Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • “Anagwidwa ndi Chifundo”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
    • Mlongo akulimbikitsa mlongo mnzake.

      “Muzimverana chisoni”

      7. N’chiyani chingatithandize kuti tizimvera ena chisoni, nanga tingasonyeze bwanji zimenezi?

      7 Monga Akhristu tikulimbikitsidwa kuti tizimvera ena chifundo ngati mmene Yesu ankachitira. Baibulo limatilimbikitsa kuti ‘tizimverana chisoni.’b (1 Petulo 3:8) Zingakhale zovuta kuti timvetse mavuto ndiponso ululu wa anthu amene akudwala matenda aakulu kapena amene akuvutika maganizo, makamaka ngati ifeyo sitinakumanepo ndi mavuto ngati amenewo. Koma kumbukirani kuti sizidalira kuti tikumane ndi mavuto amene mnzathu akukumana nawo kuti timvetse mmene akuvutikira. Mwachitsanzo, Yesu ankamvetsa mmene odwala akuvutikira ngakhale kuti iyeyo sanadwalepo. Nanga tingatani kuti tizimvetsa mavuto amene anthu akukumana nawo? Anthu amene akuvutikawo akamatiuza mavuto awo tizimvetsera modekha ndiponso tiziyerekezera kuti nafenso tili ndi mavuto ngati awowo. Tingachite bwino kudzifunsa kuti, ‘Kodi ineyo ndikanamva bwanji ndikanakhala kuti ndakumana ndi mavuto ngati amenewa?’ (1 Akorinto 12:26) Ena akamavutika, tiziyesetsa kuwamvera chisoni mwamsanga, tikatero tidzatha ‘kulankhula molimbikitsa anthu amene ali ndi nkhawa.’ (1 Atesalonika 5:14) Nthawi zina tingagwetse misozi posonyeza kuti tili ndi chisoni chifukwa cha mavuto amene mnzathu akukumana nawo, osati kungomuuza kuti nafenso zatikhudza. N’chifukwa chake Baibulo limati: “Muzilira ndi anthu amene akulira.”​—Aroma 12:15.

  • “Anagwidwa ndi Chifundo”
    ‘Bwera Ukhale Wotsatira Wanga’
    • b Mawu a Chigiriki amene anawamasulira kuti ‘tizimverana chisoni,’ kwenikweni amatanthauza kuti “tizivutikira limodzi.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena