ya Olonda—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Yesu Analidi Mwana wa Mulungu?
    Galamukani!—2006
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • N’chifukwa Chiyani Baibulo Limati Yesu Ndi Mwana wa Mulungu?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda—2006
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2001
w01 9/1 tsamba 31

Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga

Akolose 1:16 amanena za Mwana wa Mulungu kuti “zinthu zonse zinalengedwa mwa Iye ndi kwa Iye.” Kodi zinthu zonse zinalengedwa “kwa” Mwana wa Mulungu, Yesu, motani?

Yehova anagwiritsa ntchito Mwana wake wobadwa yekha ngati mmisiri polenga zinthu zina zonse, ndiko kuti, zinthu zonse kupatulapo Yesu mwiniyo. (Miyambo 8:27-30; Yohane 1:3) Moyenerera, Mwanayo amakondwera ndi zinthu zimene analengazi, ndipo m’ganizo limeneli zinalengedwa “kwa” iye.

Tikudziŵa kuti makolo amayembekeza kukondwera, ndipo nthaŵi zambiri amakondweradi ndi ana awo. N’chifukwa chake mwambi wa Baibulo umanena za “mwana amene [atate ake] akondwera naye.” (Miyambo 3:12; 29:17) N’chimodzimodzinso kuti Yehova Mulungu anakondwera ndi Aisrayeli pamene anthu akewo anali okhulupirika. (Salmo 44:3; 119:108; 147:11) Amakondweranso ndi kukhulupirika kwa anthu ake lerolino.​—Miyambo 12:22; Ahebri 10:38.

Motero, zinali zoyenera kuti Mulungu anafuna kuti wantchito mnzake, Yesu, akondwere ndi ntchito imene anagwira. Ndipotu, Miyambo 8:31 imanena kuti Mwanayo ‘anakondwera ndi dziko lake lokhalamo anthu, ndi kusekerera ndi ana a anthu.’ Akolose 1:16 amatanthauza zimenezi pamene akuti: ‘zinthu zonse zinalengedwa mwa Iye ndi kwa Iye.’

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena