Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Muziyamikira Zimene Yehova Ndi Yesu Anakuchitirani
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 3. Zimene tingachite posonyeza kuyamikira

      Tiyerekeze kuti munthu wina anakupulumutsani pamene munkamira m’madzi. Kodi mungangozinyalanyaza n’kuiwala zimene munthuyo anakuchitirani? Kapena mungayesetse kuchita zinthu zosonyeza kumuyamikira?

      Tidzapeza moyo wosatha chifukwa chakuti Yehova anatikomera mtima. Werengani 1 Yohane 4:8-10, kenako mukambirane mafunso awa:

      • N’chifukwa chiyani tikunena kuti nsembe ya Yesu ndi mphatso yapadera?

      • Kodi inuyo mukumva bwanji mukaganizira zimene Yehova ndi Yesu anakuchitirani?

      Tingasonyeze bwanji kuti timayamikira zimene Yehova ndi Yesu anatichitira? Werengani 2 Akorinto 5:15 ndi 1 Yohane 4:11; 5:3. Pambuyo powerenga lemba lililonse mukambirane funso ili:

      • Malinga ndi lembali, kodi tingasonyeze bwanji kuyamikira?

  • N’chifukwa Chiyani Muyenera Kudzipereka Ndiponso Kubatizidwa?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
    • 1. N’chiyani chimachititsa munthu kuti adzipereke kwa Yehova?

      Timadzipereka kwa Yehova chifukwa chakuti timamukonda kwambiri. (1 Yohane 4:10, 19) Baibulo limatiuza kuti: “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, moyo wako wonse, maganizo ako onse ndi mphamvu zako zonse.” (Maliko 12:30) Timasonyeza kuti timakonda Mulungu mwa zolankhula ndi zochita zathu. Zimenezi tingaziyerekezere ndi mwamuna ndi mkazi omwe amasankha kukwatirana chifukwa choti akondana. N’chimodzimodzinso ndi munthu amene amakonda Yehova. Chikondicho chimamupangitsa kuti adzipereke kwa iye komanso kubatizidwa.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena