Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mzinda Wokongola Kwambiri
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
    • 9. Kodi Yohane anafotokoza kuti mzindawo unamangidwa ndi zinthu ziti?

      9 Yohane anapitiriza kufotokoza mzindawo kuti: “Mpandawo unali womangidwa ndi mwala wa yasipi, ndipo mzindawo unali womangidwa ndi golide woyenga bwino woonekera ngati galasi. Maziko a mpanda wa mzindawo anawakongoletsa ndi miyala yamtengo wapatali ya mitundu yonse: maziko oyamba anali amwala wa yasipi, achiwiri wa safiro, achitatu wa kalikedo, achinayi wa emarodi, achisanu wa sadonu, a 6 wa sadiyo, a 7 wa kulusolito, a 8 wa belulo, a 9 wa topazi, a 10 wa kulusopurazo, a 11 wa huwakinto, ndipo a 12, wa ametusito. Komanso zitseko za pazipata 12 zija zinali ngale 12. Chitseko chilichonse chinali ngale imodzi. Ndipo msewu waukulu wa mumzindawo unali wopangidwa ndi golide woyenga bwino woonekera ngati galasi.”—Chivumbulutso 21:18-21.

      10. Kodi mfundo yakuti mzindawo unamangidwa ndi yasipi, golide komanso “miyala yamtengo wapatali ya mitundu yonse,” ikutanthauza chiyani?

      10 Mzindawu unamangidwadi mogometsa kwambiri. Pomanga mzindawu sanagwiritse ntchito zinthu zachabechabe zapadziko lapansi ngati dothi kapena miyala wamba, koma anaumanga ndi yasipi, golide woyenga bwino, komanso “miyala yamtengo wapatali ya mitundu yonse.” Miyala imeneyi ikuimiradi zinthu zomangira zakumwamba, ndipo ndi yamtengo wapatali kuposa zinthu zilizonse zomangira nyumba. Kale likasa la pangano linakutidwa ndi golide woyenga bwino, ndipo m’Baibulo kawirikawiri golide amaimira zinthu zabwino komanso zamtengo wapatali. (Ekisodo 25:11; Miyambo 25:11; Yesaya 60:6, 17) Yerusalemu Watsopano yense komanso misewu yake ikuluikulu, inamangidwa ndi “golide woyenga bwino woonekera ngati galasi.” Zimenezi zikusonyeza kuti ndi wokongola mogometsa kwambiri komanso wamtengo wapatali.

  • Mzinda Wokongola Kwambiri
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
    • 12. Kodi mfundo zotsatirazi zikusonyeza chiyani? (a) maziko a mzindawo anakongoletsedwa ndi miyala 12 yamtengo wapatali, (b) zitseko za zipata za mzindawo zinali ngale.

      12 Maziko a mzindawu nawonso ndi okongola kwambiri chifukwa chakuti anawakongoletsa ndi miyala 12 yamtengo wapatali. Zimenezi zikutikumbutsa za mkulu wa ansembe wachiyuda amene pa masiku a zikondwerero ankavala efodi wokhala ndi miyala yosiyanasiyana 12 yamtengo wapatali, yofanana ndi imene yafotokozedwa pa Chivumbulutso 21:18-21. (Ekisodo 28:15-21) Ndithudi, sikuti zimenezi zangofanana mwangozi. Koma zikusonyeza kuti Yerusalemu Watsopano adzagwiranso ntchito za wansembe, ndipo Yesu, amene ndi Mkulu wa Ansembe wapamwamba, ndiye “nyale” yake. (Chivumbulutso 20:6; 21:23; Aheberi 8:1) Komanso madalitso a utumiki wa Yesu monga mkulu wa ansembe, adzafika kwa anthu kudzera mwa Yerusalemu Watsopano. (Chivumbulutso 22:1, 2) Chitseko chilichonse mwa zitseko 12 za zipata za mzindawo, chinali ngale yokongola kwambiri. Zimenezi zikutikumbutsa fanizo la Yesu pamene anayerekezera Ufumu ndi ngale yamtengo wapatali. Aliyense wolowa pazipata za mzindawu adzakhala atasonyeza kuti amakondadi kwambiri zinthu zauzimu.—Mateyu 13:45, 46; yerekezerani ndi Yobu 28:12, 17, 18.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena