Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/00 tsamba 1
  • Lingalirani Ntchito Zodabwitsa za Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Lingalirani Ntchito Zodabwitsa za Mulungu
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Nkhani Yofanana
  • Akuchita Mawu a Mulungu Amapeza Chimwemwe
    Nsanja ya Olonda—2001
  • “Akuchita Mawu” Achimwemwe
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Kodi Mudzanena Kuti,“Ndine Pano! Munditumize Ine”?
    Nsanja ya Olonda—1987
  • Mmene Yehova Amatithandizira Kuti Tizipirira Mosangalala
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
km 10/00 tsamba 1

Lingalirani Ntchito Zodabwitsa za Mulungu

1 Kwa masiku atatu abwino, tinali pa Msonkhano Wachigawo wakuti “Akuchita Mawu a Mulungu.” Tinachotsa malingaliro athu pazimene timachita m’moyo watsiku ndi tsiku n’kuwaika pantchito zodabwitsa za Yehova. Msonkhano unakonzedwa n’cholinga chokulitsa chikhulupiriro chathu mwa Mulungu ndi m’Mawu ake, kulimbitsa unansi wathu ndi iye, ndiponso kuwonjezera changu chathu pa utumiki. Kodi tikupindula motani ndi zinthu zimene tinaphunzitsidwa?—Yoh. 13:17.

2 Mabanja Mverani Mawu a Mulungu: Nkhani yosiyirana ya mutu wakuti “Mverani Mawu a Mulungu” inatithandiza kupenda mkhalidwe wauzimu wa mabanja athu. Ana amakonda kuphunzira. Choncho, makolo oopa Mulungu analimbikitsidwa kupanga phunziro la Baibulo la banja kukhala maziko a banja lolimba mwauzimu. Mitu ya mabanja yambiri ikuphunzira ndi ana awo bulosha latsopano lakuti Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu! Zimenezi ziwathandiza kukhala ndi unansi wabwino komanso wolimba ndi Yehova. Makolo, aphunzitseni ana anu mmene angapeŵere kukhumudwitsa Mulungu. Sonyezani kuti mumam’konda komanso mumakonda zochita zake. (Sal. 103:2) Chitirani zinthu limodzi poika ndi kukwanitsa zolinga zauzimu ndiponso potumikira Yehova mokwanira.

3 Mawu a Mulungu Akuunikira Njira Yathu: Tinali osangalala kwambiri kulandira buku latsopano la Ulosi wa Yesaya—Muuni wa Anthu Onse 1. Kodi gawo loyambali mwaliŵerenga kufika pati? Buku la Yesaya limaneneratu za ziweruzo zoopsa pa mitundu yosapembedza komanso madalitso abwino a Ufumu kwa anthu a Mulungu. (Yes. 34:2; 35:10) Limalimbitsanso chikhulupiriro ndi chidaliro mwa Yehova ndiponso mmene amachitira zinthu.—Yes. 12:2-5.

4 Poŵerenga Ulosi wa Yesaya 1, mutha kuona kumayambiriro kwenikweni mmene Yesaya anakhalirabe wokhulupirika kwa Yehova atazingidwa ndi zoipa. Atafunsidwa kukhala mthenga wa Mulungu, Yesaya anayankha kuti: “Ndine pano; munditumize.” (Yes. 6:8) Kulingalira za mzimu wake wofunitsitsa kudzakulimbikitsani kupitiriza kulalikira uthenga wabwino, kutenga nawo mbali mokwanira m’ntchito yochitira “umboni kwa anthu a mitundu yonse.”—Mat. 24:14.

5 Kulingalira kwathu ntchito za Yehova kudzawonjezera ukulu wake. Choncho nyadirani mwayi wokhala akuchita Mawu a Mulungu!

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena