Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Sitinalole Kusiya Zimene Timakhulupirira
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
    • INDONESIA

      Sitinalole Kusiya Zimene Timakhulupirira

      Daniel Lokollo

      • CHAKA CHOBADWA 1965

      • CHAKA CHOBATIZIDWA 1986

      • MBIRI YAKE Mpainiya wapadera amene anakhalabe wokhulupirika pa nthawi imene ankazunzidwa.

      Daniel Lokollo

      PA 14 April, 1989, akuluakulu a boma anandimanga pamodzi ndi anthu ena atatu. Pa nthawiyi ndinkachititsa msonkhano wa mpingo m’tauni ya Maumere pachilumba cha Flores.

      Oyang’anira ndende ya m’derali anatikakamiza kuti tizichitira sailuti mbendera. Titakana, anatimenya n’kutikhazika panja kwa masiku 5, dzuwa likutentha kwambiri. Ndipo usiku, tinkazizidwa kwambiri chifukwa tinkagona pasimenti mundende zomwe zinali zazing’ono kwambiri komanso zauve. Nthawi zonse tinkakhala otopa komanso tinkamva kupweteka kwambiri chifukwa cha mabala. Woyang’anira ndendeyi ankatikakamiza kuti tingosiya zimene timakhulupirira koma tinamuuza kuti: “Tilolera kufa koma singachitire sailuti mbendera.” Ifenso tinaona kuti ndi mwayi wathu ‘kuvutika chifukwa cha chilungamo’ mofanana ndi Akhristu akale.—1 Pet. 3:14.

  • Tinapulumuka Chifukwa Chotsatira Malangizo
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
    • INDONESIA

      Tinapulumuka Chifukwa Chotsatira Malangizo

      Blasius da Gomes

      • CHAKA CHOBADWA 1963

      • CHAKA CHOBATIZIDWA 1995

      • MBIRI YAKE Mkulu amene anasamalira nkhosa mwachikondi, pa nthawi imene panali mavuto a zachipembedzo mumzinda wa Ambon, womwe ndi mbali ya zilumba za Maluku.

      M’bale Blasius da Gomes

      PA 19 January 1999, Asilamu ndi Akhristu anayamba kumenyana koopsa chifukwa ankadana kwambiri. Maguluwa ankamenyana pa mtunda wa makilomita atatu kuchokera kumene ndinkakhala.a

      Nditatsimikizira kuti banja langa ndi lotetezeka, ndinaimbira foni ofalitsa ena kuti ndidziwe mmene alili. Ndinawalimbikitsa kuti asachite mantha komanso kuti ayesetse kupewa kupita kumalo amene kunkachitika zachipolowezi. Kenako akulu anakalimbikitsa abale ndi alongo powauza mfundo za m’Malemba komanso anawalimbikitsa kuti azisonkhana m’timagulu.

      A ku ofesi ya nthambi anatilimbikitsa kuti tiuze abale ndi alongo amene ankakhala m’madera omwe anthu ankamenyana kwambiri, kuti asamukeko. Tinauza mabanja angapo malangizo amenewa, koma m’bale wina amene sanamvere anaphedwa ndi gulu la anthu olusa. Aliyense amene anamvera malangizo ochokera ku ofesi ya nthambi anapulumuka.

      a Kumenyanaku kunkachitika m’madera onse a ku Maluku ndipo kunatenga pafupifupi zaka ziwiri. Zipolowezi zinachititsa kuti anthu ambiri athawe m’nyumba zawo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena