-
Tikhaletu iwo AchikhulupiriroNsanja ya Olonda—1999 | December 15
-
-
Kugwiritsa Ntchito Bwino Mawu a Mulungu
6. Kodi Paulo anali kutchula mawu ochokera kuti pamene analemba mawu opezeka pa Ahebri 10:38?
6 Paulo anamangiriranso chikhulupiriro mwa okhulupirira anzake pogwiritsa ntchito Malemba mwaluso. Mwachitsanzo, analemba kuti: “Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo wochokera m’chikhulupiriro: ndipo ngati abwerera, moyo wanga ulibe kukondwera mwa iye.” (Ahebri 10:38) Paulo panopo anali kutchula mawu a m’buku la mneneri Habakuku.a Mawu ameneŵa ayenera kuti anali odziŵika kwa oŵerenga kalata ya Paulo, Akristu achihebri amene anali kuwadziŵa bwino kwambiri mabuku amaulosi. Poona cholinga chake, chomwe chinali kulimbitsa chikhulupiriro cha Akristu a m’Yerusalemu ndi m’madera oyandikana ndi mzindawo cha m’chaka cha 61 C.E., chitsanzo cha Habakuku chinali choyenerera zedi. Chifukwa chiyani?
7. Kodi Habakuku anaulemba liti ulosi wake, ndipo zinthu zinali motani m’dziko la Yuda panthaŵiyo?
7 Zikusonyeza kuti Habakuku analemba buku lake patangotsala zaka 20, kapena kuposapo pang’ono, kuti Yerusalemu awonongedwe mu 607 B.C.E. M’masomphenya, mneneriyo anaona Akasidi (kapena kuti, Ababulo), ‘mtundu woŵaŵa ndi waliŵiro,’ akukantha Yuda ndi kuwononga Yerusalemu, kumeza anthu ndi mitundu. (Habakuku 1:5-11) Koma tsoka limenelo linali litaloseredwa kuyambira m’tsiku la Yesaya, zaka zoposa zana limodzi m’mbuyo mwake. M’nthaŵi ya Habakuku, Yehoyakimu analoŵa m’malo Mfumu Yosiya yabwinoyo, ndipo kuipa kunachulukanso m’dziko la Yuda. Yehoyakimu anazunza ngakhalenso kupha anthu amene anali kuyankhula m’dzina la Yehova. (2 Mbiri 36:5; Yeremiya 22:17; 26:20-24) Ndiye chifukwa chaketu mneneri wachisoniyo Habakuku anafuula kuti: “Yehova, . . . mpaka liti?”—Habakuku 1:2.
8. N’chifukwa chiyani chitsanzo cha Habakuku chinathandiza Akristu m’zaka zana loyamba ndiponso lerolino?
8 Habakuku sanali kudziŵa kuti chiwonongeko cha Yerusalemu chinali pafupi motani. Mofananamo, Akristu a m’zaka zana loyamba sanali kudziŵa kuti dongosolo lazinthu lachiyuda lidzatha liti. Ifenso lerolino sitikudziŵa “tsiku ilo ndi nthaŵi yake” pamene chiweruzo cha Yehova chidzadza padongosolo loipa lino la zinthu. (Mateyu 24:36) Chotero tiyeni tione yankho la mbali ziŵiri la Yehova kwa Habakuku. Choyamba, iye anatsimikizira mneneriyo kuti mapeto adzadza panthaŵi yake. ‘Sadzazengereza,’ anatero Mulungu, ngakhale kuti kwa munthu, angaoneke ngati kuti akuchedwa. (Habakuku 2:3) Chachiŵiri, Yehova anakumbutsa Habakuku kuti: “Wolungama adzakhala ndi moyo mwa chikhulupiriro chake.” (Habakuku 2:4) Chimenechi ndi choonadi chosangalatsa ndiponso chosavuta kumva! Chofunika kwambiri si nthaŵi pamene mapetowo adzadza ayi, koma ngati tingapitirizebe kukhala moyo wachikhulupiriro.
9. Kodi atumiki omvera a Yehova anakhalabe motani ndi moyo mwa chikhulupiriro chawo (a) mu 607 B.C.E.? (b) pambuyo pa 66 C.E.? (c) N’chifukwa chiyani kulimbitsa chikhulupiriro chathu kuli kofunika zedi?
9 Yerusalemu atasakazidwa mu 607 B.C.E., Yeremiya, mlembi wake Baruki, Ebedi-Meleki, ndi Arekabu okhulupirikawo anaona choonadi cha lonjezo la Yehova kwa Habakuku. ‘Anakhalabe ndi moyo’ mwa kupulumuka chiwonongeko chowopsacho cha Yerusalemu. Chifukwa chiyani? Yehova anafupa kukhulupirika kwawo. (Yeremiya 35:1-19; 39:15-18; 43:4-7; 45:1-5) Mofananamo, Akristu achihebri a m’zaka zana loyamba ayenera kuti analabadira uphungu wa Paulo, popeza kuti pamene magulu ankhondo a Roma anazinga Yerusalemu mu 66 C.E. kenako n’kubwerera pachifukwa chosadziŵika bwino, Akristuwo anamvera mokhulupirika chenjezo la Yesu lakuti ayenera kuthaŵa. (Luka 21:20, 21) Anakhalabe ndi moyo chifukwa cha kukhulupirika kwawo. Momwemonso, ifeyo tidzakhalabe ndi moyo ngati tikhalabe okhulupirika pamene mapeto afika. N’chifukwa chofunikatu zedi cholimbitsira chikhulupiriro chathu tsopano!
-
-
Tikhaletu iwo AchikhulupiriroNsanja ya Olonda—1999 | December 15
-
-
a Paulo anatchula mawu a pa Habakuku 2:4 monga momwe alili mu Septuagint, imene ili ndi mawu akuti “ngati wina abwerera, moyo wanga ulibe kukondwera mwa iye.” Mawu ameneŵa sakupezeka m’mipukutu yachihebri imene ilipo tsopano. Ena anena kuti Septuagint inazikidwa pa mipukutu yachihebri yakale kwambiri imene kulibenso lerolino. Mulimonse mmene zinalili, Paulo anawaphatikiza pano mawuwo mosonkhezeredwa ndi mzimu woyera wa Mulungu. Chotero mawuwo ndi ouziridwa ndi Mulungu.
-