-
Kalata Yochokera ku Bungwe LolamuliraGulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
-
-
Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira
Okondedwa Ofalitsa Anzathu a Uthenga Wabwino:
Ndi mwayi waukulu kwambiri kukhala m’gulu la anthu amene akulambira Mulungu woona Yehova. Ndife “antchito anzake,” ndipo watipatsa ntchito yapadera yopulumutsa miyoyo, yomwe ndi yolalikira ndi kuphunzitsa uthenga wabwino wa Ufumu. (1 Akor. 3:9; Mat. 28:19, 20) Kuti tikwanitse kugwira bwino ntchito yomwe ikuchitika padziko lonse imeneyi mwamtendere komanso mogwirizana, tiyenera kuchita zinthu mwadongosolo.—1 Akor. 14:40.
Bukuli likuthandizani kudziwa mmene mpingo wachikhristu ukugwirira ntchito masiku ano. Likuthandizaninso kudziwa udindo umene muli nawo monga wa Mboni za Yehova. Mukamayamikira mwayi umene muli nawo komanso kukwaniritsa udindo wanu, mudzakhala ‘olimba m’chikhulupiriro.’—Mac. 16:4, 5; Agal. 6:5.
Choncho tikukulimbikitsani kuti muphunzire bukuli mosamala kwambiri. Muziona mmene mungagwiritsire ntchito zimene mukuphunzirazo pa moyo wanu. Mwachitsanzo, ngati mwangovomerezedwa kumene kukhala wofalitsa wosabatizidwa, kodi muyenera kuchita chiyani kuti mubatizidwe n’kukhala wa Mboni za Yehova? Ngati ndinu wobatizidwa, kodi mungatani kuti mupitirize kupita patsogolo mwauzimu komanso kuwonjezera utumiki wanu? (1 Tim. 4:15) Kodi mungathandize bwanji kuti mumpingo mukhale mtendere? (2 Akor. 13:11) Mayankho a mafunso amenewa akupezeka m’bukuli.
Ngati ndinu m’bale wobatizidwa, kodi mungatani kuti muyenerere kukhala mtumiki wothandiza kenako n’kudzakhala mkulu? Popeza anthu ambiri akubwera m’gulu la Mulungu, pakufunika abale ambiri oyenerera kuti azitsogolera m’mipingo. Bukuli likuthandizani kuona zimene mungachite kuti mukwanitse kukhala ndi zolinga zauzimu zimenezi.—1 Tim. 3:1.
Tikukhulupirira ndi mtima wonse kuti bukuli likuthandizani kuyamikira mwayi umene muli nawo wokhala m’gulu la Yehova. Timakukondani kwambiri ndipo timakupemphererani kuti mukhale pakati pa anthu amene adzasangalale polambira Atate wathu wakumwamba Yehova mpaka kalekale.—Sal. 37:10, 11; Yes. 65:21-25.
Ndife abale anu,
Bungwe Lolamulira la Mboni za Yehova
-
-
Gulu Lochita Chifuniro cha YehovaGulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
-
-
MUTU 1
Gulu Lochita Chifuniro cha Yehova
PADZIKO lonse, pali magulu ambiri achipembedzo, andale, amalonda ndi enanso ambiri. Magulu amenewa ali ndi zolinga zosiyanasiyana komanso amatsatira mfundo zosiyanasiyana. Koma pali gulu limodzi lomwe limasiyana kwambiri ndi magulu onsewa. Mawu a Mulungu amasonyeza kuti gulu limeneli ndi la Mboni za Yehova.
2 N’zosangalatsa kuti inuyo muli m’gulu limeneli. Mutadziwa chifuniro cha Mulungu, munayamba kuchichita. (Sal. 143:10; Aroma 12:2) Panopa mumatumikira Mulungu mwakhama limodzi ndi gulu la abale achikondi omwe akupezeka padziko lonse lapansi. (2 Akor. 6:4; 1 Pet. 2:17; 5:9) Mogwirizana ndi zimene Mawu a Mulungu analonjeza, kuchita zimenezi kumakubweretserani madalitso ambiri komanso kumakuthandizani kukhala wosangalala. (Miy. 10:22; Maliko 10:30) Mukamachita chifuniro cha Yehova mokhulupirika, mumakhalanso mukukonzekera madalitso abwino kwambiri komanso osatha a m’tsogolo.—1 Tim. 6:18, 19; 1 Yoh. 2:17.
3 Mlengi wathu wamkulu ali ndi gulu lapadziko lonse lomwe ndi losiyana kwambiri ndi magulu ena onse. Gulu limeneli limalamuliridwa ndi Yehova, yemwe ndi Mutu wa zonse. Iye ndi Woweruza wathu, Wotipatsa Malamulo komanso Mfumu yathu ndipo timamudalira kwambiri. (Yes. 33:22) Popeza kuti Mulungu amafuna kuti zinthu zonse zizichitika mwadongosolo, wakonza njira yotithandiza kuti ‘tizigwira naye ntchito limodzi’ pokwaniritsa cholinga chake.—2 Akor. 6:1, 2.
4 Pamene mapeto a dziko loipali akuyandikira kwambiri, ifeyo tikupitirizabe kupita patsogolo motsogoleredwa ndi Mfumu yathu, Khristu Yesu. (Yes. 55:4; Chiv. 6:2; 11:15) Ndipotu Yesu ananeneratu kuti otsatira ake adzachita zinthu zambiri kuposa zimene iyeyo anachita ali padziko lapansi. (Yoh. 14:12) Zimenezi zinali zoti zidzathekadi chifukwa otsatira ake anali oti adzakhalapo ambiri komanso adzagwira ntchito yolalikira kwa zaka zambiri moti adzakwanitsa kulalikira m’madera ambiri. Adzalengeza uthenga wabwino wa Ufumu mpaka kumalekezero a dziko lapansi.—Mat. 24:14; 28:19, 20; Mac. 1:8.
5 Pali umboni wosonyeza kuti zimenezi zikuchitikadi panopa. Komabe, mmene Yesu anafotokozera, ntchito yolalikira uthenga wabwino idzatha pa nthawi imene Yehova anaika. Zinthu zimene zikuchitika zikusonyeza kuti tsiku lalikulu la Yehova lochititsa mantha limene linatchulidwa m’Mawu a Mulungu layandikira.—Yow. 2:31; Zef. 1:14-18; 2:2, 3; 1 Pet. 4:7.
Tiyenera kuchita khama kuti tizichita zimene Mulungu amafuna. Kuti tichite zimenezi, tifunika kudziwa bwino mmene gulu la Mulungu limachitira zinthu
6 Pamene tikudziwa zambiri zokhudza chifuniro cha Yehova, tiyenera kuyesetsa kuchita zimene Mulungu amafuna. Kuti zimenezi zitheke, tifunika kudziwa bwino mmene gulu la Yehova limayendera ndi kuchita zinthu mogwirizana ndi gululo. Gulu la Yehova limatsatira mfundo za m’Malemba, komanso malamulo ndi ziphunzitso zopezeka m’Mawu a Mulungu.—Sal. 19:7-9.
7 Anthu a Yehova akamatsatira malangizo a m’Baibulo, amakhala mwamtendere komanso amagwira ntchito mogwirizana. (Sal. 133:1; Yes. 60:17; Aroma 14:19) Chikondi n’chimene chimathandiza abale padziko lonse kukhala ogwirizana. Monga Akhristu, timayesetsa kukonda anzathu. (Yoh. 13:34, 35; Akol. 3:14) Zimenezi zimasangalatsa
-