-
Pitirizanibe Kukhala Ndimoyo Monga Ana a MulunguNsanja ya Olonda—1987
-
-
9. Kodi ndim’lingaliro lotani m’limene Mkristu wobadwa ndi mzimu sangakhalire ndi “chizolowezi cha kuchita uchimo,” ndipo nchifukwa ninjiizi ziri choncho?
9 Kenako Yohane akulekanitsa pakati pa ana a Mulungu ndi a Mdyerekezi. (Werengani 1 Yohane 3:9-12.) Aliyense “wobadwa kuchokera mwa Mulungu sachita tchimo,” kapena kuuzolowera. “Mbewu ya Yehova,” kapena “mzimu woyera umene umapatsa munthuyo “kubadwa kwatsopano” ku chiyembekezo cha kumwamba, umakhalabe mwa munthuyo kusiyapo ngati awukaniza ndipo motero ‘kuumvetsa chisoni’ mzimuwo, kotero kuti Mulungu amauchotsa. (1 Petro 1:3, 4, 18, 19, 23; Aefeso 4:30) Kupitirizabe kukhala mmodzi wa ana a Mulungu, Mkristu wodzozedwa ndi Mulungu ‘sakhoza kuchimwa mwachizolowezi.’ Monga ‘cholengedwa chatsopano’ chokhala ndi “umunthu watsopano,” iye amayesayesa kutsutsana ndi uchimo. Iye ‘wawonjoka ku chivundi cha m’dzikoli napyola chilakolako,’ ndipo iye saali wochimwa wozolowera mu mtima mwake.—2 Akorinto 5:16, 17; Akolose 3: 5-11; 2 Petro 1:4.
-
-
Pitirizanibe Kukhala Ndimoyo Monga Ana a MulunguNsanja ya Olonda—1987
-
-
11. (a) Kodi ndiiti imene iri njira ina yodziwira awo amene saali ana a Mulungu? (b) Kusinkhasinkha panjira ya Kaini kuyenera kutisonkhezera kuchitanji?
11 Ndiponso, iye wosakonda mbale wake [sachokera kwa Mulungu].” Kwenikweni, “uthenga” umene taumva “kuyambira pachiyambi” pa miyoyo yathu monga Mboni za Yehova ngwakuti “tikondane wina ndi mnzake.” (Yohane 13:34) Chotero ife sitiri “monga Kaini,”amene anasonyeza kuti anali “wochokera kwa woipayo” mwa ‘kupha mbale wake’ mwa mkhalidwe wachiwawa wa kuchita mbanda wa Satana. (Genesis 4:2-10; Yohane 8:44) Kaini anapha Abele “popeza ntchito zake zinali zoipa, ndi za mbale wake zolungama.” Ndithudi, kusinkhasinkha panjira ya Kaini kuyenera kutisonkhezera kupewa udani wofananawo pa abale athu auzimu.
-