-
Kudinda Chidindo Isiraeli wa MulunguMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
Mphepo Zinayi
3. (a) Kodi Yohane anaona angelo akugwira ntchito yapadera yotani? (b) Kodi “mphepo zinayi” zikuimira chiyani?
3 Koma mkwiyo wa Yehova usanayambe, angelo a kumwamba akugwira kaye ntchito inayake yapadera. Yohane anaona zimenezi m’masomphenya, ndipo anati: “Zimenezi zitatha, ndinaona angelo anayi ataimirira m’makona anayi a dziko lapansi. Iwo anali atagwira mwamphamvu mphepo zinayi za dziko lapansi, kuti mphepo iliyonse isawombe padziko lapansi, panyanja, kapena pamtengo uliwonse.” (Chivumbulutso 7:1) Kodi zimenezi zikutanthauza chiyani kwa ife masiku ano? “Mphepo zinayi” zimenezi ndi chizindikiro chabwino kwambiri chophiphiritsira chiwonongeko chimene chatsala pang’ono kugwera anthu oipa padzikoli. Chiwonongekochi chidzagweranso pa “nyanja” yamafunde imene ikuimira anthu osamvera malamulo a Mulungu, ndiponso pa olamulira amene ali ngati mitengo italiitali. Iwo amadalira anthu a padzikoli kuti aziwapatsa mphamvu, ngati momwe mitengo imapezera madzi ndi chakudya munthaka.—Yesaya 57:20; Salimo 37:35, 36.
4. (a) Kodi angelo anayi akuimira chiyani? (b) Kodi n’chiyani chidzachitikire gulu la Satana lapadziko lapansi angelo akadzasiya kugwira mphepo zinayi zija?
4 Sitikukayikira kuti angelo anayi amenewa akuimira magulu anayi a angelo, amene Yehova akuwagwiritsa ntchito kuti chiweruzo chake chisayambe kufikira nthawi yake yoikidwiratu itakwana. Angelowo akadzasiya kugwira mphepo za mkwiyo wa Mulungu, ndipo mphepozo zikadzawomba nthawi imodzi kuchokera kumpoto, kum’mwera, kum’mawa ndi kumadzulo, zidzawononga zinthu koopsa. Chiwonongeko chake chidzakhala choopsa kuposa chimene chinachitika pamene Yehova anagwiritsira ntchito mphepo zinayi pobalalitsa Aelamu, n’kuwawononga ndi kuwatheratu onse. (Yeremiya 49:36-38) Komanso chidzakhala ngati “mphepo yamkuntho” yowononga kwambiri kuposa imene Yehova anagwiritsira ntchito powononga mtundu wa Amoni. (Amosi 1:13-15) Palibe mbali iliyonse ya gulu la Satana lapadziko lapansili yomwe idzapulumuke pa tsiku la mkwiyo wa Yehova. Pa tsiku limeneli, Yehova adzasonyeza kuti ndi woyenera kulamulira, ndipo palibenso amene adzatsutse zimenezi mpaka muyaya.—Salimo 83:15, 18; Yesaya 29:5, 6.
5. Kodi ulosi wa Yeremiya ukutithandiza bwanji kuona kuti chiweruzo cha Mulungu chidzawononga anthu oipa padziko lonse lapansi?
5 Kodi pali umboni wotani wosonyeza kuti chiweruzo cha Mulungu chidzawononga anthu oipa padziko lonse lapansi? Tamvani zina zimene mneneri Yeremiya ananena. Iye anati: “Taonani! Tsoka likuyenda kuchokera mu mtundu wina kupita mu mtundu wina, ndipo mkuntho wamphamvu udzafika kuchokera kumalekezero a dziko lapansi. Pa tsiku limenelo padzakhala anthu ophedwa ndi Yehova kuchokera kumalekezero a dziko lapansi kufikanso kumalekezero ena a dziko lapansi.” (Yeremiya 25:32, 33) Pa nthawi ya mkuntho wamphamvu umenewu m’pamene dziko lonse lidzakhale mumdima wandiweyani. Olamulira ake adzagwedezedwa n’kuwonongedweratu. (Chivumbulutso 6:12-14) Koma sikuti aliyense zinthu zidzamuipira. Ndiyeno kodi angelo akugwira mphepo zinayi zija pofuna kuthandiza ndani?
Kudinda Chidindo Akapolo a Mulungu
6. Kodi ndani amene anauza angelo aja kuti agwire mphepo zinayi, ndipo zimenezi zikupereka mpata wochita chiyani?
6 Yohane anapitiriza kufotokoza kuti anthu ena adzadindidwa chidindo chowathandiza kupulumuka. Iye anati: “Ndinaonanso mngelo wina akukwera kuchokera kotulukira dzuwa, ali ndi chidindo cha Mulungu wamoyo. Iye anafuula mokweza mawu, kwa angelo anayiwo, amene anapatsidwa mphamvu zowononga dziko lapansi ndi nyanja. Anafuula kuti: ‘Musawononge dziko lapansi, kapena nyanja, kapena mitengo, kufikira titadinda chidindo pamphumi za akapolo a Mulungu wathu.’”—Chivumbulutso 7:2, 3.
7. Kodi mngelo wachisanu ndani, ndipo pali umboni wotani umene ukutithandiza kudziwa zimenezi?
7 Ngakhale kuti mngelo wachisanuyu sanatchulidwe dzina, umboni wonse ukusonyeza kuti ayenera kukhala Ambuye Yesu ali mu ulemerero wake. Popeza Yesu ndiye Mkulu wa Angelo, iye akusonyezedwa akulamulira angelo enawo. (1 Atesalonika 4:16; Yuda 9) Iye akuchokera kum’mawa, mofanana ndi mmene adzachitire “mafumu ochokera kotulukira dzuwa,” omwe ndi Yehova ndi Khristu wake, pobwera kudzapereka chiweruzo. Mfumu Dariyo ndi mfumu Koresi nawonso anachokera kum’mawa pobwera kudzagonjetsa mzinda wakale wa Babulo. (Chivumbulutso 16:12; Yesaya 45:1; Yeremiya 51:11; Danieli 5:31) Ndiponso mngelo ameneyu ayenera kukhala Yesu chifukwa wapatsidwa udindo wodinda chidindo Akhristu odzozedwa. (Aefeso 1:13, 14) Komanso, angelo akadzasiya kugwira mphepo zija, Yesu ndi amene adzatsogolere magulu ankhondo akumwamba popereka chiweruzo ku mitundu ya anthu. (Chivumbulutso 19:11-16) Choncho m’pomveka kuti Yesu ndi amene akulamula kuti gulu la Satana lapadziko lapansi lisawonongedwe kaye kufikira akapolo a Mulungu atadindidwa chidindo.
-
-
Kudinda Chidindo Isiraeli wa MulunguMapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
-
-
[Chithunzi chachikulu patsamba 114]
-