-
Mzinda Wokongola KwambiriMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
6. (a) Kodi Yohane anati chiyani pofotokoza ntchito yoyeza mzinda, ndipo kuyezedwa kwa mzindawu kukusonyeza chiyani? (b) Kodi mfundo yakuti mzindawo unayezedwa “malinga ndi muyezo wa munthu, umene ulinso wofanana ndi muyezo wa mngelo” mwina ikutanthauza chiyani? (Onani mawu a m’munsi.)
6 Yohane akupitiriza kufotokoza kuti: “Tsopano amene anali kundilankhula uja ananyamula bango lagolide loyezera, kuti ayeze mzindawo, zipata zake, ndi mpanda wake. Mzindawo unali ndi mbali zinayi zofanana kutalika kwake. M’litali mwake n’chimodzimodzi ndi m’lifupi mwake. Mngeloyo anayeza mzindawo ndi bangolo, ndipo anapeza kuti unali masitadiya 12,000 kuuzungulira. M’litali mwake, m’lifupi mwake, ndi msinkhu wake, n’zofanana. Anayezanso mpanda wake, ndipo unali wautali mikono 144, malinga ndi muyezo wa munthu, umene ulinso wofanana ndi muyezo wa mngelo.” (Chivumbulutso 21:15-17) Pamene nyumba yopatulika ya pakachisi inayezedwa, zinatsimikizira kuti zolinga za Yehova zokhudza nyumbayo zidzakwaniritsidwa. (Chivumbulutso 11:1) Tsopano pamene mngelo akuyeza Yerusalemu Watsopano zikusonyeza kuti zolinga za Yehova zokhudza mzinda waulemererowu sizingasinthe.a
7. Kodi chochititsa chidwi n’chiyani ndi kukula kwa mzindawo?
7 Mzindawu ndi wochititsa chidwi kwambiri chifukwa mbali zake zonse n’zazitali mofanana. M’litali, m’lifupi komanso msinkhu wake, zinali zazitali masitadiya 12,000 (pafupifupi makilomita 2,200), ndipo unali ndi mpanda wautali mikono 144, kapena kuti mamita 64. Mzinda weniweni sungakhale waukulu choncho chifukwa ungakhale waukulu kuwirikiza nthawi 14 kuposa dziko la Israel la masiku ano, ndipo ungakhale wautali makilomita 560 kupita m’mwamba. Pajatu masomphenya a m’buku la Chivumbulutso anaperekedwa mwa zizindikiro. Ndiye kodi miyezo imeneyi ikutiuza chiyani za Yerusalemu Watsopano wakumwamba?
8. Kodi mfundo zotsatirazi zikutanthauza chiyani? (a) mpanda wa mzindawo unali wautali mikono 144, (b) muyezo wa mzindawo unali masitadiya 12,000, (c) m’litali, m’lifupi ndiponso msinkhu wa mzindawo zinali zofanana ndendende.
8 Mpanda wa mzindawo, womwe ndi wautali mikono 144, ukutikumbutsa mfundo yakuti mzindawu wapangidwa ndi anthu 144,000 amene Mulungu amawaona kuti ndi ana ake auzimu. M’litali, m’lifupi ndi msinkhu wa mzindawo zinali zofanana, ndipo muyezo wake unali masitadiya 12,000. Nambala ya 12 imene ikupezeka pa muyezo umenewu, imagwiritsidwa ntchito mophiphiritsa m’maulosi a m’Baibulo, kuimira gulu lokonzedwa mwadongosolo. Choncho Yerusalemu Watsopano ndi gulu limene linakonzedwa mwadongosolo kwambiri kuti likwaniritse cholinga chamuyaya cha Mulungu. Yerusalemu Watsopano, pamodzi ndi Mfumu Yesu Khristu, ndi gulu limene likupanga Ufumu wa Yehova. Taona kale kuti m’litali mwa mzindawo, m’lifupi mwake, ndi msinkhu wake zinali zofanana. Mofanana ndi zimenezi, Malo Oyera Koposa a m’kachisi wa Solomo, omwe munali zinthu zimene zinkaphiphiritsira kuti Yehova ali mmenemo, analinso ofanana m’litali, m’lifupi ndi msinkhu wake. (1 Mafumu 6:19, 20) Choncho m’pake kuti Yerusalemu Watsopano amene Yohane anaona, yemwe ndi wowala chifukwa cha ulemerero wa Yehova, anali wamkulu kuposa Malo Oyera Koposa aja ndiponso m’litali, m’lifupi ndi msinkhu wake zinali zofanana. Mbali zake zonse n’zofanana ndendende. Mzinda umenewu ulibe mbali iliyonse yokhota kapena yopotoka.—Chivumbulutso 21:22.
-
-
Mzinda Wokongola KwambiriMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
a Mfundo yakuti mzindawo unayezedwa “malinga ndi muyezo wa munthu, umene ulinso wofanana ndi muyezo wa mngelo” mwina ikugwirizana ndi mfundo yakuti mzindawo wapangidwa ndi a 144,000, omwe poyamba anali anthu koma anasintha n’kukhala zolengedwa zauzimu, zofanana ndi angelo.
-