-
Sonyezani Chikondi ndi Chikhulupiriro Nthaŵi ZonseNsanja ya Olonda—1987
-
-
22. Kodi ndani amene ‘samagwiritsitsa zolimba’ pa Mkristu wokhulupirika, ndipo kodi munthu wotero angapempherere chiyani ndi chidaliro?
22 Tsopano Yohane akufotokoza mwachidule mfundo zazikulu m’kalata yake. (Werengani 1 Yohane 5:18-21.) Aliyense “wobadwa kuchokera mwa Mulungu” monga Mkristu wodzozedwa ndi mzimu “sachimwa.” Yesu Kristu, “Wobadwa kuchokera mwa Mulungu” mwa mzimu woyera, ‘amyang’anira, ndipo woipayo [Satana] samamgwiritsitsa zolimba.’ Mkristu wodzozedwa wokhulupirika wotero angathe kupemphera mwachidaliro kaamba ka chilanditso kuchokera kwa woipayo ndipo angathe, mogwiritsira ntchito ‘chishyango chachikulu cha chikhulupiriro,’ kupewa chivulazo chauzimu chochokera ku ‘mivi yoyaka moto’ ya Satana.—Mateyu 6:13; Aefeso 6:16.
-
-
Sonyezani Chikondi ndi Chikhulupiriro Nthaŵi ZonseNsanja ya Olonda—1987
-
-
25. Monga Akristu, kodi ndimotani mmene tingagwiritsirire ntchito uphungu wa pa 1 Yohane 5:21?
25 Okhala m’chigwirizano ndi Mulungu wowona, Yehova, kaya akhale otsalira odzozedwa kapena a “nkhosa zina,” amafuna kumkondweretsa m’njira iriyonse. Koma mayeso akulowe tsedwa m’kulambira mafano analipo m’zaka za zana loyamba, monga momwedi aliri lerolino. Chotero moyenerera Yohane akumaliza kalata yake mwa kupereka uphungu wautate wakuti: “Tiana, dzisungireni nokha kupewa mafano.” Monga Akristu, sitimaweramira mafano. (Eksodo 20:4-6) Timadziwanso kuti kukakhala kulakwa kudziikira ife eni, chisangalalo, kapena kanthu kena kalikonse mmalo a Mulungu. (2 Timoteo 3:1, 2, 4) Ndipo kudzipatulira kwathu kwa iye kumakaniza kulambira kwathu “chirombo” chandale zadziko ndi “fano” lake. (Chivumbulutso 13:14-18; 14:9-12) Chotero ncholinga cha kukondweretsa Atate wathu wakumwamba ndi kulandira mphatso yake ya moyo wosatha, tiyeni titsimikizire m’chitsimikizo chathu cha kupewa kulambira mafano konse, osakulola konse kuwononga unansi wathu wamtengo wapatali ndi Yehova kudzera mwa Yesu Kristu
-