Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ubatizo
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Luka 3:16, 17: “Iyeyu [Yesu Kristu] adzakubatizani inu ndi . . . moto. Amene chouluzira chake chiri m’dzanja lake, kuti ayeretse padwale pake . . . mankhusu adzatentha m’moto wosazima.” (Chiwonongeko chake chikakhala chosatha.)

      Mat. 13:49, 50: “Adzatero pachimaliziro cha nthaŵi ya pansi pano: angelo adzatuluka, nadzawasankhula oipa pakati pa abwino, nadzawataya m’ng’anjo ya moto.”

      Luka 17:29, 30: “Tsiku limene Loti anatuluka m’Sodomu unavumba moto ndi sulfure zochokera kumwamba, ndipo zinawawononga onsewo; momwemo kudzakhala tsiku lakuvumbuluka Mwana wa munthu.”

      Suli wofanana ndi ubatizo wa mzimu woyera, umene unali wa ophunzirawo

      Mac. 1:5, NW: “Yohane, ndithudi, anabatiza ndi madzi, koma inu [atumwi okhulupirika a Yesu] mudzabatizidwa mu mzimu woyera pasanapite masiku ambiri kuchokera panthaŵi ino.”

      Mac. 2:2-4, NW: “Mwadzidzidzi panachitika kuchokera kumwamba phokoso longa ngati lija lamphepo yolimba yothamanga, ndipo linadzadza nyumba yonseyo mmene iwo anali kukhala. Ndipo malirime onga ngati a moto anakhala owonekera kwa aliyense wa iwo ndipo anagawidwa, ndipo linakhala pa aliyense [koma silinaphimbe kapena kumiza] aliyense wa iwo, ndipo iwo onse anakhala odzadzidwa ndi mzimu woyera nayamba kulankhula ndi malirime osiyanasiyana, monga momwe mzimu unali kuwalolera iwo kulankhula.”

  • Uchete
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Uchete

      Tanthauzo: Mkhalidwe wa amene samatenga mbali kapena kupereka chichirikizo kwa alionse amagulu aŵiri kapena oposerapo otsutsana. Chiri chowonadi cha m’mbiri yakale ndi yamakono chakuti mu mtundu uliwonse ndi m’mikhalidwe yonse Akristu owona ayesayesa kusunga uchete wotheratu m’kumenyana kwa pakati pa magulu otsutsana a dziko. Iwo samadodometsa zimene ena amachita ponena za kukhala ndi phande m’madzoma akukonda dziko lawo, kutumikira m’magulu a ankhondo, kugwirizana ndi chipani chandale zadziko, kuloŵa m’kupikisana nawo malo m’kusankhiridwa paudindo m’ndale zadziko, kapena kuchita voti. Koma iwo amalambira Yehova yekha, Mulungu wa Baibulo; iwo apatulira miyoyo yawo yonse kwa iye ndi kupereka chichirikizo chokwanira ku Ufumu wake.

      Kodi ndimalemba ati amene asonkhezera mkhalidwe wa Akristu kulinga ku ulamuliro wa maboma a dziko?

      Aroma 13:1, 5-7: “Anthu onse amvere maulamuliro a akulu [olamulira a boma]; pakuti palibe ulamuliro wina koma wochokera kwa Mulungu . . . Chifukwa chake, kuyenera kuti mukhale omvera, si chifukwa cha mkwiyo wokha, komanso chifukwa cha chikumbu mtima. . . . Perekani kwa anthu onse mangaŵa awo; msonkho kwa eni ake a msonkho; kulipira kwa eni ake a kulipidwa; kuwopa kwa eni ake a kuwopa; ulemu kwa eni ake a ulemu.” (Palibe boma limene likanakhalako popanda chilolezo cha Mulungu. Mosasamala kanthu za khalidwe la olamulira alionse pa okha, Akristu awona awasonyeza ulemu chifukwa cha udindo umene ali nawo. Mwachitsanzo, mosasamala kanthu za mmene maboma agwiritsirira ntchito ndalama za msonkho, olambira Yehova anakhoma misonkho yawo mowona mtima mobwezera mautumiki amene aliyense anapindula nawo.)

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena