Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Nyengo ya Chikumbutso ndi Nthawi Yochita Zambiri
    Utumiki wa Ufumu—2005 | February
    • [Tchati patsamba 5]

      Zitsanzo za Ndandanda Yochitira Upainiya Wothandiza Njira Zopangira Ndandanda ya Maola 12 a mu Utumiki wa Kumunda Mlungu Uliwonse

      M’mawa​—Lolemba Mpaka Loweruka

      Lamlungu lingalowe m’malo mwa tsiku lina lililonse.

      Tsiku Nthawi Maola

      Lolemba M’mawa 2

      Lachiwiri M’mawa 2

      Lachitatu M’mawa 2

      Lachinayi M’mawa 2

      Lachisanu M’mawa 2

      Loweruka M’mawa 2

      Onse Pamodzi: 12

      Masiku Awiri Athunthu

      Mukhoza kusankha masiku ena alionse awiri pa mlungu (Mogwirizana ndi masiku amene mungasankhe, ndandanda imeneyi ingakupatseni maola 48 okha pa mwezi.)

      Tsiku Nthawi Maola

      Lachitatu Tsiku Lonse 6

      Loweruka Tsiku Lonse 6

      Onse Pamodzi: 12

      Madzulo Awiri ndi Loweruka ndi Lamlungu

      Mukhoza kusankha madzulo alionse awiri a m’kati mwa mlungu.

      Tsiku Nthawi Maola

      Lolemba Madzulo 1 1⁄2

      Lachitatu Madzulo 1 1⁄2

      Loweruka Tsiku Lonse 6

      Lamlungu M’mawa Kapena Masana Okha 3

      Onse Pamodzi: 12

      Masana Atatu ndi Loweruka

      Lamlungu lingalowe m’malo mwa tsiku lina lililonse.

      Tsiku Nthawi Maola

      Lolemba Masana 2

      Lachitatu Masana 2

      Lachisanu Masana 2

      Loweruka Tsiku Lonse 6

      Onse Pamodzi: 12

      Ndandanda Yanga ya mu Utumiki

      Sankhani chiwerengero cha maola a tsiku lililonse.

      Tsiku Nthawi Maola

      Lolemba

      Lachiwiri

      Lachitatu

      Lachinayi

      Lachisanu

      Loweruka

      Lamlungu

      Onse Pamodzi: 12

  • Zofunika Kukumbukira pa Chikumbutso
    Utumiki wa Ufumu—2005 | February
    • Zofunika Kukumbukira pa Chikumbutso

      Chikumbutso cha chaka chino chidzachitika Lachinayi, pa March 24. Akulu asamalire zinthu izi:

      ◼ Pokonza nthawi ya mwambowu, onetsetsani kuti musapereke zizindikiro dzuwa lisanalowe.

      ◼ Aliyense, ngakhale wokamba nkhani, auzidwe nthawi yeniyeni ndi kumene kudzachitikire mwambowu.

      ◼ Mupezeretu mkate ndi vinyo woyenera.—Onani Nsanja ya Olonda ya February 15, 2003, tsamba 14 ndi 15.

      ◼ Mbale, matambula, thebulo labwino ndi nsalu za pathebulo ziyenera kubwera ku holo ndi kuziikiratu m’malo ake nthawi yabwino.

      ◼ Nyumba ya Ufumu kapena malo ena alionse ochitirapo mwambowu ayeretsedweretu bwinobwino.

      ◼ Muyenera kusankhiratu akalinde ndi operekera zizindikiro ndipo muwauziretu ntchito yawo ndi mmene adzayendetsere zinthu, ndiponso kuti afunika adzavale zovala zopatsa ulemu ndiponso kudzikonza bwino.

      ◼ Konzani zokapereka zizindikirozo kwa wodzozedwa aliyense amene akudwala ndipo satha kupezekapo.

      ◼ Ngati mipingo ingapo idzagwiritsa ntchito Nyumba ya Ufumu imodzi, mipingoyo iyenera kugwirizana bwino, kuti anthu asadzapanikizane pakhonde, pakhomo, m’tinjira, ndi koimika magalimoto.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena