-
Kukonzekera Nkhani ya Wophunzira mu SukuluPindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
-
-
Kukonzekera Nkhani ya Wophunzira mu Sukulu
NKHANI iliyonse m’sukulu imapereka mwayi wokuthandizani kupita patsogolo. Dziperekeni ndi mtima wonse, ndipo kupita kwanu patsogolo kudzaonekera kwa inu mwininu ndi kwa ena. (1 Tim. 4:15) Sukuluyi idzakuthandizani kukulitsa maluso anu.
Kodi mumachita mantha kulankhula pamaso pa mpingo? Zimenezo n’zachibadwa, ngakhale kuti mwakhala m’sukuluyi nthaŵi yaitali. Komabe, zilipo njira zimene mungachepetsere mantha anu. Kunyumba, khalani ndi chizoloŵezi choŵerenga mokweza kaŵirikaŵiri. Pamisonkhano yampingo, yankhani kaŵirikaŵiri, ndipo ngati ndinu wofalitsa, pitani nawoni nthaŵi zonse mu utumiki wa kumunda. Njira zimenezi zidzakuthandizani kuzoloŵera kulankhula pamaso pa anthu. Kuwonjezera apo, konzekerani nkhani zanu za wophunzira nthaŵi ikalipo, ndipo yesezani kuzikamba motulutsa mawu. Kumbukirani kuti muzikalankhula pamaso pa omvera aubwenzi. Ndipo musanakambe nkhani ina iliyonse, pempherani kaye kwa Yehova. Iye amapereka mokondwa mzimu woyera kwa atumiki ake amene amaupempha.—Luka 11:13; Afil. 4:6, 7.
Musayembekezere kuchita zodabwitsa. Kukhala wokamba bwino nkhani ndi mphunzitsi waluso kumatenga nthaŵi. (Mika 6:8) Ngati munalembetsa posachedwa m’sukuluyi, musayembekezere kuti mukakamba nkhani yothyakuka bwino kuyamba n’kuyamba. M’malo mwake limbikirani mfundo imodzi ya chilangizo cha kalankhulidwe panthaŵi imodzi. Ŵerengani ndi kumvetsetsa gawo la m’buku lino limene limafotokoza mfundo ya chilangizo imeneyo. Ngati n’kotheka, chitani zimene zandandalikidwa pambali yakuti “Zochita.” Zimenezi zidzakuthandizani kuzoloŵera luso limenelo la kalankhulidwe musanakakambe nkhani yanu kumpingo. Kumbukirani, kupita patsogolo kumadza ndi kudekha.
Kukonzekera Mbali ya Kuŵerenga
Kukonzekera kuŵerenga pamaso pa anthu kumalira zambiri, kusiyana ndi kungotchula mawu mmene awalembera m’nkhaniyo. Yesetsani kumvetsetsa zimene mukuŵerengazo. Mukangolandira mbali imeneyo, iŵerengeni mobwerezabwereza ndi cholinga chimenecho. Yesani kumvetsetsa mfundo ya sentensi iliyonse ndi lingaliro limene akulimveketsa m’ndime iliyonse. Mukatero mudzamveketsa malingalirowo molondola ndi mzimu wake. Ngati n’kotheka, yang’anani mu mtanthauzira mawu, kuti mudziŵe katchulidwe ka mawu osazoloŵereka. Imvetseni bwino nkhaniyo. Makolo angafunikire kuthandiza ana awo kuti achite zimenezi.
Kodi mumapatsidwa mbali zoŵerenga Baibulo kapena ndime m’nkhani za mu Nsanja ya Olonda? Ngati zoŵerengazo zilipo pamakaseti m’chinenero chanu, mungathandizike kwambiri ngati mumvetsera kaŵerengedweko ndi kusamala zinthu ngati katchulidwe ka mawu, kalankhulidwe, mmene amatsindikira mawu, komanso kakwezedwe ndi katsitsidwe ka mawu. Ndiyeno yesani maluso ameneŵa pakuŵerenga kwanu.
Mukayamba kukonza nkhani yanu, onetsetsani kuti mwaŵerenga ndi kumvetsetsa phunziro limene limafotokoza luso la kulankhula limene mwauzidwa kuti mukonzekere. Ngati n’kotheka, ŵerenganinso phunzirolo mutayeseza kangapo kuŵerenga momveka mbali imene mwapatsidwayo. Yesetsani kugwiritsa ntchito malangizo onse olembedwawo.
Maphunziro ameneŵa adzakuthandizani kwambiri mu utumiki wa kumunda. Pamene muli mu ulaliki, mumakhala ndi mwayi wochuluka woŵerenga kwa anthu ena. Popeza kuti Mawu a Mulungu ali ndi mphamvu yosintha miyoyo ya anthu, m’pofunika kuti muziwaŵerenga bwino. (Aheb. 4:12) Musayembekezere kudziŵa maluso onse a kaŵerengedwe pamene mwaŵerenga kamodzi kapena kaŵiri kokha ayi. Mtumwi Paulo analembera mkulu wa mumpingo komanso wodziŵa kuti: “Usamalire kuŵerenga.”—1 Tim. 4:13.
Kukonzekera Nkhani Yokambirana
Mukapatsidwa nkhani yokambirana m’sukulu, kodi mungaikonzekere motani?
Pali zinthu zitatu zofunika kuziganizira: (1) nkhani imene mwapatsidwa, (2) mtundu wake wa makambirano ndi munthu amene mudzakambirana naye, ndipo (3) mfundo ya chilangizo imene munapatsidwa kuti mukonzekere.
Muyenera kusanja mfundo pankhani imene mwapatsidwa. Koma musanafike patali, lingalirani mofatsa za mtundu wa makambirano anu ndi munthu amene mudzakambirane naye. Zimenezi n’zofunika chifukwa zidzakhudza kwambiri mfundo zimene mudzafotokoze ndi njira imene mudzazifotokozere. Kodi makambirano anu adzakhala a mtundu wanji? Kodi adzakhala osonyeza mmene mungalalikire uthenga wabwino kwa munthu amene mumam’dziŵa kale? Kapena adzakhala osonyeza mmene mungachitire pokambirana ndi munthu kwa nthaŵi yoyamba? Kodi munthuyo ndi wamkulu kapena wamng’ono kwa inu? Kodi angakhale ndi maganizo otani pankhani imene mukufuna kukambirana naye? Kodi angakhale akudziŵa zochuluka motani pankhaniyo? Kodi cholinga chanu n’chiyani pamapeto pa makambiranowo? Mayankho pa mafunso ameneŵa adzakuthandizani mmene mungakonzekerere.
Kodi mfundo za nkhani imene mwapatsidwa mungazipeze kuti? Pamasamba 33 mpaka 38 a buku lino, tafotokozapo “Mmene Mungafufuzire.” Ŵerengani gawo limenelo ndi kugwiritsa ntchito zida zofufuzira zimene mungapeze. Kaŵirikaŵiri mudzapeza mfundo zochuluka kuposa zimene mungazigwiritse ntchito. Ŵerengani mokwanira kuti mupeze mfundo zoyenerera kwambiri. Komabe mmene mukutero, kumbukirani mtundu wa makambirano a nkhani yanu komanso munthu amene mudzakambirane naye. Lembani mzera kunsi kwa mfundo zoyenera kugwiritsa ntchito.
Musanasankhe komaliza mfundo zoyenerera ndi kuiyala nkhani yanu, ŵerengani mofatsa nkhani yofotokoza luso la kulankhula limene munapatsidwa kuti mulikonzekere. Kugwiritsa ntchito kwanu luso limenelo pankhani yanu ndiko chimodzi mwa zifukwa zazikulu zokupatsirani nkhaniyo.
Mukakakamba mfundo zanu m’nthaŵi imene mwapatsidwa, mudzakhala ndi mpata wabwino wokamba mawu omaliza, chifukwa adzakupatsani chizindikiro chosonyeza kuti nthaŵi yanu yakwana. Komabe, pamene muli mu utumiki wa kumunda, nthaŵi siikhala nkhani yaikulu. Choncho pamene mukukonzekera, ganizirani za nthaŵi, koma makamaka samalani za luso la kuphunzitsa.
Mawu Pang’ono za Mtundu wa Makambirano. Pendani njira zosonyezedwa patsamba 82, ndipo sankhanipo imodzi imene ingakhale yogwira mtima kwa inu mu ulaliki komanso imene ingakuthandizeni kugwiritsa ntchito bwino mfundo za nkhani imene mwapatsidwa. Ngati mwakhala m’sukuluyi kwa nthaŵi yotalikirapo, umenewu ukhale mwayi wanu wakuti muchite khama ndi kuwonjezera maluso ena mu ulaliki.
Ngati woyang’anira Sukulu ya Utumiki akusankhirani mtundu wa makambirano, landirani musaope. Makambirano ambiri a m’nkhani amakhala ochita ulaliki. Ngati simunachitepo ulaliki umene akupatsaniwo, funsirani kwa ofalitsa amene anauchitapo. Ngati n’kotheka, yesani kukambirana nkhani imene mwapatsidwayo m’njira yofanana ndi imene mudzagwiritse ntchito m’sukulu. Zimenezi zidzakuthandizani kupeza cholinga chenicheni cha kuphunzira kwanu.
Pamene Nkhani Yanu Ili Yokamba Nokha
Ngati ndinu mwamuna, mungapatsidwe nkhani yaifupi yokaikamba ku mpingo. Pokonzekera nkhani ngati zimenezi, mfundo zoyambirira kuziganizira n’zofanana ndi zimene tafotokoza m’nkhani zokambirana za wophunzira. Kusiyana kwakukulu kumene kulipo ndiko omvera ndi kakambidwe basi.
Kumakhala bwino kukonzekera m’njira yoti aliyense mwa omvera akapindule. Ambiri omwe amakhalapo ndi oti amadziŵa kale ziphunzitso zoyambirira za m’Baibulo. Angakhale akudziŵapo zambiri pa nkhani imene munapatsidwa kuti muikambe. Ganizirani zimene akuzidziŵa kale m’nkhaniyo. Yesetsani kupeza njira imene mungawapindulitsire nayo. Dzifunseni kuti: ‘Kodi nkhani yangayi ndingaigwiritse ntchito motani kuti ndizamitse chidziŵitso changa ndi cha omvera anga pa makhalidwe a Yehova? Kodi ndi mfundo ziti zimene zingatithandize kuzindikira chifuniro cha Mulungu? Kodi nkhaniyi ingatithandize motani kupanga zosankha zanzeru m’dzikoli lodzaza zilakolako za thupi?’ (Aef. 2:3) Kupeza mayankho okhutiritsa pa mafunso ameneŵa kumalira kufufuza. Pamene mukugwiritsa ntchito Baibulo, musangoŵerenga malemba n’kuthera pomwepo. Lingalirani pamalembawo, ndipo sonyezani mmene akuperekera umboni pa mfundo zanu. (Mac. 17:2, 3) Musakhale ndi mfundo zochuluka kwambiri. Zifotokozeni m’njira yosavuta kuzikumbukira.
Pokonzekera muyenera kuganiziranso za mmene mukalankhulire. Mfundo imeneyi musaichepetse. Yesezani kukamba nkhani yanu motulutsa mawu. Khama limene mumaika pa kuŵerenga ndi kugwiritsa ntchito malangizowo pa maluso osiyanasiyana a kalankhulidwe lidzakuthandizani kwambiri kupita patsogolo. Kaya mwayamba posachedwa kukamba nkhani kapena munayamba kale, konzekerani bwino kuti mukalankhule mwachidaliro ndi mzimu wake wa nkhaniyo. Pamene mukukamba nkhani iliyonse m’sukulu, kumbukirani cholinga chogwiritsira ntchito mphatso ya kulankhula yochokera kwa Mulungu, kutamanda Yehova.—Sal. 150:6.
-
-
Kukonzekera Nkhani Zokambira MpingoPindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
-
-
Kukonzekera Nkhani Zokambira Mpingo
SUKULU ya Utumiki wa Mulungu inakonzedwa ndi cholinga chopindulitsa mpingo wonse. Nkhani zopindulitsa zimakambidwanso pamisonkhano ina yampingo ndi pamisonkhano ikuluikulu. Mukapatsidwa gawo pamisonkhano imeneyi, dziŵani kuti mwapatsidwa udindo waukulu kwambiri. Mtumwi Paulo analimbikitsa woyang’anira wachikristu Timoteo kuti asamalire chiphunzitso chake mosalekeza. (1 Tim. 4:16) Amene amafika pamisonkhano yachikristu amakhala atapatula nthaŵi yofunika kwambiri—ndipo ena amakhala atavutikirapo kwambiri—chonsecho kuti adzalandire malangizo pankhani zokhudza unansi wawo ndi Mulungu. Kupereka malangizo oterowo ndi mwayi wosaneneka! Kodi mungausamalire bwino motani?
Mfundo Zazikulu za Kuŵerenga Baibulo
Mbali imeneyi ya sukulu imachokera pa kuŵerenga Baibulo kwa mlungu uliwonse. M’pofunika kwambiri kuunika mmene mfundozo zimatikhudzira lerolino. Monga momwe timaŵerengera pa Nehemiya 8:8, Ezara ndi anzake aja anaŵerengera anthu Mawu a Mulungu, akumawafotokozera, ‘nawatanthauzira,’ ndi kuwathandiza kumvetsa mawuwo. Pamene mukamba mfundo zazikulu za m’Baibulo, mumakhala ndi mwayi wakuchita zofananazo.
Kodi mungaikonzekere motani nkhani imeneyi? Ngati n’kotheka, ŵerengani gawo la Baibulo limene mwapatsidwalo kukali mlungu umodzi kapena kuposerapo. Kenako ganizirani za mpingo wanu ndi zosoŵa zake. Musaiŵale kuipempherera. Kodi ndi uphungu uti, ndi zitsanzo ziti, ndi mfundo za makhalidwe abwino ziti m’gawo limeneli la Mawu a Mulungu zimene zingathandize pa zosoŵa zimenezo?
Apanso kufufuza n’kofunikira. Mungagwiritse ntchito mlozera nkhani wa kumapeto kwa chaka wa mu Nsanja ya Olonda. Mwa kufufuza zimene zinafalitsidwa pamavesi amene mwasankhawo, mungapeze mfundo zina zounika bwino nkhaniyo, mafotokozedwe a maulosi okwaniritsidwa, mfundo zimene nkhani zina zimaunika zokhudza Yehova, kapena malongosoledwe a mfundo za makhalidwe abwino. Musalembe mfundo zambiri. Ikani maganizo pa mavesi oŵerengeka chabe amene mwasankha. Ndi bwino kulemba mfundo zoŵerengeka ndi kuzikamba bwino.
Nkhaniyi imaphatikizaponso kupempha omvera kuti alankhulepo mmene apindulira ndi kuŵerenga Baibulo kwa mlunguwo. Kodi anapeza mfundo zotani zimene zingawathandize paphunziro lawo laumwini ndi paphunziro la banja, kapena mu ulaliki wawo kapenanso m’njira zina pamoyo wawo? Ndi makhalidwe otani a Yehova amene anaona m’zochitika za pakati pa Yehova ndi anthu osiyanasiyana, komanso mitundu ya anthu yosiyanasiyana? Kodi omverawo anaphunzirapo chiyani chimene chalimbikitsa chikhulupiriro chawo ndi kuzamitsa chiyamikiro chawo kwa Yehova? Musataye nthaŵi ndi mfundo zovuta kumva zosafunikira kwenikweni. Gogomezani makamaka tanthauzo ndi phindu lenileni la mfundo zimene mwasankhazo.
Nkhani Yolangiza
Imeneyi ingazikidwe pa nkhani yofalitsidwa kale, monga ya mu Nsanja ya Olonda kapena Galamukani! kapena buku lina. Kaŵirikaŵiri, nkhaniyo imakhala ndi mfundo zambiri zosati n’kuzitha m’nthaŵi yoperekedwa. Kodi muyenera kuikamba motani nkhaniyo? Ikambeni ngati mphunzitsi, osati ngati munthu wongofotokoza nkhani chisawawa ayi. Woyang’anira ayenera kukhala “wokhoza kuphunzitsa.”—1 Tim. 3:2.
Yambani kukonzekera mwa kuŵerenga nkhaniyo. Ŵerengani malemba ake. Sinkhasinkhani. Yesetsani kuchita zimenezo nthaŵi ikalipo lisanafike tsiku la nkhani yanu. Kumbukirani kuti abale amalimbikitsidwanso kuŵerengeratu magwero a nkhani yanuyo. Choncho, udindo wanu si kungoibwereza nkhaniyo ayi, kapena kungopereka chidule chake, koma kuonetsa mmene tingagwiritsire ntchito mfundo zake. Fotokozani mfundo zoyenera za nkhaniyo m’njira imene ingapindulitsedi mpingo.
Mmene mwana aliyense amakhalira ndi khalidwe lakelake, mpingo uliwonse umakhalanso ndi makhalidwe amene umadziŵika nawo. Kholo lodziŵa kuphunzitsa silimangobwereza kwa mwana wake mfundo za makhalidwe abwino zoloŵeza pamtima. Limakambirana ndi mwanayo. Limalingalira za khalidwe la mwanayo ndi mavuto amene mwanayo akukumana nawo. Mofananamo, aphunzitsi mumpingo amayesetsa kuzindikira zosoŵa za anthu amene akulankhula nawo ndipo amaperekapo thandizo. Komabe, mphunzitsi wozindikira amapeŵa kupereka zitsanzo zimene zingachititse manyazi wina mwa omverawo. Iye amatchula mapindu omwe amakhalapo poyenda m’njira ya Yehova ndipo amaunika uphungu wa m’Malemba umene ungathandize mpingo kuthana ndi mavuto amene ukukumana nawo.
Kuphunzitsa kwabwino kumakhudza mitima ya omvera. Kuphunzitsa koteroko sikutheka mwa kungotchula mfundo zakutizakuti, koma kuphunzitsa omverawo kuzindikira cholinga cha mfundozo. Kumafunanso kukhala ndi chidwi chenicheni pa awo amene akuphunzitsidwa. Abusa auzimu ayenera kudziŵa nkhosa zawo. Ngati mwachikondi amakumbukira mavuto amene anthu osiyanasiyana amakumana nawo, adzakhoza kulankhula mowalimbikitsa, akumasonyeza kuti amamvetsa mkhalidwe wawo, amawamvera chifundo, ndipo amawaganizira.
Monga momwe aphunzitsi aluso amadziŵira, nkhani iyenera kukhala ndi cholinga chomveketsedwa bwino lomwe. Nkhani iyenera kukambidwa m’njira younika bwino mfundo zazikulu kuti zikakumbukike. Omverawo ayenera kumakumbukira malingaliro othandiza amene adzakhudza miyoyo yawo.
Msonkhano wa Utumiki
Pokamba nkhani yochokera mu Utumiki Wathu wa Ufumu, udindo wanu ungakhale wosiyanako. Apa, si kwa inu kwenikweni kusankha mfundo zoyenerera. Kwanu n’kufotokozera mokwanira omvera anu zimene zalembedwa kale. Thandizani omvera kulingalira pa malemba amene ali maziko a uphungu uliwonse umene waperekedwa. (Tito 1:9) Nthaŵi imakhala yochepa, moti kaŵirikaŵiri siidzakulolani kuwonjezerapo mfundo zina.
Komanso, nthaŵi zina mungapemphedwe kukamba nkhani yosachokera mu Utumiki Wathu wa Ufumu. Nkhaniyo ingachokere mu Nsanja ya Olonda, kapena angangokupatsani mfundo zina pang’ono. Monga mphunzitsi, ndi udindo wanu kulingalira zosoŵa za mpingo mogwirizana ndi nkhani imene mwapatsidwayo. Mungafune kugwiritsa ntchito chitsanzo chachidule koma cholunjika pa mfundo, kapena mungasimbe chochitika choyenerera. Kumbukirani kuti udindo wanu si kungofotokoza mfundo za nkhaniyo, koma kukamba nkhaniyo m’njira imene idzathandiza mpingowo kugwira ntchito imene yaperekedwa m’Mawu a Mulungu ndi kuti azikondwa poigwira.—Mac. 20:20, 21.
Pamene mukukonzekera nkhani yanu, ganizirani mikhalidwe ya anthu a mumpingo wanu. Ayamikireni pa zimene amachita. Kodi angakulitse motani luso lawo ndi chisangalalo chawo mu ulaliki ngati agwiritsa ntchito malingaliro operekedwa m’nkhaniyo?
Kodi nkhani yanu ili ndi chitsanzo kapena mbali yokhala ndi anthu oti muwafunse mafunso? Ngati zili choncho, ziyenera kukonzedwa bwino nthaŵi ikalipo. Mungafune kupempha munthu wina kuti akonze mbali zimenezo, koma kachitidweko kaŵirikaŵiri sikakhala ndi mapindu
-