-
Yehova Ali Wololera!Nsanja ya Olonda—1994 | August 1
-
-
Kulolera, Chizindikiro cha Nzeru Yaumulungu
6. Kodi ndi tanthauzo lenileni lotani ndi malingaliro ena a liwu Lachigiriki limene Yakobo anagwiritsira ntchito polongosola nzeru yaumulungu?
6 Wophunzira Yakobo anagwiritsira ntchito liwu lokondweretsa polongosola nzeru ya Mulungu ameneyu wokhoza kusintha kwambiri. Iye analemba kuti: “Nzeru yochokera kumwamba ili . . . yololera.” (Yakobo 3:17, NW) Liwu Lachigiriki limene anagwiritsira ntchito pano lakuti (e·pi·ei·kesʹ) nlovuta kutembenuza. Otembenuza agwiritsira ntchito mawu onga “kufatsa,” “kuchitira chifundo,” “kudziletsa,” ndi “kulingalira ena.” New World Translation imalimasulira kuti “kulolera,” ndi mawu amtsinde osonyeza kuti tanthauzo lenileni ndilo “kugonja.”a Liwulo limaperekanso lingaliro la kusaumirira pa mawu a lamulo, kusakhala wokhwima mosayenerera kapena kuuma khosi. Katswiri wotchedwa William Barclay akunena kuti mu New Testament Words: “Chinthu chachikulu ndi chofunikira ponena za epieikeia nchakuti lili ndi magwero ake kwa Mulungu. Ngati Mulungu akadaumirira pa miyezo yake, ngati Mulungu akadagwiritsira ntchito pa ife miyezo yokhwima ya lamulo, kodi zikanatikhalira motani? Mulungu ali chitsanzo chopambana cha munthu amene ali wa epieikēs ndi amenenso amachitira ena mwa epieikeia.”
7. Kodi ndimotani mmene Yehova anasonyezera kulolera m’munda wa Edene?
7 Talingalirani za nthaŵi pamene mtundu wa anthu unapandukira uchifumu wa Yehova. Kukanakhala kosavuta chotani nanga kwa Mulungu kupha apandu osayamikira atatuwo, Adamu, Hava, ndi Satana! Ndi kupwetekedwa mtima kwakukulu kotani nanga kwamtsogolo kumene iye akanakupeŵa! Ndipo kodi ndani yemwe akadatsutsa kuti iye analibe kuyenera kwa kuweruza ndi chilungamo chokhwima choterocho? Komabe, Yehova samapanikizira gulu lake longa galeta lakumwambalo kuyenda pa muyezo wokhwima, wosasinthika wa chilungamo. Motero galeta limenelo silinangopitirira ndi kukagunda banja la anthu ndi ziyembekezo zonse za mtsogolo mwa chimwemwe mwa mtundu wa anthu. Mmalomwake, Yehova anayendetsa galeta lakelo pa liŵiro la mphezi. Mwamsanga pambuyo pa chipandukocho, Yehova Mulungu analinganiza chifuno chofika patali chimene chinapereka chifundo ndi chiyembekezo ku mbadwa zonse za Adamu.—Genesis 3:15.
8. (a) Kodi ndimotani mmene lingaliro lolakwa la Dziko Lachikristu limasiyanira ndi kulolera kolungama kwa Yehova? (b) Kodi nchifukwa ninji tinganene kuti kulolera kwa Yehova sikumatanthauza kuti iye angalolere molakwa miyezo yake yaumulungu?
8 Komabe, kulolera kwa Yehova sikumatanthauza kuti iye angalolere molakwa malamulo a mkhalidwe aumulungu. Matchalitchi a lerolino a Dziko Lachikristu angalingalire kuti akukhala ololera pamene akunyalanyaza makhalidwe oipa kaamba kofuna kupeza chiyanjo kwa nkhosa zawo zopanduka. (Yerekezerani ndi 2 Timoteo 4:3.) Yehova samaswa malamulo a iye mwini, ndiponso samalolera molakwa malamulo ake a mkhalidwe. Mmalomwake, amasonyeza kufunitsitsa kwa kugonja, kusinthira ku mikhalidwe, kotero kuti malamulo a mkhalidwe amenewo angagwiritsiridwe ntchito ponse paŵiri mwachilungamo ndi mwachifundo. Iye nthaŵi zonse amakumbukira kuchita chilungamo ndi mphamvu molinganiza ndi chikondi ndi nzeru yake yololera. Tiyeni tipende njira zitatu zimene Yehova amasonyezera kulolera.
“Wofunitsitsa Kukhululukira”
9, 10. (a) Kodi kukhala “wofunitsitsa kukhululukira” nkogwirizana motani ndi kulolera? (b) Kodi ndimotani mmene Davide anapindulira ndi kufunitsitsa kukhululukira kwa Yehova, ndipo chifukwa ninji?
9 Davide analemba kuti: “Pakuti Inu, Ambuye, ndinu wabwino, ndi [wofunitsitsa kukhululukira, NW], ndi wa chifundo chochulukira onse akuitana Inu.” (Salmo 86:5) Pamene Malemba Achihebri ankatembenuzidwa m’Chigiriki, liwu lotanthauza “wofunitsitsa kukhululukira” linatembenuzidwa kukhala e·pi·ei·kesʹ, kapena “kulolera.” Ndithudi, kukhala wofunitsitsa kukhululukira ndi kusonyeza chifundo ndiko mwinamwake njira yofunika koposa yosonyezera kulolera.
10 Davide mwiniyo anadziŵa bwino lomwe za kulolera kwa Yehova m’nkhani imeneyi. Pamene Davide anachita chigololo ndi Bateseba ndi kulinganiza kuti mwamuna wake aphedwe, onse aŵiri iye ndi Bateseba anayenera chilango cha imfa. (Deuteronomo 22:22; 2 Samueli 11:2-27) Ngati kuti oweruza aumunthu ouma khosi ndiwo akanaweruza mlanduwo, onse aŵiriwo akadataya miyoyo yawo. Koma Yehova anasonyeza kulolera (e·pi·ei·kes), kumene, malinga ndi kunena kwa Vine’s Expository Dictionary of Biblical Words, “kumasonyeza kulingalira ena kumene kumayang’ana ‘mwachifundo ndi mololera pa zifukwa za mlanduwo.’” Zifukwa zimene zinasonkhezera chiweruzo chachifundo cha Yehova mwachionekere zinaphatikizapo kulapa koona mtima kwa olakwawo ndi chifundo chimene Davide iye mwini anali atasonyeza kwa ena. (1 Samueli 24:4-6; 25:32-35; 26:7-11; Mateyu 5:7; Yakobo 2:13) Komabe, molingana ndi kudzilongosola kwa Yehova pa Eksodo 34:4-7, kunali kulolera pamene Yehova anawongolera Davide. Iye anatumiza mneneri Natani kwa Davide ndi uthenga wamphamvu, akumagogomezera kwa Davide mfundo yakuti iye anali atanyoza mawu a Yehova. Davide analapa ndipo motero sanafe pa tchimo lakelo.—2 Samueli 12:1-14.
-
-
Yehova Ali Wololera!Nsanja ya Olonda—1994 | August 1
-
-
a Kalelo mu 1769, wolemba dikishonale John Parkhurst anatanthauzira liwulo kukhala “kugonja, maganizo ogonja, kufatsa, kudekha, kuleza mtima.” Akatswiri ena aperekanso “kugonja” kukhala tanthauzo lake.
-