-
“Abusa Amene Mtima Wanga Wakonda”Zimene Mulungu Akutiuza Kudzera mwa Yeremiya
-
-
4. Kodi ndani akusamalira nkhosa za Mulungu masiku ano, ndipo amasonyeza mtima wotani pochita zimenezi?
4 Lonjezo la Mulungu limeneli linakwaniritsidwa kwambiri kudzera mwa Yesu, yemwe ndi M’busa Wamkulu wa nkhosa za Yehova, ndipo anadzakhala Mutu wa mpingo wachikhristu. Yesu ananena kuti iye ndi “m’busa wabwino,” amene amamveradi chifundo anthu amene akuwatsogolera. (Yoh. 10:11-15) Masiku ano Yehova akugwiritsa ntchito abusa aang’ono, kuti azisamalira nkhosa zake padziko lapansi. Ena mwa abusa amenewa ndi abale odzozedwa amene ali m’gulu la kapolo wokhulupirika ndi wanzeru ndipo ena ndi akulu a m’gulu la “khamu lalikulu,” amene amagwira ntchito yawo mokhulupirika. (Chiv. 7:9) Abusa amenewa amayesetsa kusonyeza mtima wololera kuvutikira ena potengera chitsanzo cha Yesu. Iwo amatsanzira Khristu poyesetsa kudyetsa ndi kusamalira mpingo. Ndipotu m’busa aliyense amene amanyalanyaza kapena kupondereza abale komanso kuwachitira nkhanza kapena chipongwe, adzakumana ndi tsoka. (Mat. 20:25-27; 1 Pet. 5:2, 3) Kodi Yehova amafuna kuti abusa achikhristu azichita chiyani masiku ano? Kodi tikawerenga zimene Yeremiya analemba tikuphunzira kuti akulu ayenera kukhala ndi makhalidwe komanso zolinga zotani akamagwira ntchito yawo? Tsopano tiyeni tikambirane udindo umene akulu ali nawo wothandiza ndi kuteteza abale, kuphunzitsa mumpingo komanso mu utumiki, ndiponso kuweruza.
-
-
“Abusa Amene Mtima Wanga Wakonda”Zimene Mulungu Akutiuza Kudzera mwa Yeremiya
-
-
6 Mofanana ndi abusa a nkhosa zenizeni, oyang’anira achikhristu sayenera kunyalanyaza udindo wawo wosamalira mpingo. Ngati ndinu mkulu, kodi mumakhala tcheru kuti muone zizindikiro zilizonse zosonyeza kuti abale anu akuvutika, ndipo kodi mumakhala wofunitsitsa kuwathandiza mwamsanga? Mfumu yanzeru Solomo inalemba kuti: “Uyenera kudziwa bwino maonekedwe a ziweto zako. Ika mtima wako pa magulu a ziweto zako.” (Miy. 27:23) Lemba limeneli likusonyeza kuti abusa a nkhosa zenizeni amakhala akhama, ndipo izi n’zimenenso abusa auzimu mumpingo ayenera kuchita posamalira nkhosa za Mulungu. Ngati ndinu mkulu, kodi mukuyesetsa mwakhama kupewa mtima wofuna kulamulira ena? Mfundo yakuti Petulo ananena za ‘kuchita ufumu pa anthu amene ali cholowa chochokera kwa Mulungu,’ ikusonyeza kuti n’zotheka ndithu kuti mkulu achite zimenezi. Ndiyeno kodi mungathandize bwanji kuti zimene zalembedwa pa Yeremiya 33:12 zitheke? (Werengani.) Makolo amene akulera okha ana, akazi amasiye, mabanja amene ali ndi ana opeza, komanso anthu achikulire ndi achinyamata, angafunike kuwasamalira ndi kuwathandiza mwapadera.
-