Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Helo
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Koma magwero enieni a chiphunzitso chochitira chipongwe Mulungu chimenechi ngwozama kwambiri. Malingaliro auchiwanda ogwirizanitsidwa ndi helo wozunza amasinjirira Mulungu ndipo magwero ake ndiye wosinjirira wamkulu wa Mulungu (Mdyerekezi, dzina limene limatanthauza “Wosinjirira”), iye amene Yesu Kristu anamutcha “Atate wabodza.”—Yoh. 8:44.

  • Imfa
    Kukambitsirana za m’Malemba
    • Imfa

      Tanthauzo: Kulekeka kwa kugwira ntchito konse kwa moyo. Pamene kupuma, kugunda kwamtima, ndi kugwira ntchito kwa ubongo zileka, mphamvu ya moyo pang’ono ndi pang’ono imaleka kugwira ntchito m’maselo athupi. Imfa ndiyo kusiyana ndi moyo.

      Kodi munthu analengedwa ndi Mulungu kuti afe?

      Mosemphana ndi zimenezi, Yehova anachenjeza Adamu kusakhala wosamvera, kumene kukanatsogolera ku imfa. (Gen. 2:17) Pambuyo pake, Mulungu anachenjeza Aisrayeli motsutsana ndi kudzisungira kumene kukanatsogolera ngakhale ku imfa yamwamsanga kwa iwo. (Ezek. 18:31) M’nthaŵi yokwanira anatumiza Mwana wake kukafera anthu kotero kuti awo amene akakhulupirira m’kakonzedwe kameneka akakhale nawo moyo wosatha.—Yoh. 3:16, 36.

      Salmo 90:10 limanena kuti nthaŵi yozoloŵereka ya moyo wamunthu ndiyo zaka 70 kapena 80. Zimenezo zinali zowona pamene Mose analemba, koma sizinali choncho kuyambira pachiyambi. (Yerekezerani ndi Genesis 5:3-32.) Ahebri 9:27 amati: “Popeza kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi.” Izinso, zinali zowona pamene zinalembedwa. Koma sizinali choncho Mulungu asanapereke chiŵeruzo pa Adamu wochimwayo.

      Kodi nchifukwa ninji timakalamba ndi kufa?

      Yehova analenga anthu aŵiri oyamba ali angwiro, okhala ndi chiyembekezo cha kukhala ndi moyo kosatha. Anapatsidwa ufulu wakudzisankhira. Kodi akamvera Mlengi wawo mwachikondi ndi chiyamikiro kaamba ka zonse zimene anali atawachitira? Iwo anali oti nkukhoza kotheratu kuchita choncho. Mulungu anauza Adamu kuti: “Koma mtengo wakudziŵitsa zabwino ndi zoipa usadye umenewo; chifukwa tsiku lomwe udzadye umenewo udzafa ndithu.” Mogwiritsira ntchito njoka monga

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena