-
Tetezani Ana M’Banja LanuGalamukani!—2007 | October
-
-
“OPANDA chikondi chachibadwa.” Baibulo limanena zimenezi pofotokoza mmene anthu ambiri alili “m’masiku otsiriza” ano. (2 Timoteyo 3:1, 3, 4) Kufala kwa vuto la kuchita chipongwe ana panyumba kukutsimikizira kuti ulosi umenewu ukukwaniritsidwa. Kwenikweni, mawu a Chigiriki akuti asʹ-tor-gos, omwe m’Chichewa amati “opanda chikondi chachibadwa,” amasonyeza kusowa chikondi chimene chimayenera kukhalapo pakati pa achibale, makamaka pakati pa makolo ndi ana awo.a Ndipotu nthawi zambiri achibale ndi amene amachita ana zachipongwe zotere.
-
-
Tetezani Ana M’Banja LanuGalamukani!—2007 | October
-
-
a Mabuku ena amamasulira mawu a Chigiriki chakalewa motere: “Kuumira mtima achibale.” Motero, Baibulo lina linamasulira vesi imeneyi motere: “Adzakhala . . . osowa chikondi cha pa abale awo.”
-