-
“Koposa Zonse Mukhale Nacho Chikondano Chenicheni”Dikirani!
-
-
“Koposa Zonse Mukhale Nacho Chikondano Chenicheni”
“Chitsiriziro cha zinthu zonse chili pafupi; . . . koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha.”—1 PETRO 4:7, 8.
YESU ankadziŵa kuti maola ake omaliza kukhala limodzi ndi atumwi ake anali amtengo wapatali. Ankadziŵa zimene zidzawachitikire m’tsogolo. Ophunzirawo anali ndi ntchito yaikulu yofunika kuchita, koma Yesu anadziŵa kuti adzadedwa ndi kuzunzidwa monga momwe zinachitikira kwa iye. (Yohane 15:18-20) Usiku womaliza kukhala nawo limodzi umenewo, Yesu anawakumbutsa maulendo angapo kufunika ‘kokondana wina ndi mnzake.’—Yohane 13:34, 35; 15:12, 13, 17.
2 Mtumwi Petro, amene analipo usiku umenewo, anamvetsa mfundo imeneyo. Patapita zaka zingapo, pamene Petro analemba kalata Yerusalemu atatsala pang’ono kuwonongedwa, anagogomezera kufunika kwa chikondi. Analangiza Akristu kuti: “Chitsiriziro cha zinthu zonse chili pafupi; . . . koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha.” (1 Petro 4:7, 8) Mawu a Petro ali ndi tanthauzo lalikulu kwa anthu amene akukhala mu “masiku otsiriza” a dongosolo la zinthu lilipoli. (2 Timoteo 3:1) Kodi “chikondano chenicheni” n’chiyani? N’chifukwa chiyani tifunika kukhala ndi chikondi choterocho pa ena? Ndipo tingasonyeze bwanji kuti tili nachodi?
Kodi “Chikondano Chenicheni” N’chiyani?
3 Anthu ambiri amaganiza kuti chikondi ndi chinthu chimene chiyenera kungobwera chokha popanda munthu kuchitapo kalikonse. Koma Petro sankanena za chikondi wamba. Ankanena za mtundu wapamwamba kwambiri wa chikondi. Liwu lakuti “chikondano” lopezeka pa 1 Petro 4:8 analimasulira kuchokera ku liwu lachigiriki lakuti a·gaʹpe. Liwu limenelo limatanthauza chikondi chopanda dyera chimene munthu amachisonyeza chifukwa chotsatira, kapena kulamulidwa ndi mfundo zinazake. Buku lina linati: “Chikondi cha agape chimatheka kuchilamulira chifukwa sichitengera kwenikweni mmene munthu akumvera mumtima koma munthu amatha kudziuza kuti achite chinachake.” Chifukwa chakuti tinabadwa ndi chizoloŵezi chodzikonda, timafunikira kutikumbutsa kuti tizikondana, ndi kuti tizichita zimenezi motsatira mfundo za Mulungu.—Genesis 8:21; Aroma 5:12.
4 Zimenezi sizikutanthauza kuti tiyenera kukondana chifukwa chakuti tifunika kutero basi. Sikuti munthu akamasonyeza chikondi cha a·gaʹpe sakhala waubwenzi kapena sasonyeza mmene akumvera. Petro anati ‘tikhale nacho chikondano chenicheni [“chotambasuka,” Kingdom Interlinear] mwa ife tokha.’a Komabe, kukhala ndi chikondi choterocho kumafuna kuchitapo kanthu. Ponena za mawu achigiriki amene anawamasulira kuti “chenicheni,” katswiri wina anati: “Amapereka chithunzi cha munthu amene akuthamanga amene akutambasula miyendo yake kwambiri kufika pomaliza mphamvu zake zonse pamapeto pa mpikisano.”
5 Choncho chikondi chathu sichiyenera kutichititsa zinthu zosavuta kuchita zokha, ndiponso sitiyenera kuchisonyeza kwa anthu ochepa chabe. Chikondi chachikristu chimafuna kuti ‘titambasule’ mtima wathu, tisonyeze chikondi ngakhale pamene zingakhale zovuta kutero. Mwachionekere, chikondi choterocho tiyenera kuyesetsa kuti tikhale nacho ndiponso kuti tipitirize kukhala nacho, monga momwe munthu wothamanga pa mpikisano amayenera kuphunzira ndiponso kunola luso lake. M’pofunika kwambiri kuti tikhale ndi chikondi choterocho pa wina ndi mnzake. Chifukwa chiyani? Tiyeni tionepo zifukwa zitatu.
-
-
“Koposa Zonse Mukhale Nacho Chikondano Chenicheni”Dikirani!
-
-
7 Chachiŵiri, m’pofunika kwambiri kukondana makamaka masiku ano kuti tizitha kuthandiza abale athu amene akufunika thandizo, chifukwa chakuti “chitsiriziro cha zinthu zonse chili pafupi.” (1 Petro 4:7) Tikukhala mu “nthaŵi zoŵaŵitsa.” (2 Timoteo 3:1) Zochitika padziko lapansi, masoka achilengedwe, ndi kutsutsidwa kumatibweretsera mavuto. Pa nthaŵi zovuta, timafunika kuyandikana kwambiri ndi anzathu. Chikondi chenicheni chidzatigwirizanitsa pamodzi ndi kutilimbikitsa ‘kusamalana wina ndi mnzake.’—1 Akorinto 12:25, 26.
8 Chachitatu, tiyenera kukondana chifukwa sitikufuna ‘kupatsa malo Mdyerekezi’ kuti atipezerere. (Aefeso 4:27) Satana sachedwa kugwiritsira ntchito kupanda ungwiro kwa okhulupirira anzathu, monga zofooka zawo ndi zolakwa zawo, kuti atikhumudwitse. Kodi mawu osaganizira bwino amene wokhulupirira mnzathu wanena kapena zochita zake zosaganizira ena zidzatichititsa kudzipatula ku mpingo? (Miyambo 12:18) Sizidzatero ngati tili ndi chikondi chenicheni! Chikondi choterocho chimatithandiza kukhala pamtendere ndi kutumikira Mulungu mogwirizana ndiponso “ndi mtima umodzi.”—Zefaniya 3:9.
-
-
“Koposa Zonse Mukhale Nacho Chikondano Chenicheni”Dikirani!
-
-
13 Chikondi chimatithandiza kunyalanyaza zolakwa za ena. Kumbukirani kuti pamene Petro ankalimbikitsa anthu amene anawalembera kalata yake ‘kukhala ndi chikondano chenicheni mwa iwo okha,’ anapereka chifukwa chimene kuchita zimenezi kulili kofunika kwambiri. Iye anati: “Pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo.” (1 Petro 4:8) ‘Kukwirira’ machimo sikutanthauza kubisa machimo aakulu. Machimo oterowo amayenera kukanenedwa kwa anthu a udindo mu mpingo ndipo amachitapo kanthu. (Levitiko 5:1; Miyambo 29:24) Kungakhale kupanda chikondi ndiponso kusemphana ndi Malemba kulola kuti anthu amene akuchita machimo aakulu apitirizebe kupweteka anthu ena osalakwa.—1 Akorinto 5:9-13.
14 Nthaŵi zambiri, zolakwa za okhulupirira anzathu zimakhala zazing’ono. Tonsefe timalakwa m’mawu ndi m’zochita zathu nthaŵi ndi nthaŵi, ndipo timakhumudwitsana kapena kukwiyitsana. (Yakobo 3:2) Kodi tizifulumira kufalitsa zolakwa za ena? Kuchita zimenezo kungangoyambitsa mikangano mu mpingo. (Aefeso 4:1-3) Ngati timachita zinthu mwachikondi, ‘sitidzaneneza’ kapena kuti, kufalitsa, zolakwa za wokhulupirira mnzathu. (Salmo 50:20) Monga momwe pulasitala ndi penti zimabisira kunyansa kwa khoma, chikondi chimabisa zolakwa za ena.—Miyambo 17:9.
-
-
“Koposa Zonse Mukhale Nacho Chikondano Chenicheni”Dikirani!
-
-
a Pa 1 Petro 4:8, mabaibulo ena amanena kuti tizikondana “moonadi,” “mwakuya,” kapena “moona mtima.”
-