-
Kusamalira Makolo OkalambaGalamukani!—1994 | February 8
-
-
Kusamalira Makolo Okalamba
“NDINALI kukhala maso usana ndi usiku, koma ndinalingalirabe zimenezo kukhala mwaŵi.” Umo ndimmene mkazi wina wokwatiwa anafotokozera kusamalira amayi ake okalamba. Kwa mkaziyu, ndi kwa ena ambiri, kusamalira makolo okalamba kuli chinthu chabwino.
Iko kukukhalanso chochitika chofala kwambiri. Gulu la msinkhu limene likukula mofulumira koposa mu United States likunenedwa kukhala gulu la azaka zopitirira 75 zakubadwa. Mu 1900, Aamereka azaka 75 kapena kuposerapo anali osafika chiŵerengero cha miliyoni imodzi. Pofika mu 1980 pafupifupi mamiliyoni khumi anali opitirira zaka 75. Anthu okalamba akukhala ndi moyo nthaŵi yotalikirapo, ndipo pafupifupi mmodzi mwa atatu a awo azaka 85 kapena kupitirirapo amafunikira chisamaliro chanthaŵi zonse.
Pamene kuli kwakuti kusamalira munthu wosakhoza kudzichitira zinthu kungakhale chochitika chopindulitsa, kuli ndi zovuta zake. Ngati kholo lanu limodzi kapena onse aŵiri akalamba ndipo akufunikira chisamaliro chanu, mungapeze mbali zina kukhala zovuta. Kungoona kuti thanzi lawo likufookerafookera kumakupwetekanidi mtima. Ndipo ngati mupatsidwa chithandizo chochepa kapena ngati simupatsidwa chilichonse ndi ziŵalo zina za banja, pamenepo mumasiyiridwa mtolo waukulu wa kupereka chisamalirocho.
Mungapezenso kuti mosasamala kanthu za msinkhu wanu, simumadziona kukhala wamkulu pamaso pa makolo anu. Iwo angakhale ndi chikhoterero cha kukuchitirani monga mwana wamng’ono, ndipo chikhoterero chanunso chingakhale cha kuchita mogwirizana ndi zimenezo. Kusoŵeka kwa chichirikizo cha malingaliro cha mabwenzi kungawonjezere kupsinjika pa kupereka chisamaliro kwanu.
Komabe, zovuta za kupereka chisamaliro siziyenera kudodometsa kusunga unansi wanu wapafupi ndi makolo anu. Malemba amalangiza achikulire momvekera bwino “ [kusonyeza kudzipereka kwaumulungu, NW ] m’banja lawo, ndi kubwezera akuwabala; pakuti ichi ncholandirika pamaso pa Mulungu.” Kumbali ina, “wopitikitsa amayi, ndiye mwana wochititsa manyazi ndi wogwetsa nkhope.”—1 Timoteo 5:4; Miyambo 19:26.
Kudzipereka kwaumulungu kosonyezedwa mwa kupereka chisamaliro kungakhale chinthu cholemeretsa. Koma choyamba, muyenera kudziŵa zimene makolo anu amafunikira kwenikweni monga chithandizo chanu. Nkhani zotsatirazi zingakuthandizeni kudziŵa ndi kukwaniritsa zosoŵa zimenezo. Ndipo pamene kuli kwakuti nkhanizi zikusumika kwambiri pazimene zingachitidwe m’nyumba, ndikodziŵika kuti m’zochitika zina, chifukwa cha kukhala ndi thanzi lofooka kwambiri kapena kukalamba, kholo lingafunikire chithandizo cha akatswiri, monga chija chopezeka m’nyumba zosamalira okalamba.
-
-
Kupenda Zosoŵa za Makolo AnuGalamukani!—1994 | February 8
-
-
Kupenda Zosoŵa za Makolo Anu
KUTI mukhale wothandiza kwenikweni kwa makolo anu okalamba, muyenera kudziŵa zosoŵa ndi zokonda zawo. Apo phuluzi—ndi zolinga zabwino—mungapereke zinthu ndi mautumiki osafunikira kwa makolo anu ndipo amene ngakhale iwo sakuwafuna nkomwe, ngakhale kuti angazengereze kukuuzani zimenezo. Ndiyeno unansi wanu, chifukwa cha kusamvetsetsana, ungakhale wovutitsa mosafunikira osati kwa ino nokha komanso kwa makolo anu.
Kodi Iwo Amafunanji Kwenikweni?
Polingalira kuti tsiku lina kudzakhala kofunikira kusamutsira makolo ake m’nyumba mwake, mkazi awasamutsa panthaŵi yomweyo. Pambuyo pake apeza kuti makolo akewo adakali okhoza kudzikhalira m’nyumba yawoyawo—ndipo akakhala okondwa kwambiri mwanjirayo!
Atasamutsa makolo ake kudzakhala nawo m’nyumba mwake, mwana wamwamuna akuti: “Simudzindilipira ndalama pokhala m’nyumba mwanga! Simungatero pambuyo pondichitira zinthu zambiri zonsezo!” Komabe, zimenezi zichititsa makolo ake kudzilingalira kukhala odalira pa munthu wina mopambanitsa. M’kupita kwanthaŵi iwo amuuza kuti angakonde ulemu wa kukhala othandiza mwanjira inayake.
Banja litumikira makolo awo okalamba m’njira yaing’ono iliyonse kutsimikizira kuti iwo ali mumkhalidwe wabwino ndipo sakuthodwa ndi zochitachita. Pambuyo pake apeza kuti makolo awo amafuna kudzichitira okha zinthu zambiri.
M’chilichonse cha zitsanzo zili pamwambazi, mautumiki ochitidwawo anali osafunikira ndi osafunidwa ndi makolowo. Zimenezi zingathe kuchitika mosavuta ngati mwana wamwamuna kapena wamkazi wokhala ndi cholinga chabwino asonkhezeredwa ndi lingaliro lopambanitsa la kukhala ndi thayo kapena ngati pali kusamvetsetsana ponena za zosoŵa zenizeni za makolo. Talingalirani za kuvutika maganizo kosafunikira kumene zimenezi zimachititsa kwa onse okhudzidwa. Ndithudi, mankhwala ake ndiwo kupenda zosoŵa ndi zokonda zenizeni za makolo anu.
Kodi makolo anu akufunikiradi kusamukira m’nyumba mwanu pakali pano? Kodi iwo akufuna kutero nkomwe? Zingakudabwitseni kudziŵa kuti okalamba ena amakhumba kwambiri kukhala ndi moyo wodziimira paokha monga momwe kungathekere. Powopa kuonedwa kukhala osayamikira, iwo angazengereze kuuza ana awo kuti angakonde kudzikhalira okha m’nyumba yawoyawo, mosasamala kanthu za zovuta. Iwo angakhale akukonda ana awo ndi kulakalaka kuthera nawo nthaŵi limodzi. Koma kodi akhale odalira pa ana awo? Iyayi, iwo angakonde kudzichitira okha zinthu.
Mwinamwake tsiku lina kudzakhala kofunikira kusamutsira makolo anu m’nyumba mwanu. Komabe, ngati nthaŵiyo siinafikebe, ndipo ngati mowona mtima iwo akufuna kudzikhalira okha, nkuwamaniranji zakazo za kudziimira paokha? Kodi masinthidwe ena apanyumba kapena kuwaimbira lamya kwa nthaŵi zonse kapena kuwachezera kungachititse kuti apitirize kukhala m’nyumba yawo? Iwo angakhale achimwemwe kwambiri m’nyumba yawoyawo, akumadzipangira zosankha zawo za tsiku ndi tsiku.
Wopereka chisamaliro wina anafotokoza kufulumira kwake kwa kusamutsira amayi ake m’nyumba mwake kuti: “Pamene atate anamwalira, tinatenga amayi ndi kukhala nawo, tikumawachitira chisoni. Koma zinachitika kuti iwo anakhalabe ndi moyo kwa zaka 22. M’malo mogulitsa nyumba yawo, iwo akanapitirizabe kukhalamo. Musakhale ofulumira kusankha njira zimene ziyenera kutsatiridwa. Chosankha chonga chimenecho, chitapangidwa chimavuta kuchisinthanso.”—Yerekezerani ndi Mateyu 6:34.
‘Komabe,’ inuyo mungatsutse motero, ‘bwanji ngati chinachake chichitika kwa mmodzi wa makolo anga pamene akukhala m’nyumba yawoyawo? Ngati amayi kapena atate angagwe ndi kudzipweteka, ndingamve kukhala waliwongo kwambiri! ’ Imeneyi ndinkhaŵa yomvekera bwino, makamaka ngati nyonga kapena thanzi la makolo anu yakhala yofooka kwambiri moti palidi chiwopsezo cha ngozi. Komabe, ngati sizili choncho, dzifunseni nokha ngati kuti nkhaŵa yanuyo ili kaamba ka makolo anu kapena kaamba ka inu mwini, kuti mupeŵe kudzimva waliwongo mosayenera.
Talingaliraninso kuthekera kwakuti makolo anu angakhale bwinopo m’nyumba yawoyawo. M’buku lakuti You and Your Aging Parents, Edith M. Stern ndi Dr. Mabel Ross akunena kuti: “Kufufuza kwasonyeza kuti anthu okalamba amakhala okangalika ndi aumoyo kwambiri pamene ali m’nyumba zawozawo koposa kwina kulikonse. Mwachidule, zoyesayesa zambiri zolakwika za kupangitsa zaka zotsirizira kukhala zabwinopo zimangokhala zachipambano m’kuzipangitsa kunyonyotsoka mofulumira kwambiri.” Chotero, thandizani makolo anu kukhala ndi moyo modziimira paokha monga momwe kungathekere, pamenenso mukupereka chisamaliro ndi mautumiki amene ali ofunikiradi kwa iwo. Muyeneranso kupenda nthaŵi ndi nthaŵi ndi kupanga masinthidwe pamene zosoŵa za makolo anu zikuwonjezereka kapena ngakhale kuchepekera.
Khalani Atcheru
Mwakupenda thanzi ndi mikhalidwe ya makolo anu, mwinamwake kuwatenga ndi kukhala nawo m’nyumba mwanu ndiko kungakhale chosankha chabwino koposa. Ngati ndichoncho, khalani atcheru ponena za kuthekera kwakuti iwo angakonde kumadzichitira okha zinthu zambiri monga momwe kungathekere. Mofanana ndi anthu a msinkhu uliwonse, mwachionekere nawonso amakhumba kukhala ozindikirika, kukhala ndi programu yawoyawo ya zochita, ndi mabwenzi awoawo. Zimenezi zingakhale zabwino. Ngakhale kuti kudzakala kokondweretsa kuchitira pamodzi zinthu zina pachibale, kungakhale bwino kwa inu kupatula zochita zina kaamba ka banja lanulanu lokhalo ndi kulola makolo anunso kukhala ndi zochita zawozawo. Wopereka chisamaliro wina ananena mwanzeru kuti: “Tsimikizirani kuti makolo anu ali ndi mipando yabwinopo ndi zithunzithunzi zojambulidwa zimene amakonda kwambiri.”
Poyesayesa kuzindikira zosoŵa zenizeni za makolo anu, lankhulani nawo. Mvetserani nkhaŵa zawo ndipo khalani atcheru ndi zimene angakhale akuyesa kukuuzani. Afotokozereni zimene muli wokhoza kuwachitira ndi zimene simuli wokhoza kotero kuti asadzagwiritsidwe mwala ndi ziyembekezo zonama. “Khalani wozindikira bwino lomwe zimene zingayembekezeredwe kwa onse a m’banja,” anatero wopereka chisamaliro wina. “Kambitsiranani kaŵirikaŵiri kuwapeŵetsa kukhala ndi malingaliro oipa ndi kuipidwa mtima.” Ngati mupanga malonjezo aliwonse anthaŵi yaitali a kuwachitira chinthu (“Ndidzidzakuonani pa Lolemba lililonse masana”; “Ndidzakhala ndikupita nanu pamapeto a mlungu aliwonse”), ndibwino ngati mungakumveketse bwino kuti mudzafuna kuyesa kwa nyengo yanthaŵi yakutiyakuti ndi kuona mmene zidzayendera. Mwakutero, ngati zioneka kukhala zosatheka, mwaŵi ulipo kale wa kusintha zimenezo.
Palibe chilichonse cha zotchulidwa pamwambapa chimene chiyenera kutengedwa kukhala chifukwa chomanira makolo ulemu ndi chithandizo zowayenerera. Lingaliro la Mlengi pankhaniyi nlomvekera bwino. Ana achikulire ayenera kupatsa makolo awo ulemu, chisamaliro, ndi chichirikizo. Yesu anatsutsa Afarisi odziyesa okha olungama chifukwa cha kupotoza malemba kuti alungamitse kunyalanyaza kwawo makolo. Mawu olongosola momvekera bwino a pa Miyambo 30:17 amasonyeza kunyansidwa kumene Mulungu amakhala nako pa awo amene salemekeza makolo awo kuti: “Diso lochitira atate wake chiphwete, ndi kunyoza kumvera amake, makungubwi a kumtsinje adzalikolowola, ana a mphungu adzalidya.”—Onani Marko 7:9-13; 1 Timoteo 5:4, 8.
Pamene mukupereka chisamaliro chofunikira kwa makolo anu, mungapezenso zovuta zatsopano. Kodi mungachite nazo motani zimenezi? Nkhani yotsatira idzapereka malingaliro ena.
[Zithunzi patsamba 5]
Kholo lingasangalale kudzichitira zinthu ndi mabwenzi ndiponso ndi banja
-
-
Kupereka Chisamaliro Kuchita ndi Zovuta za tsiku ndi TsikuGalamukani!—1994 | February 8
-
-
Kupereka Chisamaliro Kuchita ndi Zovuta za tsiku ndi Tsiku
NGATI kupereka chisamaliro kumakudzetserani zovuta, makamaka zimene simunayembekezere, mungadzimve kukhala waliwongo. Mungazizwe kuti: ‘Kodi pali chilichonse cholakwika muunansi wanga ndi makolo anga? Kodi achikulire m’zitaganya zambiri samakhala ndi moyo mwachimwemwe ndi makolo awo m’miyoyo yawo yonse?’
Eya, mkhalidwe wanu ungakhale wosiyana. Mwina makolo anu asamukira m’nyumba mwanu pambuyo pokhala paokha popanda inu kwa zaka 20, 30, 40, kapena kuposerapo. Izi zikutanthauza kuti inuyo ndi makolo anu munaumba maumoyo ndi zizoloŵezi payekhapayekha kwa nthaŵi yaitali ya miyoyo yanu. M’kupita kwa zaka makumi angapo, maumoyo amenewo ndi zizoloŵezi zingakhale zosiyana kwambiri. Koma tsopano, monga wopereka chisamaliro, mukuyang’anizana ndi kufunika kwa kugwirizanitsa moyo wanu ndi ya awo amene mukuwasamalira. Ichi chingakhale chovuta kwambiri kuposa ndi mmene zikanakhalira ngati munali kukhala pamodzi nthaŵi yonseyo.
Ndiponso, makolo ena angakhale odwala kwambiri kapena m’njira zina angafunikire chisamaliro chapadera chowonjezereka. Pamene kuli kwakuti, moyamikirika, mungakhale mukupereka zofunikira ndi kusaona kufunika kulikonse pakali pano kwa kuika makolo anu m’nyumba zosamalira okalamba, mkhalidwe umenewu mosakayikira umachititsa zovuta za tsiku ndi tsiku pa nonsenu. Kusamalira makolo anu nkwachibadwa. Kukalamba ndi kudwala sikwachibadwa. Sichinali konse chifuno cha Mlengi kuti anthu adzithedwa nyonga yawo ndi thanzi akamakula. Chifukwa chake, musaganize kuti pali chinachake cholakwika ndi inu chifukwa chakuti mkhalidwe umafuna zowonjezereka kwa inu, mwamalingaliro ndi mwakuthupi, kuposa zimene munayembekezera.—Genesis 1:26-31; Salmo 90:10.
Zovuta zochititsidwa ndi kupereka chisamaliro sizimatanthauza kwenikweni kuti palibe unansi wabwino pakati pa inu ndi makolo anu. Makamaka ngati munali nawo ndi unansi wabwino kumbuyoko asanafunikire chithandizo chanu, kuli kwachionekere kuti zovuta zilizonse zimene mukuyang’anizana nazo zili kaamba ka zitokoso zimene kusamalira makolo kungadzetse. Kodi ndimotani mmene mungachitire mwachipambano ndi zovuta za tsiku ndi tsiku?
Kuchita ndi Malingaliro Aliwongo
Ngakhale anthu amene akuchita zonse zimene angathe ndi zimene ayenera kuchitira makolo awo, nthaŵi zina amamva kukhala aliwongo posachita zoposerapo. Komabe, liwongo losayenera lingakhale vuto. Mungapeze kuti mukupanga zosankha zokhala ndi chifuno cha kuthetsa liwongo lanulo koma osati kwenikweni cha kudzithandiza inu eni kapena makolo anu. Mwachitsanzo, kodi chingachitike nchiyani ngati, poyesa kuthetsa malingaliro ake aliwongo losayenera, mkazi amwerekera m’kupereka chisamaliro ndi kunyalanyaza mwamuna wake ndi ana ake? Mkaziyo, mwamuna wake, ndi ana akewo akavutika ndi zotulukapo zake. Motero musalole liwongo losayenera kulamulira umoyo wanu.
Kodi nthaŵi zina mumamva kukhala waliwongo chifukwa kukuoneka kuti simungachitire makolo anu zokwanira? Pamenepo, nkothekera kuti zosoŵa za makolo anu zikuposa zimene mukhoza kupereka. Mkhalidwewo ungakhale wakuti, mosasamala kanthu ndi zimene muchita, nthaŵi zonse pamakhalabe zowonjezereka zimene mukanachita. Ndiponso, ngati muona kupereka chisamaliro kukhala njira yobwezera makolo anu zonse zimene anakuchitirani monga chisamaliro pokula, mudzadzimva waliwongo nthaŵi zonse, chifukwa chakuti simungathe konse kuwabwezera zonse.
Buku lakuti You and Your Aging Parents limatchula kufunika kwa kusankha mlingo wa zimene mudzachitira makolo anu. Ilo limati: “Mudzapeŵa kupwetekedwa mtima ndi kupsinjika maganizo kwambiri ngati muzika [zosankha zanu] makamaka, osati pazimene mungakonde kuchita kapena zimene muyenera kuchita koma pazimene mungathe kuchita.”
Inde, dziŵani motsimikiza zimene muganiza kuti mukhoza kuchita. Kungakhale kothandiza ngati mupempha chithandizo cha bwenzi lodalirika limene limadziŵa zokhoza zanu, zolephera zanu, ndi mkhalidwe wa banja lanu. Kodi mungathe kutenga makolo anu ndi kuwasunga m’nyumba mwanu? Kodi muli nawo malo okwanira? Kodi iwo adzalola kusamuka? Ngati makolo anu sakukhala nanu, kodi mungathe kumawachezera kaŵirikaŵiri motani, ndipo liti? Ngati muchita zimene mungathe, simufunikira kumva kukhala waliwongo. Komabe, ngati mumvabe kukhala waliwongo, zindikirani kuti malingalirowo ali osayenera ndipo akanizeni kulamulira zosankha zanu.
Gaŵanani Mtolowo
Buku la Baibulo la Mlaliki limanena mmene kuliri koipa ‘kupambanitsa kukhala woipa’ kapena ‘kupambanitsa kukhala wolungama’ ndi kuti kupambanitsa kukhala wolungama kungachititse ‘kudziwononga wekha.’ (Mlaliki 7:16-18) Zimenezi zingachitike ngati muyesa kukwaniritsa zoposa zimene mufuna kuchita, zimene mukhoza kuchita, ndipo ngakhale zimene muyenera kuchita.
Ngati mudali kale ndi programu ya zochita yokwanira musanayambe kusamalira makolo anu, muyenera kuchotsapo zochita zina kapena kupeza chithandizo. Komabe, ambiri ofunikira chithandizo amazengereza kupempha. Iwo angakhale amanyazi kwambiri kapena anganene kuti ena samafuna kuthandiza. Komabe, mumadzivulaza nokha limodzi ndi ena oloŵetsedwamo ngati mudzitopetsa kwambiri. M’buku lake lonena za kupereka chisamaliro, mlembi E. Jane Mall akutcha kudzitopetsa koteroko “nthenda ya kudzipha.” Iye akulangiza kuti: “Muyenera kukhala ndi ndandanda ya zofunika zoyamba, ndipo zitatu za zofunika zanu zoyamba ziyenera kukhala nthaŵi yokhala ndi [mnzanu wa muukwati], nthaŵi yokhala ndi ana anu ndi mabwenzi anu, ndi nthaŵi ya inu mwini.”
Inde, mungafunikire kugaŵana mtolowo. Chotero, kodi mungapite kuti kukafunako chithandizo? Banja, mabwenzi, anansi, ndi akatswiri angathadize. Koma muyenera kupempha chithandizocho. Ndipo muyenera kupempha mwachindunji. Kungopereka malingaliro kaŵirikaŵiri sikumagwira ntchito. Mungadabwe kuona amene ali ofunitsitsa kuthandiza ndi kuchuluka kwawo ngati muchita kuti zosoŵa zanu zidziŵike momvekera bwino ndi mapempho anu motsimikiza. Mwachitsanzo, mungapemphe munthu wina kukuthandizani kuyeretsa nyumba. Ngati zimenezo zikakupatsani mpumulo wofunikira, pamenepo imeneyi sinthaŵi yakuti muumirire pakuyeretsa nyumba inu eni chifukwa chakuti ‘palibe aliyense amene adzaiyeretsa bwino lomwe.’
Ngati muli ndi abale ndi alongo, nawonso ali ndi thayo la kusamalira makolo awo. Mwinamwake mwachita mbali yonse kapena mbali yaikulu ya kupereka chisamaliro kufikira tsopano, mukumaganiza kuti abale ndi alongo anu ali osakhoza kapena osafunitsitsa kuthandiza. Komabe, kodi mwapempha chithandizo chawo mwachindunji? Anthu ena angachitepo kanthu—ngati auzidwa momvekera bwino kuti chithandizo chikufunikira.
Ena amadzigangira kusamalira kholo lawo poyesa kudzipezera kapena kutetezera chiyanjo cha makolo. Kapena angadzimve kukhala amtima wosunga munthu mwakuchita okha ntchito yonseyo. Iwo angadandaule kuti ena sakupereka chisamalirocho, koma iwonso angasonyeze zizindikiro zosonyeza kuti akufuna kuti zikhale motero. Zimenezi zingakhale mtundu wa kupambanitsa kukhala wolungama. Koma kodi nkuikiranji mavuto osafunikira pa inu mwini? Ngati chithandizo chilipo, chipempheni, ndipo chigwiritsireni ntchito.
Chenjezo nali: Musayembekezere kuti abale anu ndi alongo adzagaŵana nanu thayolo molingana. Ngakhale kuti nthaŵi zina kungakhale kotheka kwa iwo kuchita zimenezo, kaŵirikaŵiri mikhalidwe yawo imachititsa zimenezo kukhala zovuta, ndipo ngakhale zosatheka. M’zochitika zambiri kumakhala kothandiza kwa chiŵalo chimodzi cha banja kukhala wopereka chisamaliro chenicheni, pamene ziŵalo zina za banja, makamaka achimwene ndi achemwali, zikuthandiza ndi ndalama ndi mwa kuimba lamya, kuwachezera, kapena nthaŵi zina kutengera makolowo kunyumba kwawo kapena pamaulendo a kumapeto kwa mlungu.
Kukhalirana Pafupi
Kukhalirana pafupi kungabutse zinthu zazing’ono zokwiyitsa. Zizoloŵezi zimene mukhoza kulolera mosavuta kwa bwenzi lanu zingaoneke kukhala zosalolereka kwa chiŵalo chabanja chapafupi.
Ndiponso, makolo anu anganene kanthu kena konga, ‘Kukanakhala kotheka ukanakhala nane kwa nthaŵi yokulirapo, koma ndidziŵa kuti uli wotanganitsidwa kwambiri.’ Mawuŵa angabise zimene kholo likuganiza zakuti simumadera nkhaŵa makolo anu kwenikweni. Mwina mungayankhe mawuwo ndi mkwiyo. Koma mmalo mokwiya, kodi sikungakhale bwinopo kusamalira nkhaŵa yobisala yeniyeniyo ya kholo lanu, kufuna kwawo kukhala nanu kwa nthaŵi yotalikirapo? Ngakhale ngati simungathe kuchita mogwirizana ndi pempho lawo, kufotokoza zinthu mokoma mtima kudzakhala ndi zotulukapo zabwino mmalo mwa yankho lopweteka.—Miyambo 12:18.
Kuyesayesa mwakhama kukulitsa mikhalidwe imene ikulimbikitsidwa m’Baibulo kudzakukhozetsani kukhalabe wokoma mtima komanso wolimba ngati kuli kofunikira. Buku la Baibulo la Akolose limavomereza motsimikizirika kuti nthaŵi zina timakhala ndi “chifukwa pa mnzake.” Limatilangiza kupitiriza “kulolerana wina ndi mnzake, ndi kukhululukirana eni okha.” Limatichichizanso kuvala “mtima wachifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, chifatso, ndi kuleza mtima.” (Akolose 3:12-14) Ndithudi, mikhalidwe yoteroyo idzakhala yothandiza kwambiri kuchepetsa zokwiyitsa zochititsidwa ndi kukhalirana pafupi.
Ngakhale pamenepo, ngati nthaŵi zina muphophonya, kutaya mtima, ndi kunena kanthu kena kamene muganiza kuti simunafunikira kunena, “dzuŵa lisaloŵe muli chikwiyire.” Pepesani mwamsanga, ndipo iŵalani nkhaniyo. Musailole kukhala chinthu chinanso chokuchititsani kudzimva waliwongo.—Aefeso 4:26, 27.
Kukhala ndi Nthaŵi ndi Malo Amtseri
Ngati inuyo ndi makolo anu mumakhala m’nyumba imodzi, kungakukhalireni kovuta kupeza nthaŵi ndi malo amtseri. Komabe, zimakhala zofunikira pamlingo wakutiwakuti kwa inuyo ndi makolo anu. Mungakambitsirane nawo za vuto limeneli ndi kumvana kuti nthaŵi ndi malo akutiakuti ali amtseri kwa inu kapena kwa abanja lanu. Mwachitsanzo, kwa mabanja ena, koma osati onse, kutseka chitseko ndi kuikako chikwangwani cholembedwapo kuti musadodometse kungazindikiridwe ndi onse kukhala chosonyeza malo kapena nthaŵi yamtseri kwa munthu yemwe ali mkatimo.
Ngati chipindacho chilibe chitseko, chochinga chonyamulika kapena chenga chingatumikire chifuno chofananacho. Chikumbutso choyenera chingaperekedwe ngati nthaŵi yamtseri yofunikirayo imadodometsedwa mosayembekerezeka. Mfundo ili yakuti, kufunika kwa nthaŵi ndi malo amtseri kwa wina kuyenera kulemekezedwa ndi onse m’banja.
Mwaŵi
Kumbukirani kuti ngakhale kuti kufooka kulikonse kwa thanzi la makolo anu kungakhale koŵaŵitsa kwa inu, Mlengi wathu, Yehova, amafuna kuti ife tikhale ndi mlingo wa chisangalalo ngakhale pamene tiyang’anizana ndi mikhalidwe yopereka chiyeso. Ntchito imeneyi ingakuthandizeninso kuyandikira pafupi ndi Yehova pamene muyedzamira pa iye mwapemphero. Wopereka chisamaliro wina ananena motere: “Nthaŵi zonse ndinali kukhala pafupi ndi Yehova, koma kupereka chisamaliro kunandiphunzitsa kudalira pa iye kotheratu. Kunali ngati kusiyana kokhala pakati pa kulankhula palamya ndi munthu wokhala kutali kwambiri ndi kukhala ndi munthuyo. Yehova anali nane pompo.”
Kupereka chisamaliro kuli mwaŵi ndiponso thayo. Lankhulanani ndi makolo anu kotero kuti mudziŵe zosoŵa zawo. Apezereni zofunikira zawo, ndipo khalanibe achisangalalo pochita zimenezo.—Afilipi 4:4-7; 1 Petro 5:7.
-