Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • fy mutu 16 tsamba 183-191
  • Mangirani Banja Lanu Mtsogolo Mokhalitsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mangirani Banja Lanu Mtsogolo Mokhalitsa
  • Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • PHINDU LA KUDZILETSA
  • LINGALIRO LOYENERA LA UMUTU
  • ‘KHALANI WOTCHERA KHUTU’
  • NTCHITO YAIKULU YA CHIKONDI
  • BANJA LIMENE LIMACHITA CHIFUNIRO CHA MULUNGU
  • BANJA NDI MTSOGOLO MWANU
  • Londolani Mtendere Waumulungu m’Moyo wa Banja
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Makiyi Aŵiri a Ukwati Wokhalitsa
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Kupangitsa Moyo Wabanja Kukhala Wabwino
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Khalani Odzipereka kwa Mulungu Panyumba
    Lambirani Mulungu Woona Yekha
Onani Zambiri
Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
fy mutu 16 tsamba 183-191

Mutu 16

Mangirani Banja Lanu Mtsogolo Mokhalitsa

1. Kodi chifuno cha Yehova chinali chotani pa kakonzedwe ka banja?

PAMENE Yehova anakwatitsa Adamu ndi Hava, Adamu anasonyeza chisangalalo chake mwa kulakatula ndakatulo yachihebri yoyambirira kulembedwa. (Genesis 2:22, 23) Komabe, Mlengi anali ndi zochuluka m’maganizo kuposa kudzetsa chabe chimwemwe kwa ana ake aumunthu. Iye anafuna kuti anthu okwatirana ndiponso mabanja achite chifuniro chake. Anauza okwatirana oyambawo kuti: “Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi, muligonjetse: mulamulire pa nsomba za m’nyanja, ndi pa mbalame za m’mlengalenga, ndi pa zamoyo zonse zakukwaŵa padziko lapansi.” (Genesis 1:28) Imeneyo inali ntchito yaulemerero ndi yofupa kwambiri! Ndipo iwo pamodzi ndi ana awo amtsogolo akanakhala achimwemwe kwabasi, ngati Adamu ndi Hava akanachita chifuniro cha Yehova mwa kumvera konse!

2, 3. Kodi ndi motani mmene mabanja angapezere chimwemwe chachikulu koposa lerolino?

2 Lerolinonso, mabanja amakhala achimwemwe pamene achitira pamodzi chifuniro cha Mulungu. Mtumwi Paulo analemba kuti: “Chipembedzo [“kudzipereka kwaumulungu,” NW] chipindula zonse, popeza chikhala nalo lonjezano la ku moyo uno, ndi la moyo ulinkudza.” (1 Timoteo 4:8) Banja lokhala ndi kudzipereka kwaumulungu limenenso limatsatira chitsogozo cha Yehova chopezeka m’Baibulo lidzapeza chimwemwe mu “moyo uno.” (Salmo 1:1-3; 119:105; 2 Timoteo 3:16) Ngakhale ngati mmodzi yekha m’banja ndiye amagwiritsira ntchito mapulinsipulo a Baibulo, zinthu zimakhalapo bwino kuposa ngati palibe amene amatero.

3 Buku lino lafotokoza mapulinsipulo ambiri a Baibulo amene amathandiza kupeza chimwemwe cha banja. Mwachionekere, mwaona kuti ena a iwo aonekera mobwerezabwereza m’buku lonseli. Chifukwa ninji? Chifukwa chakuti amanena za mfundo zamphamvu za choonadi zimene zimagwira ntchito kaamba ka ubwino wa onse m’mbali zosiyanasiyana za moyo wa banja. Banja limene limayesayesa kugwiritsira ntchito mapulinsipulo a Baibulo ameneŵa limapeza kuti kudzipereka kwaumulungu kulidi ndi “lonjezano la ku moyo uno.” Tiyeni tionenso anayi a mapulinsipulo ofunika amenewo.

PHINDU LA KUDZILETSA

4. Kodi nchifukwa ninji kudziletsa kuli kofunika muukwati?

4 Mfumu Solomo anati: “Wosalamulira mtima wake akunga mudzi wopasuka wopanda linga.” (Miyambo 25:28; 29:11) ‘Kulamulira mtima,’ kudziletsa, nkofunika kwambiri kwa amene akufuna ukwati wachimwemwe. Kugonja ku maganizo owononga, onga ukali kapena chilakolako chachisembwere, kudzawononga zinthu zimene zidzatenga zaka zambiri kukonza—ngati zingakonzedwe nkomwe.

5. Kodi munthu wopanda ungwiro angakulitse motani kudziletsa, ndipo pali mapindu otani?

5 Ndithudi, palibe aliyense amene ali mbadwa ya Adamu amene angakhoze kulamulira kotheratu thupi lake lopanda ungwiro. (Aroma 7:21, 22) Komabe, kudziletsa ndiko chipatso cha mzimu. (Agalatiya 5:22, 23) Chifukwa chake, mzimu wa Mulungu udzabala chipatso cha kudziletsa mwa ife ngati tipempherera mkhalidwe umenewu, ngati tigwiritsira ntchito uphungu woyenera wopezeka m’Malemba, ndipo ngati tiyanjana ndi ena amene amausonyeza ndi kupeŵa awo amene samatero. (Salmo 119:100, 101, 130; Miyambo 13:20; 1 Petro 4:7) Kachitidwe kameneko kadzatithandiza ‘kuthaŵa dama,’ ngakhale pamene tiyesedwa. (1 Akorinto 6:18) Tidzakana chiwawa ndi kupeŵa kapena kugonjetsa uchidakwa. Ndipo tidzakhala odekha pamene tiputidwa ndi pochita ndi mikhalidwe yovuta. Tiyeni tonsefe—kuphatikizapo ana—tikulitse chipatso cha mzimu chofunika chimenechi.—Salmo 119:1, 2.

LINGALIRO LOYENERA LA UMUTU

6. (a) Kodi makonzedwe okhazikitsidwa ndi Mulungu a umutu ali otani? (b) Kodi mwamuna ayenera kukumbukira chiyani kuti umutu wake ubweretse chimwemwe pabanja?

6 Pulinsipulo lofunika lachiŵiri ndilo kuzindikira umutu. Paulo anafotokoza kakonzedwe koyenera ka zinthu pamene anati: “Ndifuna kuti mudziŵe, kuti mutu wa munthu yense ndiye Kristu; ndi mutu wa mkazi ndiye mwamuna; ndipo mutu wa Kristu ndiye Mulungu.” (1 Akorinto 11:3) Zimenezi zimatanthauza kuti mwamuna amatsogolera m’banja, mkazi wake amakhala wochirikiza wokhulupirika, ndipo ana amamvera makolo awo. (Aefeso 5:22-25, 28-33; 6:1-4) Komabe, dziŵani kuti umutu umadzetsa chimwemwe kokha pamene uchitidwa mwa njira yoyenera. Amuna amene amatsatira kudzipereka kwaumulungu amadziŵa kuti umutu sikupondereza wina. Iwo amatsanzira Yesu, Mutu wawo. Ngakhale kuti Yesu anali kudzakhala “mutu pamtu pa zonse,” iye “sanadza kutumikiridwa koma kutumikira.” (Aefeso 1:22; Mateyu 20:28) Mwamuna wachikristu amachita umutu wake mwa njira imodzimodziyo, osati modzipindulitsa iye yekha, koma kusamalira zofunika za mkazi wake ndi ana ake.—1 Akorinto 13:4, 5.

7. Kodi ndi mapulinsipulo otani a m’Malemba amene adzathandiza mkazi kukwaniritsa ntchito yake yopatsidwa ndi Mulungu m’banja?

7 Mkazi wotsatira kudzipereka kwaumulungu samapikisana kapena kuyesa kulamulira mwamuna wake. Amakondwera kumchirikiza ndi kuthandizana naye. Nthaŵi zina Baibulo limanena mkazi kukhala “wa” mwamuna wake, likumamveketsa bwino kuti mwamuna ndiye mutu. (Genesis 20:3) Mwa ukwati mkazi amakhala pansi pa “lamulo kwa mwamuna wake.” (Aroma 7:2) Panthaŵi imodzimodzi, Baibulo limatcha mkazi “womthangatira.” (Genesis 2:20) Iye amapereka mikhalidwe ndi maluso amene mwamuna wake alibe, ndipo amampatsa chichirikizo chofunikira. (Miyambo 31:10-31) Baibulo limanenanso kuti mkazi ndi “mnzake,” wogwira naye ntchito wa mwamuna wake. (Malaki 2:14) Mapulinsipulo a m’Malemba ameneŵa amathandiza mwamuna ndi mkazi kumvetsetsa malo a wina ndi mnzake ndi kuchitirana ulemu woyenera.

‘KHALANI WOTCHERA KHUTU’

8, 9. Longosolani mapulinsipulo ena amene adzathandiza onse m’banja kukulitsa maluso awo a kulankhulana.

8 M’buku lino kufunika kwa kulankhulana kwagogomezeredwa kaŵirikaŵiri. Chifukwa ninji? Chifukwa chakuti kuthetsa mavuto sikumakhala kovuta kwambiri pamene anthu akambitsirana ndi kumvetserana. Kwagogomezeredwa kaŵirikaŵiri kuti kulankhulana ndi kwa anthu aŵiri. Wophunzira Yakobo ananena motere: “Munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula.”—Yakobo 1:19.

9 Nkofunikanso kusamala ndi mmene timalankhulira. Mawu aukali, amkangano, kapena osuliza kwambiri samapanga kulankhulana kwabwino. (Miyambo 15:1; 21:9; 29:11, 20) Ngakhale pamene zonena zathu zili zoona, ngati tizinena mwa njira yankhanza, monyada, kapena mosalingalira ena, zikhoza kupweteka ena m’malo mwa kuwathandiza. Mawu athu ayenera kukhala abwino, “okoleretsa.” (Akolose 4:6) Mawu athu ayenera kukhala ngati “zipatso zagolidi m’nsengwa zasiliva.” (Miyambo 25:11) Mabanja amene amaphunzira kulankhulana bwino ali pafupi kwambiri kupeza chimwemwe.

NTCHITO YAIKULU YA CHIKONDI

10. Kodi ndi mtundu wotani wa chikondi umene uli wofunika koposa muukwati?

10 Liwu lakuti “chikondi” likupezeka kambiri m’buku lonseli. Kodi mukukumbukira mtundu wa chikondi umene ukunenedwa kwenikweni? Nzoona kuti chikondi cha mwamuna ndi mkazi (Chigiriki, eʹros) nchofunika muukwati, ndipo m’maukwati achipambano, chikondano chozama ndi ubwenzi (Chigiriki, phi·liʹa) zimakula pakati pa mwamuna ndi mkazi. Koma chofunika koposa ndicho chikondi chotchedwa a·gaʹpe m’Chigiriki. Ichi ndicho chikondi chimene tiyenera kukhala nacho kwa Yehova, kwa Yesu, ndi kwa mnansi wathu. (Mateyu 22:37-39) Ndicho chikondi chimene Yehova amasonyeza kwa anthu onse. (Yohane 3:16) Nkwabwino chotani nanga kuti ifenso tikhoza kusonyeza chikondi chimodzimodzicho kwa anzathu a muukwati ndi ana athu!—1 Yohane 4:19.

11. Kodi chikondi chimathandiza motani kukhala ndi ukwati wabwino?

11 Muukwati chikondi cholemekezeka chimenechi chimakhaladi “chomangira cha mtima wamphumphu.” (Akolose 3:14) Chimamanga pamodzi aŵiri okwatirana ndi kuwachititsa kufuna kuchita zabwino koposa kwa wina ndi mnzake ndi kwa ana awo. Pamene mabanja akumana ndi mikhalidwe yovuta, chikondi chimawathandiza kusamalira zinthu mogwirizana. Pamene okwatirana akukula, chikondi chimawathandiza kuchirikizana ndi kupitiriza kumvetsetsana. “Chikondi . . . sichitsata za mwini yekha, . . . chikwirira zinthu zonse, chikhulupirira zinthu zonse, chiyembekeza zinthu zonse, chipirira zinthu zonse. Chikondi sichitha nthaŵi zonse.”—1 Akorinto 13:4-8.

12. Kodi nchifukwa ninji kukonda Mulungu kumachititsa okwatirana kulimbitsa ukwati wawo?

12 Umodzi wa ukwati umakhala wolimba makamaka pamene umangidwa, osati ndi chikondi cha pakati pa okwatiranawo chokha, koma kwenikweni ndi chikondi chawo kwa Yehova. (Mlaliki 4:9-12) Chifukwa ninji? Chabwino, mtumwi Yohane analemba kuti: “Ichi ndi chikondi cha Mulungu, kuti tisunge malamulo ake.” (1 Yohane 5:3) Chotero, okwatirana ayenera kuphunzitsa ana awo kudzipereka kwaumulungu osati chabe chifukwa chakuti amakonda kwambiri ana awo koma chifukwa chakuti Yehova amalamula zimenezi. (Deuteronomo 6:6, 7) Ayenera kupeŵa chisembwere osati chabe chifukwa chakuti amakondana koma makamaka chifukwa amakonda Yehova, amene ‘adzaweruza adama ndi achigololo.’ (Ahebri 13:4) Ngakhale ngati wina wa okwatirana achititsa mavuto aakulu muukwati, chikondi cha pa Yehova chidzasonkhezera winayo kutsatirabe mapulinsipulo a Baibulo. Ndithudi, alidi achimwemwe mabanja amene chikondi chawo kwa wina ndi mnzake nchomangidwa ndi chikondi kwa Yehova!

BANJA LIMENE LIMACHITA CHIFUNIRO CHA MULUNGU

13. Kodi kukhala wofunitsitsa kuchita chifuniro cha Mulungu kudzathandiza motani anthu kusumika maso pa zinthu zofunika kwenikweni?

13 Moyo wonse wa Mkristu wazikidwa pa kuchita chifuniro cha Mulungu. (Salmo 143:10) Ichi nchimene kudzipereka kwaumulungu kumatanthauza kwenikweni. Kuchita chifuniro cha Mulungu kumathandiza mabanja kusumika maso pa zinthu zofunika kwenikweni. (Afilipi 1:9, 10, NW) Mwachitsanzo, Yesu anachenjeza kuti: “Ndinadza kusiyanitsa munthu ndi atate wake, ndi mwana wamkazi ndi amake, ndi mkazi wokwatiwa ndi mpongozi wake: ndipo apabanja ake a munthu adzakhala adani ake.” (Mateyu 10:35, 36) Mogwirizana ndi chenjezo la Yesu, otsatira ake ambiri azunzidwa ndi apabanja pawo enieniwo. Nzachisoni ndi zopweteka chotani nanga! Komabe, maunansi a banja sayenera kupambana chikondi chathu kwa Yehova Mulungu ndi Yesu Kristu. (Mateyu 10:37-39) Ngati munthu apirira mosasamala kanthu za chitsutso cha banja, otsutsawo angasinthe pamene aona zipatso zabwino za kudzipereka kwaumulungu. (1 Akorinto 7:12-16; 1 Petro 3:1, 2) Ngakhale ngati zimenezo sizichitika, palibe ubwino wokhalitsa umene umapezeka mwa kuleka kutumikira Mulungu chifukwa cha chitsutso.

14. Kodi chikhumbo cha kuchita chifuniro cha Mulungu chidzathandiza motani makolo kupindulitsa ana awo?

14 Kuchita chifuniro cha Mulungu kumathandiza makolo kupanga zosankha zoyenera. Mwachitsanzo, m’malo ena anthu amakonda kuona ana monga chuma choikizira, ndipo amadalira ana awo kuti adzawasunge akakalamba. Pamene kuli kwakuti nkwabwino ndi koyenera kwa ana kusamalira makolo awo okalamba, malingaliro amenewo sayenera kuchititsa makolo kulimbikitsa ana awo kukhala ndi moyo wokondetsa chuma. Makolo samathandiza ana awo ngati awaphunzitsa kukonda chuma kuposa zinthu zauzimu.—1 Timoteo 6:9.

15. Kodi ndi motani mmene Yunike, amake Timoteo, analili chitsanzo chabwino koposa cha kholo limene linachita chifuniro cha Mulungu?

15 Chitsanzo chabwino pa zimenezi ndicho cha Yunike, mayi wake wa Timoteo, bwenzi lachichepere la Paulo. (2 Timoteo 1:5) Ngakhale kuti iye anakwatiwa kwa munthu wosakhulupirira, Yunike, limodzi ndi Loisi, gogo wake wa Timoteo, anaphunzitsa bwino lomwe Timoteo kulondola kudzipereka kwaumulungu. (2 Timoteo 3:14, 15) Timoteo atakula, Yunike anamlola kuchoka panyumba ndi kuyamba ntchito yolalikira Ufumu monga mmishonale mnzake wa Paulo. (Machitidwe 16:1-5) Ayenera kukhala atakondwera chotani nanga kuona mwana wake akukhala mmishonale wokangalika! Kudzipereka kwake kwaumulungu monga munthu wachikulire kunasonyeza kuphunzitsidwa kwabwino kumene analandira paubwana. Ndithudi, Yunike anapeza chikhutiro ndi chisangalalo pakumva malipoti a utumiki wokhulupirika wa Timoteo, ngakhale kuti mwinamwake analakalaka kukhala naye pafupi.—Afilipi 2:19, 20.

BANJA NDI MTSOGOLO MWANU

16. Monga mwana, kodi ndi nkhaŵa yoyenera yotani imene Yesu anasonyeza, koma kodi cholinga chake chachikulu chinali chotani?

16 Yesu analeredwa m’banja laumulungu, ndipo monga munthu wachikulire, anasonyeza nkhaŵa yoyenera ya mwana kwa amake. (Luka 2:51, 52; Yohane 19:26) Komabe, cholinga chachikulu cha Yesu chinali kuchita chifuniro cha Mulungu, ndipo kwa iye zimenezi zinaphatikizapo kutsegulira anthu njira ya ku moyo wosatha. Anachita zimenezi pamene anapereka moyo wake wangwiro waumunthu monga dipo kaamba ka anthu ochimwa.—Marko 10:45; Yohane 5:28, 29.

17. Kodi ndi ziyembekezo zaulemerero zotani zimene njira ya moyo yokhulupirika ya Yesu inatsegulira awo ochita chifuniro cha Mulungu?

17 Yesu atamwalira, Yehova anamuukitsira ku moyo wakumwamba ndi kumpatsa ulamuliro waukulu, potsirizira pake akumamukhazika monga Mfumu ya Ufumu wakumwamba. (Mateyu 28:18; Aroma 14:9; Chivumbulutso 11:15) Nsembe ya Yesu inatheketsa anthu ena kusankhidwa kuti akalamulire pamodzi naye mu Ufumuwo. Inatseguliranso njira anthu onse owongoka mtima kudzasangalala ndi moyo wangwiro padziko lapansi lobwezeretsedwa ku mikhalidwe yaparadaiso. (Chivumbulutso 5:9, 10; 14:1, 4; 21:3-5; 22:1-4) Umodzi wa mwaŵi waukulu koposa umene tili nawo lero ndiwo wa kulalikira uthenga wabwino waulemerero umenewu kwa anansi athu.—Mateyu 24:14.

18. Kodi ndi chikumbutso ndi chilimbikitso chotani chimene chikuperekedwa ku mabanja ndi kwa anthu ena?

18 Monga momwe mtumwi Paulo anasonyezera, kukhala ndi moyo wa kudzipereka kwaumulungu kuli ndi lonjezo lakuti anthu akhoza kupeza madalitso amenewo mu moyo “ulinkudza.” Ndithudi, imeneyi ndiyo njira yabwino koposa yopezera chimwemwe! Kumbukirani, “dziko lapansi lipita, ndi chilakolako chake; koma iye amene achita chifuniro cha Mulungu akhala ku nthaŵi zonse.” (1 Yohane 2:17) Chifukwa chake, kaya ndinu mwana kapena kholo, mwamuna kapena mkazi, kapena ndinu wachikulire wosakwatira wokhala ndi ana kapena wopanda ana, yesetsani kuchita chifuniro cha Mulungu. Ngakhale pamene muli wopanikizika kapena kuyang’anizana ndi mavuto aakulu, musaiŵale kuti ndinu mtumiki wa Mulungu wamoyo. Motero, lolani kuti machitidwe anu akondweretse Yehova. (Miyambo 27:11) Ndipo lolani kuti mayendedwe anu akupatseni chimwemwe tsopano ndi moyo wosatha m’dziko latsopano likudzalo!

KODI MAPULINSIPULO A BAIBULO AŴA ANGATHANDIZE MOTANI . . . BANJA LANU KUKHALA LACHIMWEMWE?

Tikhoza kukulitsa kudziletsa.—Agalatiya 5:22, 23.

Ndi lingaliro loyenera la umutu, onse aŵiri mwamuna ndi mkazi amayesa kupezera banja zabwino koposa.—Aefeso 5:22-25, 28-33; 6:4.

Kulankhulana kumaphatikizapo kutchera khutu.—Yakobo 1:19.

Chikondi kwa Yehova chidzalimbitsa ukwati.—1 Yohane 5:3.

Kuchita chifuniro cha Mulungu ndiko cholinga chachikulu cha banja.—Salmo 143:10; 1 Timoteo 4:8.

MPHATSO YA UMBETA

Si munthu aliyense amene amakwatira kapena kukwatiwa. Ndipo si okwatirana onse amene amasankha kukhala ndi ana. Yesu anali mbeta, ndipo ananena kuti umbeta ndi mphatso pamene ukhalapo “chifukwa cha Ufumu wakumwamba.” (Mateyu 19:11, 12) Mtumwi Paulonso anasankha kusakwatira. Ananena za umbeta ndi ukwati womwe kukhala “mphatso.” (1 Akorinto 7:7, 8, 25-28) Chifukwa chake, pamene kuli kwakuti buku lino lafotokoza kwambiri nkhani zokhudza ukwati ndi kulera ana, tisaiŵale za madalitso ndi mfupo zothekera za kukhala mbeta kapena kukwatira koma popanda ana.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena