Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/95 tsamba 7
  • Kodi Mukuona Kusoŵako?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mukuona Kusoŵako?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Nkhani Yofanana
  • “Mukhale Nacho Chikondano Chenicheni mwa Inu Nokha”
    Ogwirizana m’Kulambiridwa kwa Mulungu Yekha Wowona
  • “Mukhale Nacho Chikondano Chenicheni”
    Lambirani Mulungu Woona Yekha
  • Thandizo Lopezekeratu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Pitirizani Kukonda Yehova ndi Anthu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
km 4/95 tsamba 7

Kodi Mukuona Kusoŵako?

1 Yehova amafotokozedwa kukhala Mthandizi ndi Ngaka. Tikudziŵa kuti tingathe kupita kwa iye panthaŵi ya kusoŵa ndipo adzatithandiza. (Sal. 18:2; 46:1) Tingatsanzire mkhalidwe wachifundo umenewu mwa kupereka thandizo kwa ena pamene tiona kusoŵa kwawo.

2 Kodi nchiyani chimene chimasonkhezera munthu kudzipereka kuthandiza wina? Anthu ochuluka amadziŵa kuti kuchita zimenezi ndi chibadwa cha munthu cha chikondi. Indedi Mawu a Mulungu amalimbikitsa zimenezi. (Aroma 15:1) Paulo anatilimbikitsa ‘kusapenyerera zathu za ife tokha, koma kupenyerera za anzathu.’—Afil. 2:4.

3 Kuchita zimenezi kungatikondweretse tonsefe. (Mac. 20:35) Paulo anatchula mnyamatayo Timoteo monga chitsanzo cha munthu amene ‘akasamalira za kwa’ abale ake. (Afil. 2:20) Ndi bwino kuti tili ndi achichepere ambiri m’mipingo lerolino amene ali ndi khalidwe longa limenelo. Koma kaya ndife wachichepere kapena wachikulire, zilipo zinthu zimene tiyenera kuchita titaona kusoŵa kwina.

4 Kodi munalingalirapo kuti ena ali ndi zosoŵa zimene zingasamaliridwe bwinopo? Mwinamwake mbale kapena mlongo anali m’chipatala, ndipo oŵerengeka okha ndiwo anakamzonda; kapena wina anapuwala, koma panalibe wotumikira kapena wothandiza ntchito za panyumba. Yesu amaona aja amene akutumikira Yehova monga a m’banja limodzi amene amasamaliranadi. (Marko 3:33-35) M’fanizo la nkhosa ndi mbuzi, iye anasonyeza kuti aja amene ali kudzanja lamanja la Mfumu ali oyanjidwa chifukwa cha kuthandiza kwawo abale a Mfumuyo.—Mat. 25:40.

5 Kodi Ndingathandize Motani? Kodi chingachitidwe nchiyani kuti thandizo liperekedwe pamene pali kusoŵa koonekeratu? Kodi ife tingayambe kuthandiza mwa njira ina? Mwinamwake pali okalamba amene afunikira chilimbikitso, koma alibe mabwenzi apafupi owathandiza. Pangakhale achichepere amene afunikira thandizo. Banja lokondwerera chatsopano la ana ambiri lingafike pa Nyumba Yaufumu pamene wofalitsa yemwe amaphunzira nawo palibe. Iwo angayamikire ngati wina angadzipereke kuthandiza ana awo.

6 Pamene chikondi chathu pa choonadi ndi gulu la Yehova chikukula, nakonso kuzindikira ena mumpingo ndi kuwadera nkhaŵa kumakula. Paulo anatilimbikitsa kukulitsa mikhalidweyo pankhaniyi. (2 Akor. 6:11-13) Yesu anagogomezera kuti kusonyezana kwathu chikondi ndiko njira yaikulu imene timasonyezera kuti tilidi otsatira ake.—Yoh. 13:35.

7 Chotero pamene tiona kusoŵa, chikondi chenicheni pa abale athu ndi mpingo chiyenera kutisonkhezera kuchitapo kanthu ndi kuwathandiza mwa njira iliyonse imene tingathe. (Agal. 6:9, 10) Kusamalira ena kumeneku kumatigwirizanitsa pamodzi m’zomangira zolimba za chikondi ndi umodzi. (1 Akor. 10:24) Mwa njira imeneyi, timachita mbali yathu ya kusamalira kusoŵa mumpingo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena