-
Kodi Mulungu Amafuna Kuti Tiziulula Ndiponso Kulapa Machimo Athu?Nsanja ya Olonda—2010 | September 1
-
-
M’buku la Yakobe mulinso mawu olimbikitsa akuti: “Kodi pali wina amene akudwala [mwauzimu] pakati panu? Aitane akulu a mpingo, ndipo iwo am’pempherere, am’pake mafuta m’dzina la Yehova. Ndipo pemphero la chikhulupiriro lidzachiritsa wodwalayo, ndipo Yehova adzamuutsa. Ndiponso ngati anachita machimo, iye adzakhululukidwa.”—Yakobe 5:14, 15.
-
-
Kodi Mulungu Amafuna Kuti Tiziulula Ndiponso Kulapa Machimo Athu?Nsanja ya Olonda—2010 | September 1
-
-
Choyamba, ayenera ‘kum’paka mafuta.’ Mafuta amenewa akutanthauza mphamvu yochiritsa ya Mawu a Mulungu. Mtumwi Paulo anafotokoza kuti “mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. . . . Amathanso kuzindikira malingaliro ndi zolinga za mtima,” kutanthauza kuti amalowerera m’maganizo ndi mu mtima mwa munthu. (Aheberi 4:12) Akulu amagwiritsa ntchito Baibulo mwaluso kuthandiza munthu wodwala mwauzimuyo kuona chimene chinachititsa kuti achite tchimo. Amamuthandizanso kudziwa zimene ayenera kuchita kuti akonze zimene analakwitsazo n’kuyamba kuchita zimene Mulungu amafuna.
-