-
Kulinganiza Tsopano Kaamba ka Zaka Chikwi ZikudzazoNsanja ya Olonda—1989 | September 1
-
-
5. Kodi ndi uti umene udzakhala mkhalidwe wa Satana ndi ziwanda mkati mwa Kulamulira kwa Zaka Chikwi kwa Kristu?
5 Mawu akuti “zaka chikwi” pa Chibvumbulutso 20:4 sali ophiphiritsira koma amalozera ku zaka chikwi za kalenda. Mkati mwa Zaka Chikwi zimenezo, Satana Mdyerekezi ndi makamu ake a ziwanda adzakhala m’phompho, popeza kuti asananene za Kulamulira kwa Zaka Chikwi kwa Kristu, mtumwi Yohane ananena kuti: “Ndipo ndinawona mngelo anatsika Kumwamba, nakhala nacho chifungulo cha phompho, ndi unyolo waukulu m’dzanja lake. Ndipo anagwira chinjoka, njoka yakaleyo, ndiye mdyerekezi ndi Satana, nammanga iye zaka chikwi, namponya kuphompho, natsekapo, nasindikizapo chizindikiro pamwamba pake, kuti asanyengenso amitundu kufikira kudzatha zaka chikwi; patsogolo pake ayenera kumasulidwa iye kanthaŵi.”—Chibvumbulutso 20:1-3.
-
-
Kulinganiza Tsopano Kaamba ka Zaka Chikwi ZikudzazoNsanja ya Olonda—1989 | September 1
-
-
7. Kodi nchiyani chimene Baibulo limasonyeza ponena za nthaŵi ndi mkhalidwe wa Kulamulira kwa Zaka Chikwi kwa Yesu Kristu?
7 Ngakhale kuli tero, mogwirizana ndi Malemba, Kulamulira kowona kwa Zaka Chikwi kwa Yesu Kristu kudakali kutsogolo. Kukwaniritsidwa kwamakono kwa ulosi wa Baibulo kukusonyeza kuti iko kuli pafupi kwenikweni. Mkati mwa Zaka Chikwi zenizenizo, Satana ndi ziwanda zake adzaikidwadi m’phompho, ndipo Yesu Kristu ndi oloŵa m’nyumba anzake a 144,000 adzalamulira mtundu wonse wa anthu popanda kuloŵereramo kwa gulu la Mdyerekezi. Dalitso losatha la mtundu wonse wa anthu wowomboledwa, m’kukwaniritsidwa kwa pangano la Yehova ndi “bwenzi” lake Abrahamu, lidzayamba ndi “khamu lalikulu,” omwe adzapulumuka “chisautso” chosayerekezedwako chimene dongosolo la zinthu loipa iri lidzatha nacho. Lidzafutukukira kwa anthu akufa mabiliyoni angapo owomboledwa ndi “mwazi wa Mwanawankhosa,” Yesu Kristu. (Yakobo 2:21-23; Chibvumbulutso 7:1-17; Genesis 12:3; 22:15-18; Mateyu 24:21, 22) Kufika pa nthaŵiyo, awa adzawukitsidwa kuchokera ku tulo tawo ta imfa m’manda a chikumbukiro kupita ku moyo pa dziko lapansi.—Yohane 5:28, 29.
-