-
Mmene Mungakhalire Kholo LachipambanoNsanja ya Olonda—1988 | May 1
-
-
Amayi a Timoteo ndipo mwinamwake agogo ake, Loisi, anatsimikizira kuti sanali malingaliro awo omwe anamsangalatsa iye kuchokera ku ubwana; m’malomwake, iwo anadziŵa kuti zinali ziphunzitso za Yehova zomwe zikampangitsa iye kukhala wanzeru kaamba ka chipulumutso. Kalata yolembedwa kwa Timoteo ndi mtumwi Wachikristu Paulo inalongosola kuti: “Koma ukhalebe iwe mu izi zimene waziphunzira, nutsimikizika mtima nazo, podziŵa amene adakuphunzitsa; ndi kuti kuyambira ukhanda wako wadziŵa malemba opatulika, okhoza kukupatsa nzeru kufikira chipulumutso, mwa chikhulupiriro cha mwa Kristu Yesu.”—2 Timoteo 3:14, 15.
-
-
Mmene Mungakhalire Kholo LachipambanoNsanja ya Olonda—1988 | May 1
-
-
Mosakaikira, Timoteo analingaliranso mtundu wa anthu umene amayi ake ndi agogo ake anali—anthu auzimu mowonadi. Iwo sanakhoze kumunamiza iye kapena kupotoza chowonadi kaamba ka dyera; iwo sanakhozenso kukhala onyenga. Timoteo, ngakhale kuli tero, analibe kukaikira ponena za zinthu zimene anaphunzira. Ndipo palibe kukaikira kuti moyo wake wauchikulire monga Mkristu wachangu unatonthoza mtima wa amayi ake okhulupirika.
-