-
Yesu Ndi Mesiya Amene Mulungu Ananeneratu Kuti AdzabweraKodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
-
-
Mneneri winanso wa Mulungu, dzina lake Mika, ananeneratu kuti mwana ameneyu akadzakula adzakhala mfumu komanso kuti adzabadwira ku “Betelehemu Efurata.” (Mika 5:2) Pa nthawi imene Yesu anabadwa, ku Isiraeli kunali mizinda iwiri imene inkadziwika ndi dzina lakuti Betelehemu. Mzinda umodzi unali kufupi ndi ku Nazareti, pomwe wina unali kufupi ndi Yerusalemu ku Yuda. Mzinda wa Betelehemu wakufupi ndi Yerusalemu poyamba unkatchulidwa kuti Efurata ndipo kumeneku ndi komwe Yesu anabadwira mogwirizana ndi mmene ulosi unanenera.—Mateyu 2:1.
Ulosi wina unaneneratu kuti Mwana wa Mulungu adzaitanidwa kuti “atuluke mu Iguputo.” Yesu ali mwana makolo ake anapita naye ku Iguputo. Iwo anabwerera naye kwawo pambuyo pa imfa ya Herode ndipo kumeneku kunali kukwaniritsidwa kwa ulosiwu.—Hoseya 11:1; Mateyu 2:15.
Pa tchati chimene chili patsamba 200, malemba amene ali pansi pa mutu wakuti “Ulosi” akufotokoza zinthu zosiyanasiyana zokhudza Mesiya. Yerekezetsani zimene malemba amenewa akunena ndi zomwe zili m’malemba omwe ali pansi pa mutu wakuti “kukwaniritsidwa kwake.” Kuchita zimenezi kungawonjezere zifukwa zina zokuchititsani kukhulupirira kuti Mawu a Mulungu ndi oona.
Mukamawerenga malembawa muyenera kukumbukira kuti malemba amene ali ndi ulosiwo analembedwa zaka zambirimbiri Yesu asanabadwe. Yesu ananena kuti: “Zonse zokhudza ine zolembedwa m’chilamulo cha Mose, m’Zolemba za aneneri ndi m’Masalimo ziyenera kukwaniritsidwa.” (Luka 24:44) Ndipo mukaona m’Baibulo lanu mungatsimikizire kuti maulosi onsewa anakwaniritsidwadi.
-
-
Kudziwa Zoona Zokhudza Atate, Mwana, ndi Mzimu WoyeraKodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
-
-
ZAKUMAPETO
Kudziwa Zoona Zokhudza Atate, Mwana, ndi Mzimu Woyera
ANTHU amene amakhulupirira kuti pali Mulungu Atate, Mulungu Mwana ndi Mulungu Mzimu Woyera amanena kuti mwa Mulungu mmodzi muli anthu atatu. Iwo amakhulupirira kuti atatu onsewa ndi ofanana mphamvu komanso onse alibe chiyambi.
-