Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kodi Mulungu Amafuna Kuti Tiziulula Ndiponso Kulapa Machimo Athu?
    Nsanja ya Olonda—2010 | September 1
    • M’buku la Yakobe mulinso mawu olimbikitsa akuti: “Kodi pali wina amene akudwala [mwauzimu] pakati panu? Aitane akulu a mpingo, ndipo iwo am’pempherere, am’pake mafuta m’dzina la Yehova. Ndipo pemphero la chikhulupiriro lidzachiritsa wodwalayo, ndipo Yehova adzamuutsa. Ndiponso ngati anachita machimo, iye adzakhululukidwa.”​—Yakobe 5:14, 15.

  • Kodi Mulungu Amafuna Kuti Tiziulula Ndiponso Kulapa Machimo Athu?
    Nsanja ya Olonda—2010 | September 1
    • Choyamba, ayenera ‘kum’paka mafuta.’ Mafuta amenewa akutanthauza mphamvu yochiritsa ya Mawu a Mulungu. Mtumwi Paulo anafotokoza kuti “mawu a Mulungu ndi amoyo ndi amphamvu. . . . Amathanso kuzindikira malingaliro ndi zolinga za mtima,” kutanthauza kuti amalowerera m’maganizo ndi mu mtima mwa munthu. (Aheberi 4:12) Akulu amagwiritsa ntchito Baibulo mwaluso kuthandiza munthu wodwala mwauzimuyo kuona chimene chinachititsa kuti achite tchimo. Amamuthandizanso kudziwa zimene ayenera kuchita kuti akonze zimene analakwitsazo n’kuyamba kuchita zimene Mulungu amafuna.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena