-
Chithandizo kwa Omafawo m’Nyengo Yathu YamakonoGalamukani!—1991 | November 8
-
-
Chithandizo kwa Omafawo m’Nyengo Yathu Yamakono
MKAZIYO, dokotala iyemwiniyo, anali atangochoka kumene m’chochitika chopweteka koposa. Iye adawona gogo wake wachikazi akufa m’chipinda cha m’chipatala cha odwala mosachiritsika pambuyo pa opaleshoni ya kansa imene “iwo sanaifune konse.”
“Misozi yanga pa maliro awo sinali chifukwa cha imfa yawo, pakuti gogo wanga wachikazi anali atakhala ndi moyo wautali, wokwanira,” dokotalayo analemba motero. “Ndinalira chifukwa cha ululu umene iwo anapirira, ndipo chifukwa cha kusakwaniritsidwa kwa zofuna zawo. Ndinalirira amayi ŵanga ndi ana awo, chifukwa cha lingaliro lawo la kutayikiridwa kwawo ndi kugwiritsidwa mwala.”
Komabe, inu mungafune kudziŵa, ponena za kuthekera kwa kuthandiza munthu wodwala mosachiritsika woteroyo. Dokotalayu akupitiriza kuti:
“Kwakukulukulu, ndinadzilirira: chifukwa cha liwongo lalikulu limene ndinamva pa kusakhoza kuwapulumutsa ku ululu ndi kuzunzika, ndi chifukwa cha kupereŵera kowopsa kumene ndinamva monga dokotala, wosakhoza kuchiritsa, wosakhoza kuchepetsa kuvutika. Pakuti palibe kulikonse m’maphunziro anga kumene ndinaphunzitsidwa kulandirika kwa imfa kapena kumwalira. Utenda unali mdani—woyenera kulimbana naye panthaŵi iriyonse, ndi mphamvu iriyonse yotsirizira. Imfa inali chigonjetso, kulephera; nthenda yalizunzo chikumbutso chosalekeza cha kusoŵa mphamvu kwa dokotala. Chithunzithunzi cha gogo wanga wachikazi wokondedwa chondiyang’ana ndi maso owopsedwa pamene anali pa makina opeperera mu ICU chimandifikirafikira kufikira lerolino.”
Mdzukulu wamkazi wachikondi ameneyu anayambitsa nkhani yocholoŵana yamakhalidwe, yazamankhwala ndi zalamulo imene tsopano ikukambitsiridwa m’makhoti ndi zipatala kuzungulira dziko lonse: Kodi nchiyani chimene chiri chabwino koposa kaamba ka odwala opanda chiyembekezo m’nyengo yathu yopita patsogolo mwaluso lazopangapanga?
Ena ali ndi lingaliro lakuti zirizonse zothekera mwazamankhwala ziyenera kuchitidwa kaamba ka munthu aliyense amene akudwala. Lingaliro limeneli likunenedwa ndi Association of American Physicians and Surgeons kuti: “Thayo la dokotala kwa wodwala wokomoka, wotsiruka, kapena chirema silimadalira pa chiyembekezo cha kuchira. Dokotalayo nthaŵi zonse ayenera kuchitapo kanthu mokomera ubwino wa wodwalayo.” Zimenezi zimatanthauza kupereka mankhwala onse kapena chithandizo chamankhwala chimene chingaperekedwe mothekera. Kodi mukulingalira kuti zimenezi nthaŵi zonse nzabwino koposa kwa munthu amene akudwala kwakukulu?
Kwa anthu ochuluka njirayo imamvekeradi kukhala yoyamikirika. Komabe, m’zaka makumi oŵerengeka apitawo, kuchita ndi mankhwala opititsidwa patsogolo ndi luso lazopangapanga kwadzutsa lingaliro latsopano ndi losiyana. Mu pepala la 1984 losonyeza posinthira lokhala ndi mutu wakuti “Thayo la Dokotala Kwa Odwala Opanda Chiyembekezo,” gulu la madokotala khumi odziŵa linati: “Kutsika m’kupatsidwa mankhwala kwamphamvu kwa wodwala wopanda chiyembekezo kuli koyenera pamene kupatsidwa mankhwala koteroko kukangotalikitsa njira ya kumwalira yovuta ndi yopweteka.” Zaka zisanu pambuyo pake madokotala amodzimodziwo anafalitsa nkhani ya mutu umodzimodziwo imene inatchedwa “Lingaliro Lachiŵiri.” Polingalira vuto limodzimodzilo, iwo ananena mawu omvekera bwino: “Madokotala ochuluka ndi akatswiri azamakhalidwe . . . chifukwa cha chimenecho, anena kuti kuli bwino kuleka kudyetsa ndi kuthirira [madzi] odwala omafa akutiakuti, odwala mosachiritsika, kapena okomoka mwachikhalire.”
Sitinganyalanyaze mawu oterowo kukhala kupeka chabe kapena kukhala nthanangula chabe zimene ziribe chochita ndi ife. Akristu ambiri ayang’anizana ndi zosankha zovuta m’nkhaniyi. Kodi wodwala mopanda chiyembekezo wokondedwayo ayenera kukhalitsidwa moyo ndi makina othandizira kupuma? Kodi kudyetsera m’mitsempha kapena njira zodyetsera zosakhala zachibadwa ziyenera kugwiritsiridwa ntchito kwa wodwala mosachiritsika? Pamene mkhalidwewo uli wopanda chiyembekezo, kodi ndalama zonse za wachibale, kapena za banja lonse, ziyenera kuwonongedwera kulipirira kupatsidwa mankhwala, mwinamwake kophatikizapo kupita kumalo akutali kukalandira chisamaliro chazamankhwala chopititsidwa patsogolo?
Mosakaikira inu mukuzindikira kuti mafunso oterowo sali osavuta kuyankha. Monga momwe mukafunira kuthandiza bwenzi lodwala kapena wokondedwa, ngati munafunikira kuyang’anizana ndi mafunso ameneŵa inu mungafune kudziŵa kuti: ‘Kodi Mkristu ali ndi chitsogozo chotani? Kodi ndimagwero otani amene alipo kaamba ka chithandizo? Chofunika koposa, kodi Malemba amanenanji pankhaniyo?’
-
-
Kodi Pali Chithandizo Chotani kwa Odwala Mosachiritsika?Galamukani!—1991 | November 8
-
-
Kodi Pali Chithandizo Chotani kwa Odwala Mosachiritsika?
M’NTHAŴI zaposachedwapa lingaliro la anthu ponena za imfa ndi kumwalira lakhala likusintha m’mbali zambiri za dziko.
Nthaŵi zakale madokotala anavomereza imfa monga mapeto osapeŵeka a utumiki wawo kwa odwala—mapeto oyenera kufeŵetsedwa, ndipo kaŵirikaŵiri oyenera kusamaliridwa panyumba.
Posachedwapa kwambiri, pogogomezera luso ndi kuchiritsa, ogwira ntcito yazipatala afikira pakuwona imfa kukhala kulephera kapena kugonjetsedwa. Choncho cholinga chachikulu cha ntchito yazamankhwala chakhala chija cha kuletsa imfa pamtengo uliwonse. Limodzi ndi kusintha kumeneku panadzayamba kubuka kwa luso latsopano kotheratu la kuchititsa anthu kukhala ndi moyo motalikirapo koposa mmene kukanakhalira kothekera kalelo.
Luso lazamankhwala ladzetsa kupita patsogolo kosakanika m’maiko ambiri; komabe, ladzutsa kunyumwira kowopsa. Dokotala wina ananena kuti: “Madokotala ochuluka ataya chinthu chofunika chimene chinali mbali yokondeka ya mankhwala, ndipo chimenecho ndicho chifundo. Makina, kugwira ntchito bwino ndi kulondoloza zachotsa mumtima kukondwera, chifundo, chisoni, ndi kudera nkhaŵa kaamba ka munthuyo. Mankhwala tsopano ndiwo sayansi yosakondweretsa; ukoma wake uli wa nyengo ina. Munthu womafayo angapeze chitonthozo chochepa kwa dokotala wamakina.”
Limenelo ndilingaliro chabe la munthu mmodzi, ndipo ndithudi sichitsutso chadziko lonse cha madokotala. Komabe, mwina mwawona kuti anthu ochuluka akhala ndi mantha akukhalitsidwa amoyo ndi makina.
Pang’onong’ono lingaliro lina linayamba kumveka. Linali lakuti m’zochitika zina anthu ayenera kuloledwa kufa mwachibadwa, mwaulemu, ndi mosadodometsedwa ndi zithandizo zamakina. Kupenda kochitidwira magazini a Time kunavumbula kuti oposa chigawo chimodzi mwa zitatu cha ofikiridwa analingalira kuti dokotala ayenera kuloledwa kuleka kupereka mankhwala ochirikiza moyo kwa wodwala mosachiritsika. Kupendako kunafika pamawu aŵa: “Atadzipereka ku zosapeŵeka, [anthu] amafuna kufa mwaulemu, osamangirirdwa ku gulu la makina m’chipinda cha odwala mosachiritsika monga chinthu chopendedwa mkati mwa galasi.” Kodi mukuvomereza? Kodi zimenezo zigwirizana motani ndi lingaliro lanu pankhaniyi?
Mayankho Olingaliridwa
Kumadalira pa mwambo wa munthu kapena chitaganya kumene anakulira, pali kusiyana kwakukulu m’kulingalira nkhani ya imfa ndi kumwalira. Komabe, anthu m’maiko ambiri akusonyeza chikondwerero chowonjezereka m’vuto la odwala mosachiritsika. M’zaka zingapo zapitazo, akatswiri amakhalidwe, madokotala, ndi anthu onse achirikiza zoyesayesa kusintha kusamaliridwa kwa ovutika oterowo.
Pakati pa njira zochuluka zopendedwa kuti athetse nkhaniyi, yogwiritsiridwa ntchito koposa m’zipatala zina ndiyo njirayo “Do Not Resuscitate” (Musatsitsimutse), kapena DNR. Kodi mukudziŵa zimene imeneyi imaphatikiza? Pambuyo pakukambitsirana kwakukulu ndi banja la wodwalayo, ndipo makamakanso ndi wodwalayo, malingaliro otsimikizirika apasadakhale amapangidwa, ndipo ameneŵa amalembedwa patchati cha wodwalayo. Zimenezi zimasumikidwa pa ziletso zimene zidzaikidwa pazoyesayesa za kudzutsanso, kapena kutsitsimula, wodwala wopanda chiyembekezoyo ngati mkhalidwe wake ungaipirepo.
Pafupifupi aliyense amazindikira kuti chinthu chachikulu m’zosankha zovuta zoterozo chiyenera kukhala “Kodi nchiyani chimene wodwalayo akafuna kuti chichitidwe?” Komabe, chimene chimalipanga kukhala vuto lowopsa nchakuti kaŵirikaŵiri wodwalayo amakhala wosazindikira kapena mwinamwake wosakhoza kupanga zosankha zake zanzeru. Zimenezi zachititsa cholembedwa chimene chingatchedwe chosankha chenicheni. Ncholinganizidwa kulola anthu kufotokoza mwatsatanetsatane pasadakhale mankhwala amene akafuna m’masiku awo otsiriza. Mwachitsanzo, chosankha choterocho chinganene kuti:
“Ngati ndingakhale ndi mkhalidwe wosachiritsika kapena wosakhoza kusinthika umene udzadzetsa imfa yanga mkati mwa nthaŵi yaifupi kwambiri, nchikhumbo changa kuti moyo wanga usatalikitsidwe mwakugwiritsira ntchito njira zochirikiza moyo. Ngati mkhalidwe wanga uli wokhoza kufa ndipo ndine wosakhoza kupanga zosankha zokhudza kuchiritsidwa kwanga, ndilangiza dokotala wondisamalira kusapereka kapena kuchotsa njira zimene zingangotalikitsa njira yofera ndipo nzosafunika kaamba ka mpumulo wanga kapena kusamva ululu.” Zolembedwa zoterozo zingafotokozedi mwatsatanetsatane mtundu wa njira zochiritsira zimene munthuyo afuna kapena safuna kuti zigwiritsiridwe ntchito mumkhalidwe wosachiritsika.
Zosankha zenizeni zotero, ngakhale kuti sizigwira ntchito mwalamulo mumikhalidwe yonse, zimazindikiridwa m’malo ambiri. Anthu oyerekezeredwa kukhala mamiliyoni asanu mu United States alemba zosankha zenizeni zamankhwala. Akuluakulu m’dziko limenelo amalingalira zimenezi kukhala njira yabwino koposa yopezeka kutsimikizirira kuti zofuna zake zikulemekezedwa ndi kutsatiridwa.
Kodi Ndimtundu Wotani wa Mankhwala Kapena Chisamaliro?
Bwanji ponena za kusamaliridwa kwenikweniko kwa odwala mosachiritsika? Mwinamwake njira yatsopano yapadera koposa yakhala lingaliro lotchedwa hospice, lozindikiridwa mowonjezereka padziko lonse. Koma kodi “hospice” nchiyani?
Mmalo motanthauza malo kapena nyumba, hospice m’lingaliro lino limatanthauza kwenikweni lingaliro kapena programu ya chisamaliro cha odwala mosachiritsika. Latengedwa kuliwu Lachifrenchi chanyengo yapakati lofotokoza malo opumira aulendo. Hospice limasumika panjira yagulu (madokotala, manesi, ndi antchito odzifunira) imene imachita kutsimikizira kuti wodwala mosachiritsika akusungidwa bwino ndipo kwenikweni mopanda ululu, makamaka m’nyumba ya wodwala mwiniyo.
Ngakhale kuli kwakuti mahospice ena amapezeka m’zipatala, ambiri ngodziimira. Ochuluka amagwiritsira ntchito zithandizo zachitaganya, zonga ngati kuchezera manesi, akatswiri azakadyedwe, nduna zaboma, ndi madokotala owongola mafupa. Mmalo mwakugwiritsira ntchito njira zamankhwala zonkitsa, chisamaliro cha hospice chimagogomezera chifundo chachikulu. Mmalo mwa kuchiritsidwa kwamphamvu kwa nthenda ya wodwalayo, chimasumika pa kuchiritsa kwamphamvu ululu wa wodwalayo. Dokotala wina analongosola motere: “Hospice siri chisamaliro chocheperapo kapena chosakhala chisamaliro kapena chisamaliro chotchipa. Ndiyo mtundu wosiyana kotheratu wa chisamaliro.”
Kodi kulabadira kwanu lingaliro limeneli nkotani? Kodi njira imeneyi ikuwonekera kukhala imene mukulingalira kuti iyenera kukambitsiridwa ndi aliyense wa okondedwa anu amene angapezedwe kukhala akuyang’anizana ndi matenda osachiritsika, ndipo mwinamwake limodzi ndi dokotala wophatikizidwa?
Ngakhale kuli kwakuti chisamaliro cha hospice chingakhale chisakupezeka m’dera lanu tsopano, kuthekera nkwakuti chidzatero mtsogolo, pakuti gulu la hospice likukula padziko lonse. Cholingaliridwa poyamba kukhala choyesayesa chotsutsa njira zokhazikitsidwa, chisamaliro cha hospice pang’onopang’ono chaloŵa m’mbali yaikulu ya zamankhwala, ndipo tsopano chikulingaliridwa kukhala njira ina yovomerezedwa ya odwala mosachiritsika. Mwa njira zake zochiritsira, makamaka kugwiritsiridwa ntchito moyenera kwa mibulu yopha ululu, hospice yawonjezera kupita patsogolo kwina kwapadera kuchisamaliro chazamankhwala.
M’kalata yolembedwera New England Journal of Medicine, Dr. Gloria Werth anasimba imfa ya mbale wake mu hospice kuti: “Panthaŵi iriyonse mankhwala, chakudya, kapena madzi sizinakakamizidwe pa mbale wanga. Iye anali waufulu kudya, kumwa, . . . kapena kumwa mankhwala monga momwe anafunira . . . Koma chabwino koposa ponena za hospice nchakuti zikumbukiro zathu za imfa ya Virginia ziri zotsitsimutsa mwapadera ndi zosangalatsa. Kodi zimenezi zinganenedwe kangati mobwerezabwereza pambuyo pa imfa m’chipinda cha odwala mosachiritsika?”
[Mawu Otsindika patsamba 26]
“Mankhwala tsopano ndiwo sayansi yosakondweretsa; ukoma wake uli wa nyengo ina. Munthu womafayo angapeze chitonthozo chochepa kwa dokotala wamakina”
[Mawu Otsindika patsamba 27]
Hospices imasumika pa kuchiritsidwa kwamphamvu kwa ululu wa wodwalayo mmalo mwa kuchiritsidwa kwamphamvu kwa nthenda yeniyeniyo
-
-
Chithandizo Chabwino Koposa Chikupezeka!Galamukani!—1991 | November 8
-
-
Chithandizo Chabwino Koposa Chikupezeka!
KWA Mkristu chosankha ndi ukulu wa chisamaliro cha odwala mosachiritsika zingadzutse mafunso aakulu. Mwachitsanzo:
Kodi kukakhala kosagwirizana ndi malemba kuchita zochepera koposa zonse zothekera kusungitsa moyo? Ndipo ngati kuli kovomerezedwa kulola munthu wina kufa mwachibadwa, popanda kudodometsa kwaukatswiri kotalikitsa moyo, bwanji ponena za kuphera chifundo—kachitidwe kotsimikizirika, kadala kothetsera kuvutika kwa wodwalayo mwakufupikitsadi kapena kuthetsa moyo wake?
M’tsiku lathu ndi nyengo, ameneŵa ndiwo mafunso ofunika. Komabe, sitiri opanda chithandizo powayankha.
Wolemba wouziridwa moyenerera anati: “Mulungu ndiye pothaŵirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m’masautso.” (Salmo 46:1) Zimenezo ziridi choncho kwa ife polingalira nkhani yomwe iripo tsopano. Yehova Mulungu ndiye magwero a chithandizo chanzeru koposa ndi chaukatswiri koposa. Iye wawona miyoyo ya anthu zikwi mamiliyoni ambiri. Amadziŵa—bwinopo koposa dokotala aliyense, katswiri wazamakhalidwe, kapena loyala—chimene chiri chabwino koposa. Choncho tiyeni tiwone chithandizo chimene amapangitsa kupezeka kwa ife.—Salmo 25:4, 5; Ahebri 4:16.
Lingaliro Lolungama la Moyo
Tichita bwino kuzindikira kuti lingaliro la kusungitsa moyo pa mtengo uliwonse silolekezera kwa akatswiri azamankhwala. Liri chotulukapo chachibadwa cha lingaliro lofala lamakono. Nchifukwa ninji ziri choncho? Eya, ngati moyo ulipowu ndiwo wokha umene ulipo, pamenepo kungawonekere kuti moyo wathu weniweniwo uyenera kusungidwa mumikhalidwe iriyonse ndi pa mtengo uliwonse. Koma lingaliro lofala ladziko limeneli mumikhalidwe ina lachititsa zochitika zosasangalatsa—anthu okomoka akumakhalitsidwa “amoyo” pamakina kwazaka zambiri.
Ndiponso, pali ena amene amakhulupirira kusafa kwa moyo waumunthu. Malinga ndi lingaliro lawo, moyo uno uli kokha siteshoni yapanjira ya kuchinthu china chabwinopo. Plato, mmodzi wa oyambitsa lingaliroli, anati:
“Kaya imfa ikhale mkhalidwe wa kusakhalako ndi kusazindikira kotheratu, kapena, monga momwe ambiri amanenera, pamakhala kusintha ndi kusamuka kwa moyo kuchokera padziko lino kumka kulina. . . . Ngati imfa iri ulendo womka kumalo ena, . . . kodi ndiubwino wotani, o abwenzi ndi oŵeruza anga, umene ungakhale waukulu koposa umenewu?”
Munthu wokhala ndi kukhulupirira kotero angawone imfa monga bwenzi, yoyenera kulandiridwa ndipo mwinamwake ngakhale kufulumizidwa. Komabe, Baibulo limaphunzitsa kuti moyo ngwopatulika kwa Yehova. “Pakuti chitsime cha moyo chiri ndi inu,” wamasalmo wouziridwa analemba motero. (Salmo 36:9) Pamenepa, kodi Mkristu wowona ayenera kuvomereza kukhala ndi phande m’kuphera chifundo?
Ena amalingalira kuti pali chisonyezero Chamalemba chankhaniyi pamene Mfumu Sauli, wovulazidwa kwambiri, anachonderera wonyamula zida wake kumupha. Iwo alingalira zimenezi kukhala mpangidwe wa kuphera chifundo, kachitidwe kadala kofulumizira imfa ya munthu wina amene anali kale kumafa. Pambuyo pake Mwamaleki anadzinenera kukhala atalolera pempho la Sauli kuti aphedwe. Koma kodi Mwamaleki ameneyo analingaliridwa kukhala atachita bwino kuthetsa kuvutika kwa Sauli? Kutalitali. Davide, wodzozedwa wa Yehova, analamula kuti Mwamaleki ameneyu aphedwe chifukwa cha liwongo lamwazi. (1 Samueli 31:3, 4; 2 Samueli 1:2-16) Pamenepo, chochitika Chabaibulo chimenechi sichimalungamitsa mwanjira ina iriyonse kukhala ndi phande kwa Mkristu m’mbali iriyonse ya kuphera chifundo.a
Komabe, kodi zimenezi zimatanthauza kuti Mkristu ayenera kuchita zirizonse zothekera mwaluso kutalikitsa moyo umene ulinkutha? Kodi munthu ayenera kutalikitsa njira yofera monga momwe kungathekere? Malemba amaphunzitsa kuti imfa, siri bwenzi la munthu, koma mdani. (1 Akorinto 15:26) Ndiponso, akufa sakuvutika ndipo sakusangalala, koma ali mumkhalidwe wofanana ndi tulo. (Yobu 3:11, 13; Mlaliki 9:5, 10; Yohane 11:11-14; Machitidwe 7:60) Ziyembekezo za moyo zamtsogolo za akufa zimadalira kotheratu pa mphamvu ya Mulungu yowaukitsa kupyolera mwa Yesu Kristu. (Yohane 6:39, 40) Motero tikupeza kuti Mulungu watipatsa chidziŵitso chothandizachi: Imfa sichinthu choyenera kulakalakidwa, koma palibenso thayo lakutembenukira kuzoyesayesa zosaphula kanthu zakutalikitsira njira yofera.
Zitsogozo Zachikristu
Kodi Mkristu angagwiritsire ntchito zitsogozo ziti m’chochitika kumene wokondedwa ali mumkhalidwe wakufa?
Choyamba, tiyenera kuzindikira kuti mkhalidwe uliwonse pawokha wophatikiza uthenda wosachiritsika ngwosiyana, wosiyana kwambiri, ndipo palibe malamulo okhudza yonseyo. Ndiponso, Mkristuyo ayenera kusamala kulingalira malamulo adzikolo m’nkhani zoterozo. (Mateyu 22:21) Kumbukiraninso kuti palibe Mkristu wachikondi amene angachirikize kunyalanyazidwa kwa zamankhwala.
Kokha pamene pali nthenda yosachiritsika yotsimikizirika (kumene mkhalidwe watsimikiziridwa bwino lomwe kukhala wopanda chiyembekezo) kulingalira kuyenera kuperekedwa ku kupempha kuti luso lochirikiza moyo liimitsidwe. Mumikhalidwe yotero palibe chifukwa Chamalemba choti nkuumirira paluso lazamankhwala limene likangotalikitsa njira yofera imene iri yopita patsogolo koposa.
Kaŵirikaŵiri imeneyi ndimikhalidwe yovuta kwambiri ndipo ingaphatikizepo zosankha zovutitsa maganizo. Mwachitsanzo, kodi munthu angadziŵe motani pamene mkhalidwe uli wopanda chiyembekezo? Ngakhale kuli kwakuti palibe aliyense amene angakhale wotsimikizira kotheratu, nzeru iyenera kugwiritsiridwa ntchito pamodzi ndi uphungu wosamalitsa. Pepala lina lazamankhwala lolangiza madokotala limati:
“Ngati pali kusamvana ponena za mapendedwe anthenda kapena zizindikiro zake zapasadakhale kapena zonse ziŵiri, njira yochirikizira moyo iyenera kupitirizidwa kufikira kuvomerezana koyenera kutafikiridwa. Komabe, kuumirira pakutsimikizirika kopambana mlingo woyenera kungalefule maganizo a dokotala amene akuchita ndi zosankha zachisamaliro chazamankhwala mwachiwonekere m’zochitika zopanda chiyembekezo. Lipoti lakamodzikamodzi la wodwala wokhala ndi mkhalidwe wofanana amene anapulumuka sindilo chifukwa chachikulu chopitirizira chisamaliro chazamankhwala champhamvu. Kuthekera kwaziŵerengero zazing’ono zoterozo sikumaposa ziyembekezo zoyenera za chotulukapo chimene chidzatsogolera zosankha zachisamaliro chazamankhwala.”
M’vuto lotero, Mkristuyo, kaya wodwala kapena wachibale, moyenerera akayembekezera chithandizo chakutichakuti kuchokera kwa dokotala wake. Pepala lazamankhwala limeneli likumaliza kuti: “Mulimonse mmene zingakhalire, kuli kosalungama kungopereka ziŵerengero za zenizeni zamankhwala ndi zosankha ndi kusiya wodwalayo ali wokaikaika wopanda chitsogozo chirichonse chowonjezereka chonena za njira zina zogwira ntchito ndi zosagwira ntchito.”
Akulu Achikristu amumpingomo, pokhala aminisitala achikulire, angakhalenso othandiza kwambiri. Ndithudi, wodwalayo ndi banja lake lenileni ayenera kupanga chosankha chawochawo cholama mumikhalidwe yogwedeza maganizo imeneyiyo.
Potsirizira, sinkhasinkhani mfundo zimenezi. Akristu amafunitsitsa kukhalabe ndi moyo kotero kuti asangalale ndi kutumikira Mulungu. Komabe, iwo amazindikira kuti m’dongosolo lamakonoli, tonsefe tikufa; m’lingaliro limeneli tonsefe ndife odwala mosachiritsika. Kuli kokha mwa mwazi wansembe wa Yesu Kristu chakuti tiri ndi chiyembekezo chirichonse cha kusintha mkhalidwewo.—Aefeso 1:7.
Ngati imfa ifikiradi wokondedwa, zovuta monga momwe zimenezi ziriri, sitimasiidwa tikuvutika ndi kumva chisoni “monganso otsalawo, amene alibe chiyembekezo.” (1 Atesalonika 4:13) Mmalomwake, tingapeze chitonthozo chakuti tinachita bwino koposa moyenerera monga momwe tikanathera kwa wodwala wathu wokondedwa ndi kuti chithandizo chirichonse chazamankhwala chimene tinagwiritsira ntchito chinali kwenikweni chithandizo chakanthaŵi. Komabe, tiri ndi lonjezo losangalatsa la Uyo amene adzatimasula m’mavuto onse oterowo pamene ‘mdani wotsiriza, imfa, adzathedwa.’—1 Akorinto 15:26.
Inde, potsirizira pake chithandizo chabwino koposa cha omafawo chidzachokera kwa Mulungu amene anapereka moyo kwa anthu oyamba ndi amene amalonjeza chiukiriro cha okhulupirira mwa iye ndi Mwana wake, Yesu Kristu.—Yohane 3:16; 5:28, 29.
-